< Mika 6 >

1 Winj gima Jehova Nyasaye wacho: “Chungʼ malo, ket kwayoni e nyim gode; thuche mondo owinj wach ma in-go.
Tamverani zimene Yehova akunena: “Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri; zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.
2 “Un gode, winjuru wach ma Jehova Nyasaye nigo kodu, chikuru itu un mise mochwere mag piny. Nikech Jehova Nyasaye nigi wach kod joge; en gi bura gi jo-Israel.
Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri; tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi. Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake; Iye akutsutsa Aisraeli.
3 “Un joga en angʼo ma asetimonu? Asemiyou tingʼ mapek e yo mane? Dwokauru ane.
“Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani? Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.
4 Ne agolou e piny Misri kendo agonyou thuolo e piny wasumbini. Ne aoro Musa, mondo otelnu, bende naoro Harun gi Miriam.
Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo. Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni, pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.
5 Un joga parieuru kaka Balak ruodh jo-Moab nongʼado rieko, kendo kaka Balaam wuod Beor nodwoko. Parieuru wuoth mane uago Shitim nyaka Gilgal, mondo mi ungʼe timbe makare mag Jehova Nyasaye.”
Anthu anga, kumbukirani zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha. Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala, kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”
6 En angʼo ma dabigo e nyim Jehova Nyasaye kendo akulrago e nyim Nyasaye moloyo? Dabi e nyime gi misengini miwangʼo pep koso gi nyiroye ma jo-higa achiel?
Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba? Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza, ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?
7 Donge Jehova Nyasaye dibed mamor ka akelone imbe alufe gi alufe, kata ka kelone moo mamol ka aora? Dachiw nyathina makayo eka wena kethona, koso nyodo mar ringra eka wena richona?
Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000, kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta? Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga? Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?
8 Osenyisi gima ber yaye dhano. To angʼo ma Jehova Nyasaye dwaro ni itim? Odwaro ni iti gadiera kendo iher kecho ji kendo iwuoth mobolore e nyim Nyasachi.
Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino. Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe? Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.
9 Winjuru! Luong Jehova Nyasaye ne dala maduongʼ chutho luoro nyingi en rieko. “Yie kum momiyi kaachiel gi ngʼama ochiwe.
Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda ndi nzeru kuopa dzina lanu. “Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.
10 Yaye oganda ma timbegi mono, bende wiya pod diwil awila gi mwandu-u muyudo e yor mecho, kod giu mag pimo mokwongʼ?
Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo, ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?
11 Bende dagony ngʼat man-gi rapim mag mayo ji gi gorogoro modi?
Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo, ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?
12 Joge machwo momewo gin joma ohero lweny. To joge mamoko duto gin jo-miriambo kendo lewgi wacho miriambo.
Anthu ake olemera amachita zachiwawa; anthu ake ndi abodza ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.
13 Kuom mano, asechako tiekou, kendo asechako kethou nikech richou.
Choncho, ndayamba kukuwonongani, kukusakazani chifukwa cha machimo anu.
14 Ubiro chiemo to ok unuyiengʼ; unusik mana ka udenyo. Unukan gik moko to ok ginikonyu, nikech gik mukano nachiwne jowasiku.
Mudzadya, koma simudzakhuta; mudzakhalabe ndi njala. Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika, chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.
15 Unupidh cham to ok unukagi; ubiro biyo zeituni to ok unukonyru gi modhigi un uwegi, bende ubiro biyo mzabibu to ok unumadh divai mag-gi.
Mudzadzala, koma simudzakolola. Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito. Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.
16 Useluwo buche mag Omri kod timbe duto mag jood Ahab, kendo useluwo kitgi gi timbegi. Emomiyo abiro weyou ne kethruok kendo jowu ibiro chaa. Ubiro tingʼo ajara mag ogendini duto.”
Inu mwatsatira malangizo a Omuri ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu, ndi khalidwe lawo lonse. Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu; mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”

< Mika 6 >