< Nehemia 1 >

1 Magi e weche Nehemia wuod Hakalia: E dwe mar Kislev e higa mar piero ariyo, kane pod antiere kama ochiel gi ohinga motegno mar Susa,
Awa ndi mawu a Nehemiya mwana wa Hakaliya: Pa mwezi wa Kisilevi, chaka cha makumi awiri, pamene ndinali mu mzinda wa Susa,
2 Hanani, ma en achiel kuom owetena, nobiro koa Juda kaachiel gi joma moko, kendo ne apenjogi kuom jo-Yahudi mane otony, bende ne apenjogi kuom Jerusalem.
Hanani mmodzi mwa abale anga, anabwera ndi anthu ena kuchokera ku Yuda, ndipo ine ndinawafunsa za Ayuda otsala amene sanatengedwe ukapolo, ndiponso za mzinda wa Yerusalemu.
3 Ne giwachona niya, “Jogo mane otony oa e twech kendo modwogo e gwengʼni nigi chandruok malich to gi wichkuot. Ohinga mar Jerusalem osemukore kendo dhorangeyege osewangʼ gi mach.”
Anandiyankha kuti, “Amene sanatengedwe ukapolo aja ali pa mavuto aakulu ndipo ali ndi manyazi. Khoma la Yerusalemu ndilogamukagamuka ndipo zipata zake zinatenthedwa ndi moto.”
4 Kane awinjo wechegi, to ne abet piny mi aywak. Kuom ndalo manok nakuyo kendo natweyo chiemo kalamo e nyim Nyasach polo.
Nditamva zimenezi, ndinakhala pansi ndi kuyamba kulira. Ndinalira kwa masiku angapo. Ndinkasala zakudya ndi kumapemphera pamaso pa Mulungu Wakumwamba.
5 Bangʼe ne alemo kama: “Jehova Nyasaye, ma Nyasach Polo, in Nyasaye maduongʼ kendo malich miwuoro, marito singruok mare mar hera gi jogo mohere kendo morito chikene.
Ndinkati: “Inu Yehova, Mulungu wakumwamba, Mulungu wamkulu ndi woopsa. Mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu.
6 Yie ichik iti kendo iyaw wangʼi mondo iwinj lemo ma jatichni lamo odiechiengʼ gotieno ne jotichni, ma gin jo-Israel. Ahulo richowa ma wan jo-Israel, kaachiel gi an kod od wuora wasetimoni;
Tcherani khutu lanu ndi kutsekula maso anu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune limene ndikupemphera usana ndi usiku pamaso panu kupempherera Aisraeli, atumiki anu. Ndikuvomereza machimo a Aisraeli amene tinakuchimwirani. Ndithu, ine ndi banja la makolo anga tinakuchimwirani.
7 waseketho e nyimi adier kendo ok waseluoro chike kod puonj mane imiyo jatichni Musa.
Ife tinakuchitirani zoyipa zambiri. Sitinamvere mawu anu, malamulo ndi malangizo anu amene munapereka kwa mtumiki wanu Mose.
8 “Parie puonj mane imiyo jatichni Musa, kiwacho ni, ‘Ka ok ubedo jo-ratiro, to abiro keyou e dier ogendini,
“Kumbukirani mawu amene munawuza mtumiki wanu Mose akuti, ‘Ngati mukhala osakhulupirika, ndidzakubalalitsani pakati pa mitundu ina.
9 to ka udwogo ira kendo urito chikena, to kata obedo ni jou oke e tungʼ piny ka tungʼ piny, abiro chokogi ka agologi kuondego mi akelgi kama aseyiero kaka kar dak mar Nyinga.’
Koma mukabwerera kwa Ine, mukamvera malamulo anga ndi kuwatsatadi, ndiye kuti ngakhale anthu anu atabalalika kutali chotani, Ine ndidzawasonkhanitsa kuchokera kumeneko ndi kubwera nawo ku malo amene ndinasankha kuti azidzayitanira dzina langa.’
10 “Gin jotichgi kendo jogi, mane ireso gi tekoni maduongʼ kod badi maratego.
“Iwo ndi atumiki anu ndi anthu anu, amene munawawombola ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu.
11 Yaye, Ruoth Nyasaye, mad ichik iti ne lamo mar jatichnini kendo bende ni lamo mag jotichni man-gi ilo mar miyo nyingi luor. Mi jatichni odhi maber ka inyise ngʼwono e nyim ngʼatni.” Ne an jatingʼ divai mar ruoth.
Inu Ambuye tcherani khutu lanu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune ndiponso pemphero la atumiki anu amene amakondwera kuchitira ulemu dzina lanu. Lolani kuti mtumiki wanune zinthu zindiyendere bwino lero ndi kuti mfumu indichitire chifundo.” Nthawi imeneyi nʼkuti ndili woperekera zakumwa kwa mfumu.

< Nehemia 1 >