< Ngeche 16 >

1 Chuny dhano chano gik modwaro timo, to dwoko margi aa kuom Jehova Nyasaye.
Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
2 Yore duto mag dhano nenorene ni longʼo, to Jehova Nyasaye ema ongʼeyo mopondo mag chuny.
Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
3 Ket gimoro amora mitimo e lwet Jehova Nyasaye, to chenrogi biro dhi maber.
Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
4 Gik moko duto ma Jehova Nyasaye timo oseketo gikogi, kendo giko mar joricho en tho.
Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
5 Jehova Nyasaye odagi ji duto man-gi sunga e chunygi. Ngʼe ma malongʼo: Ok ginitony ni kum.
Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
6 Nikech hera kod adiera ema omiyo richo otimne misango, kuom luoro Jehova Nyasaye miyo ngʼato kwedo richo.
Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
7 Ka yore ngʼato moro Jehova Nyasaye, to omiyo kata wasike dak kode gi kwe.
Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
8 Ber bedo gi matin kod tim makare, moloyo mangʼeny kod tim ma ok kare.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
9 E chuny dhano ochano yore, to Jehova Nyasaye ema telone ondamo mage.
Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
10 Ruoth wuoyo kaka chik mar Nyasaye dwaro, to dhoge ok onego ndhog bura makare.
Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
11 Rapim mopogore opogore makare aa kuom Jehova Nyasaye, to gik mipimogo manie mifuke gin meke moloso.
Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
12 Ruodhi mon gi timbe maricho, nikech kom mar loch obedo mana kuom tim makare.
Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
13 Ruodhi ohero joma wacho adiera kendo gigeno ngʼat mawacho adiera.
Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
14 Mirimb ruoth en jaote mar tho, to ngʼat mariek biro hoye.
Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
15 Ka wangʼ ruoth nenore mamor to nitiere ngima, ngʼwonone chalo gi rumbi mag koth e ndalo chwiri.
Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
16 To ber maromo nade yudo rieko moloyo dhahabu, yiero ngʼeyo tiend wach moloyo fedha!
Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
17 Yor ngʼat moriere tir kwedore gi richo; ngʼat manono yorene orito ngimane!
Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
18 Sunga kelo masira, chuny mar ngʼayi kelo chwanyruok.
Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
19 Ber bedo gi chuny mobolore e dier jochan, moloyo pogo gik moyaki gi josunga.
Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
20 Ngʼato angʼata mawinjo puonj dhi maber, to ojahawi ngʼatno moketo genone kuom Jehova Nyasaye.
Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
21 Ngʼat man-gi paro en ngʼat mariek, kendo weche mowacho gin mana puonj.
A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
22 Winjo wach en soko mar ngima ne jogo man kode, to fuwo kelo kum ne joma ofuwo.
Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
23 Ngʼat mariek rito weche mawuok e dhoge, kendo wechene mowinjore kelo puonj makare.
Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
24 Weche mag mor chalo gi mor kich gimit ne chuny kendo gikelo ngima ni choke.
Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
25 Nitie yo manenore ne dhano ni nikare, to gikone otero mana ngʼato e tho.
Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
26 Miluma ma jatich nigo miyo otiyo matek, kendo kech makaye miyo omedo tiyo matek.
Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
27 Ngʼat marach chano timo timbe maricho, to wechene chalo mach mager.
Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
28 Ngʼat ma timbene richo kelo mana miero, to jakwoth pogo osiepe moherore.
Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
29 Ngʼat ma ja-mahundu wuondo jabute mi otere e yorno ma ok ber.
Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
30 Tangʼ gi ngʼat ma buonjo kodi nikech onyalo bet ni ochano timoni marach, ngʼatno maluwo dhoge ochomo timbe maricho.
Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
31 Lwar en osimbo mar duongʼ to iyude gi ngʼat man-gi ngima makare.
Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
32 Ngʼat ma terore mos ber moloyo jalweny, ngʼat makweyo mirimbe ber moloyo ngʼat mamonjo dala maduongʼ.
Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
33 Igoyo ombulu mondo ongʼe gima ditim, to kuom ngʼado weche duto Jehova Nyasaye ema tieko.
Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.

< Ngeche 16 >