< Ngeche 10 >

1 Ngeche mag Solomon: Wuowi mariek kelo mor ni wuon mare, to wuowi mofuwo miyo min mare chuny lit.
Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
2 Mwandu moyudi e yo marach onge gi ohala; to tim makare reso ji e tho.
Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
3 Jehova Nyasaye ok we ngʼat makare obed gi kech, to oketho gombo mar joricho.
Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
4 Lwedo manyap miyo ngʼato bedo jachan, to lwedo ma jakinda kelo mwandu.
Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
5 Ngʼat makayo cham e kinde oro en wuowi mariek, to ngʼat ma nindo kinde keyo en wuowi makwodo wich.
Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
6 Gweth sidho kondo mar loch ewi ngʼat makare, to timbe mahundu opongʼ e dho ngʼat marach.
Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
7 Paro miparogo ngʼat makare nobed gweth, to nying ngʼat marach nolal.
Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
8 Ngʼat mariek e chunye rwako chike, to ngʼat mofuwo ma wachne ngʼeny dhi e kethruok.
Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
9 Ngʼat mobidhore wuotho kaonge luoro, to ngʼatno maluwo yore mobam ibiro yudo mapiyo.
Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
10 Ngʼat madiemo wangʼe giwuond kelo kuyo, to ngʼat mofuwo ma wachne ngʼeny dhi e kethruok.
Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
11 Dho ngʼat makare en soko mar ngima, to timbe mahundu opongʼo dho ngʼat marach.
Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
12 Sigu kelo miero, to hera umo maricho duto.
Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
13 Rieko iyudo e dho jogo mongʼeyo tiend wach, to luth en mar ngʼe ngʼatno maonge gi rieko mar ngʼado bura.
Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
14 Joma riek okano ngʼeyo, to dho joma ofuwo kelo kethruok.
Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
15 Mwandu mar jomoko e ohinga mochiel motegno ma gigengʼorego, to dhier e kethruok mar jochan.
Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
16 Pok joma kare kelonegi ngima, to mwandu ma joricho yudo kelonegi kum.
Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
17 Ngʼat mawinjo weche mirieyego wuotho e yo madhiyo e ngima, to ngʼat motamore kethone tero ji mamoko e yor lal.
Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
18 Ngʼatno mapando sigu manie chunye, dhoge nigi miriambo, to ngʼatno ma jakwoth ofuwo.
Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
19 Ka weche ngʼeny, to richo ok nyal bare ma ok obetie, to ngʼat marito lewe oriek.
Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
20 Lew ngʼat makare en fedha mowal, to chuny ngʼat marach nigi ohala matin.
Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
21 Dho ngʼat makare konyo ji mangʼeny, to ngʼat mofuwo tho nikech rem mar ngʼeyo ngʼado bura.
Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
22 Gweth mar Jehova Nyasaye kelo mwandu, kendo ok omed chandruok kuome.
Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
23 Ngʼat mofuwo yudo mor e timbe maricho, to ngʼat man-gi winjo bedo mamor kuom rieko.
Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
24 Gima ngʼat marach oluoro biro loye; to gima ngʼat makare dwaro ibiro miye.
Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
25 Ka auka mager ofuto, to joricho otieko; to joma kare chungo motegno nyaka chiengʼ.
Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
26 Mana kaka kong awayo machamo lak kendo ka iro malungo wenge, e kaka jasamuoyo ni jogo moore.
Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
27 Luoro Jehova Nyasaye miyo idak amingʼa, to higni mar ngʼat marach ingʼado bedo machwok.
Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
28 Geno mar joma kare en mor, to geno mar joricho nolal nono.
Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
29 Yor Jehova Nyasaye e kar pondo ni joma kare, to en kethruok ni jogo matimo richo.
Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
30 Joma kare ok nopudh ngangʼ, to joricho ok nodongʼ e piny.
Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
31 Dho joma kare kelo rieko, to lep mar richo nongʼad oko.
Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
32 Lew joma kare ongʼeyo gima owinjore, to dho joricho wacho mana gik mochido.
Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.

< Ngeche 10 >