< Mika 5 >

1 Chokuru jokedo mau, yaye dala maduongʼ mar jokedo, nikech wasikwa osegonwa agengʼa. Gibiro goyo lemb ruodh jo-Israel gi luth.
Iwe mzinda wa anthu ankhondo, sonkhanitsa anthu ako ankhondo, pakuti anthu atizungulira kuti alimbane nafe. Adzakantha ndi ndodo pa chibwano cha wolamulira wa Israeli.
2 “To in Bethlehem Efratha, kata obedo ni itin e dier dhout Juda, kuomi ema ngʼat manobedna jatend Israel nowuogie, ngʼat machakruok mare noa chon, kinde machon gi lala.”
“Koma iwe Betelehemu Efurata, ngakhale uli wonyozeka pakati pa mafuko a Yuda, mwa iwe mudzatuluka munthu amene adzalamulira Israeli, amene chiyambi chake nʼchakalekale, nʼchamasiku amakedzana.”
3 Kuom mano Israel ibiro jwangʼ nyaka kinde ma dhako man-gi ich nonywolie nyathi, kendo owetene mamoko nodwogi mi riwre gi jo-Israel.
Nʼchifukwa chake Israeli adzasiyidwa mpaka pa nthawi imene mayi amene ali woyembekezera adzachire. Ndipo abale ake onse otsalira adzabwerera kudzakhala pamodzi ndi Aisraeli.
4 Enochungʼ mi okwa rombe gi teko mar Jehova Nyasaye, ka en gi duongʼ mar Jehova Nyasaye ma Nyasache. Joge nodag maonge luoro nikech duongʼne nochop e tunge piny,
Iye adzalimbika, ndipo adzaweta nkhosa zake mwa mphamvu ya Yehova, mu ulemerero wa dzina la Yehova Mulungu wake. Ndipo iwo adzakhala mu mtendere, pakuti ukulu wake udzakhala ponseponse pa dziko lapansi.
5 kendo en owuon ema nobed kwe margi. Ka jo-Asuria omonjo pinywa, kendo ka ginyono kuondewa mochiel motegno, to wabiro yiero jokwath abiriyo mondo oked kodgi; adier jotendwa aboro norad kodgi.
Ndipo Iye adzakhala mtendere wawo. Asiriya akadzalowa mʼdziko lathu ndi kuyamba kuthira nkhondo malo athu otetezedwa, tidzawadzutsira abusa asanu ndi awiri, ngakhalenso atsogoleri asanu ndi atatu.
6 Gibiro loyo piny jo-Asuria gi ligangla, piny jo-Nimrod ibiro loyo gi ligangla mowuodhi. Noresgi e lwet jo-Asuria ka nomonj pinywa, kendo ka nochopi e tongʼwa.
Iwo adzagonjetsa dziko la Asiriya ndi lupanga, dziko la Nimurodi adzalilamulira mwankhondo. Adzatipulumutsa kwa Asiriya akadzafika mʼmalire a mʼdziko lathu kudzatithira nkhondo.
7 Joka Jakobo modongʼ nobed e dier ogendini mangʼeny, mana ka thoo moa kuom Jehova Nyasaye kata ka ngʼidho ma omoko e lum, malal apoya nono ne dhano bende ok nyal rito dhano.
Otsalira a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu yambiri ya anthu ngati mame ochokera kwa Yehova, ngati mvumbi pa udzu, omwe sulamulidwa ndi munthu kapena kudikira lamulo la anthu.
8 Joka Jakobo modongʼ nobed e dier ogendini, ginibed e dier ji mayoreyore, mana ka sibuor e dier le mag bungu, kata ka sibuor matin e dier rombe, makidho kendo nyulo kokadho, maonge ngʼama nyalo resogi.
Otsala a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu ya anthu, mʼgulu la anthu a mitundu yambiri, ngati mkango pakati pa nyama za mʼnkhalango. Ngati mwana wa mkango pakati pa gulu la nkhosa, amene pozidutsa amazidya ndi kuzikhadzula, ndipo palibe angathe kuzilanditsa.
9 Notingʼ lweti malo kiseloyo wasiki, kendo joma kedo kodi duto notieki.
Mudzagonjetsa adani anu, ndipo adani anu onse adzawonongeka.
10 Jehova Nyasaye owacho niya, “E odiechiengno anaketh fareseu kendo nabanj gecheu mag lweny.
Yehova akuti, “Tsiku limenelo ndidzawononga akavalo anu onse ndi kuphwasula magaleta anu.
11 Anaketh mier madongo manie pinyu mochiel motegno kendo anamuk ohingau.
Ndidzawononga mizinda ya mʼdziko mwanu ndi kugwetsa malinga anu onse.
12 Abiro tieko timbeu mag jwok ma ok unuchak ugo gagi kendo.
Ndidzawononga ufiti wanu ndipo sikudzakhalanso anthu owombeza mawula.
13 Abiro ketho kido mopa mau kod kite mulamo manie dieru. Ok unuchak ukulru piny ne gik ma lwetu oloso.
Ndidzawononga mafano anu osema pamodzi ndi miyala yanu yopatulika imene ili pakati panu; simudzagwadiranso zinthu zopanga ndi manja anu.
14 Abiro muko sirni mag nyasachu ma Ashera mi agol kuomu kendo abiro ketho miechu madongo chuth.
Ndidzazula mitengo ya mafano a Asera imene ili pakati panu, ndipo ndidzawononga mizinda yanu.
15 Anachul kuor gi mirima kod gero kuom ogendini ma osedagi luora.”
Ndidzayilanga mwaukali ndi mokwiya mitundu imene sinandimvere Ine.”

< Mika 5 >