< Kwan 30 >

1 Musa nowacho ne jotend dhout Israel niya, “Jehova Nyasaye ochiko kama:
Mose anawuza Aisraeli onse zonse zimene Yehova anamulamula. Iye anati, “Zimene Yehova walamula ndi izi:
2 Ka ngʼato osingore ne Jehova Nyasaye kata kokwongʼore mar timo gimoro to kik olokre, to nyaka one ni ochopo singruokneno.
Munthu wamwamuna ngati walonjeza kwa Yehova kapena kulumbira kuti adzachita zimene walumbirazo, asaphwanye mawuwo koma ayenera kuchita chilichonse chimene wanena.
3 “Ka nyako ma rawera ma pod odak e od wuon mare osingore ne Jehova Nyasaye kata okwongʼore mar timo gimoro
“Pamene munthu wamkazi amene akukhalabe mʼnyumba ya abambo ake alumbira kwa Yehova kuti adzachita zimene walonjeza pa ubwana wake,
4 mi wuon mare owinjo singruokneno to ok owacho gimoro, to kwongʼruokneno nyaka siki.
abambo ake namva kulumbira kwakeko kapena kulonjeza kwake kuti adzachitadi, ndipo abambo akewo wosayankhula kanthu, mkaziyo achitedi zomwe analumbirazo. Ayenera kudzachita zonse zimene walonjeza zija.
5 To ka wuon mare okwero e kinde mosingoreno, to onge kwongʼruok kata singruok mare ma osingorego manitimre; Jehova Nyasaye noweye thuolo nikech wuon mare osedagi.
Koma ngati abambo akewo amva kulumbira kwake ndi kumukaniza, palibe lamulo lomukakamiza mkaziyo kuchita zimene walonjeza. Yehova adzamukhululukira chifukwa abambo ake anamukaniza.
6 “Ka onywome bangʼ ka osekwongʼore kata orikni ochiwo singruok motweye
“Ngati akwatiwa atalumbira kale kapena ngati alonjeza mofulumira ndi pakamwa pake,
7 mi chwore owinje to olingʼ alingʼa, to kwongʼruokneno nobed kamano.
mwamuna wake ndi kumva kulumbira kwakeko koma wosanenapo kanthu, mkaziyo achitedi zomwe walumbirazo. Achite ndithu zomwe walonjeza zija.
8 To ka chwore owinjo wachni mokwere, to oketho kwongʼruok motweye kata singruok mane orikni chiwo, kendo Jehova Nyasaye kete thuolo.
Koma ngati mwamuna wake amuletsa atamva kulumbira kwakeko, pamenepo amumasula mayiyo ku zimene analumbira komanso ku zimene analonjeza mosaganiza bwinozo ndipo Yehova adzamukhululukira.
9 “Kwongʼruok kata singruok moro amora ma dhako ma chwore otho kata dhako ma mowere gi chwore otimo nosiki.
“Mayi wamasiye kapena wosiyidwa ukwati akalumbira kapena kulonjeza kuti adzachita kanthu kalikonse, ayenera kukachitadi.
10 “Ka dhako modak gi chwore okwongʼore kata otwere gi kwongʼruok
“Koma ngati mayi wokwatiwa alumbira nalonjeza kuti adzachitadi zimene walonjeza,
11 mi chwore owinjo wachni to ok owachone gimoro kendo ok okwere, to kwongʼruokno nyaka siki.
mwamuna wake ndi kumva kulumbira kwakeko koma osayankhulapo kanthu, osamuletsa, ayenera kuchitadi zonse zimene walumbira ndi zonse zimene walonjeza.
12 To ka chwore odagi kwongʼruokneno, to onge gimoro amora mane chiege owacho manyalo make. Chwore osekethogi, kendo Jehova Nyasaye nokete thuolo.
Koma ngati mwamuna wake amva ndi kumuletsa kuti asachite zomwe walumbirazo, palibe lamulo lomukakamiza mayiyo kuchita zomwe walumbirazo kapenanso zimene walonjeza. Popeza mwamuna wake wamuletsa, Yehova adzamukhululukira mayiyo.
13 Chwor dhako nyalo guro kata ketho singruok kata kwongʼruok ma chiege dwaro sandorego.
Mwamuna wake ali ndi mphamvu zovomereza kapena kukana zimene mayiyo walumbira kapena zimene walonjeza zokhudza kudzilanga yekha.
14 To ka chwore ok owacho gimoro kuom wachno odiechiengʼ ka odiechiengʼ, to nochop kwongʼruok mage kod singruok mage duto motwerego. Kwongʼruokgo nosiki nikech kane owinjogi to nolingʼ.
Ndipo ngati mmawa mwake ndi masiku otsatira mwamuna wake sanenapo kanthu atamva zimenezi, mayiyo achitedi zimene walumbira kapena zimene walonjeza. Mwamunayo wavomereza zimenezo, chifukwa sanamuwuze kanthu mayiyo pa tsiku limene anamva akulonjeza kapena kulumbira.
15 To ka dipo ni olokore bangʼe modagi kosewinjogi, to ketho mar chiege nobed e wiye owuon.”
Koma ngati mwamunayo amukaniza patapita kanthawi atazimva kale, iyeyo ndiye wochimwa mʼmalo mwa mayiyo.”
16 Magi e chike mane Jehova Nyasaye omiyo Musa kaluwore gidak manie kind dichwo gi dhako, kendo e kind wuoro gi nyare ma pod tin modak e odgi.
Awa ndiwo malamulo amene Yehova analamula Mose za mwamuna ndi mkazi wake, ndiponso abambo ndi mwana wawo wamkazi amene akanali mtsikana wokhalabe mʼnyumba ya abambo akewo.

< Kwan 30 >