< Kwan 29 >

1 “‘E odiechiengʼ mokwongo mar dwe mar abiriyo losuru chokruok mowal kendo kik uti tijeu mapile. En odiechiengʼ mugoyoe turumbete.
“‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga.
2 Chiwuru misango miwangʼo pep mar nyarwath achiel, im achiel kod nyiimbe abiriyo moromo higa achiel, ma duto onge songa mondo obed kaka misango madungʼ tik mangʼwe ngʼar mamoro Jehova Nyasaye.
Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova.
3 Rwath ka rwath nyaka chiw gi chiwo mar cham maromo kilo apar mar mogo mayom moru gi mo; im to chiw gi kilo abiriyo;
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri.
4 nyiimbe abiriyogo moro ka moro uchiw gi kilo adek.
Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi.
5 Ewi mago meduru nywok achiel kaka chiwo mar pwodhruok e richo.
Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
6 Magi imedo ewi misango miwangʼo pep mar dwe ka dwe kod mago michiwo pile ka pile kaachiel gi chiwo mar cham kod misango miolo piny mana kaka owinjore. Gin chiwo miwangʼo pep ne Jehova Nyasaye, madungʼ tik mangʼwe ngʼar mamoro Jehova Nyasaye.
Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.
7 “‘E odiechiengʼ mar apar mar dwe mar abiriyo beduru gi chokruok mowal. Nyaka utwe chiemo kulamo kendo kik uti tich moro amora.
“‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito.
8 Kelneuru Jehova Nyasaye chiwo madungʼ tik mangʼwe ngʼar mar misango miwangʼo pep mar nyarwath, im achiel kod nyiimbe abiriyo ma jo-higa achiel, mago maonge songa.
Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema.
9 Rwath ka rwath nyaka chiw gi chiwo mar cham maromo kilo apar mar mogo mayom moruw gi mo; im to uchiw gi kilo abiriyo;
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri;
10 to nyiimbe abiriyo-ka, to uchiw gi kilo adek.
kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo.
11 Ewi mago meduru nywok achiel kaka chiwo mar pwodhruok e richo, kumedo gi chiwo mar pwodhruok e richo kod misango miwangʼo pep mapile pile mikelo gi chiwo mar cham, kod misango miolo piny.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.
12 “‘E odiechiengʼ mar apar gabich e dwe mar abiriyo, losuru chokruok mowal kendo kik uti tijeu mapile. Losneuru Jehova Nyasaye sawo kuom ndalo abiriyo.
“‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri.
13 Kelnauru Jehova Nyasaye chiwo madungʼ tik mangʼwe ngʼar mar misango miwangʼo pep mar rwedhi apar gadek, imbe ariyo kod nyiimbe apar gangʼwen mahikgi achiel, maonge songa.
Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
14 Kuom rwedhi apar gadekgo kelnauru chiwo mar cham maromo kilo apar mar mogo mayom moru gi mo; kuom imbe ariyogo, chiwuru kilo abiriyo ne moro ka moro;
Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri.
15 to kuom nyiimbe apar gangʼwen-ka, to uchiw kilo adek.
Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi.
16 Ewi mago meduru nywok achiel kaka misango mar pwodhruok e richo, kumedo ewi misango miwangʼo pep mapile kod chiwo mar cham gi misango miolo piny.
Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
17 “‘E odiechiengʼ mar ariyo chiwuru nyirwedhi apar gariyo, imbe ariyo kod nyiimbe apar gangʼwen mahikgi achiel, ma duto onge songa.
“‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema.
18 Chiwo mag cham kod misango miolo piny nyaka keti kaka chik dwaro maromre gi rwedhigo, imbego kod nyiimbego.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
19 Ewi mago meduru nywok achiel kaka chiwo mar pwodhruok e richo, kumedo ewi misango miwangʼo pep mapile kod chiwo mar cham, kaachiel gi misango miolo piny.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
20 “‘E odiechiengʼ mar adek chiwuru rwedhi apar gachiel, imbe ariyo kod nyiimbe apar gangʼwen ma jo-higa achiel, ma duto onge songa.
“‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
21 Chiwo mag cham kod misango miolo piny nyaka keti kaka chik dwaro maromre gi rwedhigo, imbego kod nyiimbego.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
22 Ewi mago meduru nywok achiel kaka chiwo mar pwodhruok e richo, kumedo ewi misango miwangʼo pep mapile kaachiel gi misango miolo piny.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
23 “‘E odiechiengʼ mar angʼwen chiwuru rwedhi apar, imbe ariyo kod nyiimbe apar gangʼwen ma jo-higa achiel, ma duto onge songa.
“‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
24 Chiwo mag cham kod misango miolo piny nyaka keti kaka chik dwaro maromre gi rwedhigo, imbego kod nyiimbego.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
25 Ewi mago meduru nywok achiel kaka chiwo mar pwodhruok e richo, kumedo ewi misango miwangʼo pep mapile kaachiel gi chiwo mar cham kaachiel gi misango miolo piny.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
26 “‘E odiechiengʼ mar abich chiwuru rwedhi ochiko, imbe ariyo kod nyiimbe apar gangʼwen ma jo-higa achiel, ma duto onge songa.
“‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
27 Chiwo mag cham kod misango miolo piny nyaka keti kaka chik dwaro maromre gi rwedhigo, imbego kod nyiimbego.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
28 Ewi mago meduru nywok achiel kaka chiwo mar pwodhruok e richo, kumedo ewi misango miwangʼo pep mapile kaachiel gi chiwo mar cham kaachiel gi misango miolo piny.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
29 “‘E odiechiengʼ mar auchiel chiwuru rwedhi aboro, imbe ariyo kod nyiimbe apar gangʼwen ma jo-higa achiel, ma duto onge songa.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
30 Chiwo mag cham kod misango miolo piny nyaka keti kaka chik dwaro maromre gi rwedhigo, imbego kod nyiimbego.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
31 Ewi mago meduru nywok achiel kaka chiwo mar pwodhruok e richo, kumedo ewi misango miwangʼo pep mapile kaachiel gi chiwo mar cham kaachiel gi misango miolo piny.
Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
32 “‘E odiechiengʼ mar abiriyo chiw rwedhi abiriyo, imbe ariyo kod nyiimbe apar gangʼwen ma jo-higa achiel, ma duto onge songa.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
33 Chiwo mag cham kod misango miolo piny nyaka keti kaka chik dwaro maromre gi rwedhigo, imbego kod nyiimbego.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
34 Ewi mago meduru nywok achiel kaka chiwo mar pwodhruok e richo, kumedo ewi misango miwangʼo pep mapile kaachiel gi chiwo mar cham kaachiel gi misango miolo piny.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
35 “‘E odiechiengʼ mar aboro chok oganda kanyakla kendo kik uti tije mapile.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
36 Kelneuru Jehova Nyasaye chiwo madungʼ tik mangʼwe ngʼar mar misango miwangʼo pep mar rwath achiel, im achiel kod nyiimbe abiriyo ma jo-higa achiel, ma duto onge songa.
Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
37 Chiwo mag cham kod misango miolo piny nyaka keti kaka chik dwaro maromre gi rwadhno, imno kod nyiimbego.
Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
38 Ewi mago meduru nywok achiel kaka chiwo mar pwodhruok e richo, kumedo ewi misango miwangʼo pep mapile mar cham kaachiel gi misango miolo piny.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
39 “‘Kuom chiwo mar kwongʼruok kod chiwo mar hera, losneuru Jehova Nyasaye sewni moyier kaka: misango miwangʼo pep, chiwo mag cham, misango miolo piny kod chiwo mag lalruok.’”
“‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’”
40 Musa nonyiso jo-Israel gigo duto mane Jehova Nyasaye ochike.
Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.

< Kwan 29 >