< Tim Jo-Lawi 26 >

1 Kik ulos kido moro amora mopa kata chungo siro moro milamo bende kidi moro amora mopa kik yud e pinyu kukulorune kulame. An e Jehova Nyasaye ma Nyasachu.
“‘Musadzipangire mafano ndipo musayimike chifanizo chosema kapena mwala woti mudzipembedza. Musayike mwala wosema mʼdziko mwanu kuti muziwugwadira. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
2 Rituru Sabato maga, kendo luoruru kara maler mar lemo. An e Jehova Nyasaye.
“‘Muzisunga Masabata anga ndipo muzilemekeza malo anga wopatulika. Ine ndine Yehova.
3 Ka urito buchena kendo urito chikena,
“‘Mukamayenda motsata malangizo anga ndi kumvera mosamalitsa malamulo anga,
4 to abiro kelonu koth e kinde mowinjore, kendo pinyu nochieg cham mi yiendeu nonyag olembe.
ndidzakupatsani mvula pa nyengo yake. Nthaka yanu idzabala zokolola zake, ndipo mitengo ya mʼmunda idzabala zipatso zake.
5 Ubiro dino cham nyaka chop kinde muponoe mzabibu kendo ubiro pono mzabibu nyaka chop kinde muchwoyoe bende ubiro bedo gi chiemo moromou kendo ubiro dak gi kwe e pinyu.
Mudzakhala mukupuntha tirigu mpaka nthawi yothyola mphesa, ndipo mudzakhala mukuthyola mphesa mpaka nthawi yodzala. Mudzadya chakudya chanu mpaka kukhuta ndipo mudzakhala mʼdziko lanu mwamtendere.
6 Anamiu kwe e pinyu, mi ununindi maonge ngʼama nomiu luoro. Anatieki ondiegi duto e dieru kendo ligangla ok nomonju kata matin.
“‘Ndidzabweretsa mtendere mʼdziko lanu, ndipo muzidzagona popanda wokuopsezani. Ndidzachotsa nyama zakuthengo zoopsa mʼdziko mwanu, ndipo mʼdzikomo simudzakhala nkhondo.
7 Unuriemb jowasiku duto e dieru kendo ununeg-gi.
Mudzapirikitsa adani anu, ndipo mudzawagonjetsa ndi lupanga pamaso panu.
8 Jou abich nobed gi teko mar riembo ji mia achiel, kendo jou mia achiel nobed gi teko mar riembo ji gana apar, kendo ununeg wasiku.
Anthu asanu mwa inu adzapirikitsa anthu 100, ndipo anthu 100 mwa inu adzathamangitsa anthu 10,000, ndipo adani anuwo mudzawagonjetsa ndi lupanga.
9 Abiro olonu gweth, kendo abiro miyo unywol mi ununyaa mathoth, kendo abiro chopo singruok duto mane atimo kodu.
“‘Ndidzakukumbukirani ndi kukupatsani ana ambiri ndi kukuchulukitsani. Ndidzasunga pangano langa ndi inu.
10 Cham mag higa makadho manie decheu noromu chamo nyaka chop kinde ma ugologie oko mondo uyud thuolo mar rwako cham manyien.
Mudzakhala mukudyabe chakudya chogonera ndipo mudzachotse chakudyacho mʼnkhokwe kuti mupezemo malo woyika chakudya china chatsopano.
11 Abiro loso kar dakna e dieru kendo ok anajwangʼu kata matin.
Ndidzakhala pakati panu, ndipo sindidzayipidwa nanu.
12 Anawuoth e dieru mi nabed Nyasachu, kendo unubed joga.
Ine ndidzayendayenda pakati panu ndipo ndidzakhala Mulungu wanu. Inu mudzakhala anthu anga.
13 An e Jehova Nyasaye ma Nyasachu mane ogolou e piny Misri, mondo kik ubed wasumb jo-Misri kendo ne aturo lodi mane otwenu mi koro sani uwuotho tir.
Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto kuti musakhalenso akapolo a Aigupto. Ndinadula mipiringidzo ya goli lanu ndi kukuthandizani kuti muziyenda momasuka.
14 To ka unutamru winja ma ok urito chikenago duto,
“‘Koma mukadzapanda kundimvera ndi kuphwanya malamulo anga onsewa,
15 ma udagi buchena kendo uchayo chikena, ma ok urito chikena duto ma uketho singruok mara mane atimo kodu,
ndipo ngati mudzanyoza malangizo anga ndi kunyansidwa ndi malamulo anga, ndi kulephera kumvera zonse zimene ndakulamulani, ndi kuswa pangano langa,
16 to koro ngʼeuru chuth ni mae e kaka abiro timonu: Anapou gi masira kod tho marach, gi tuo mayuyo wangʼ gi tuo mamiyo del dhe. Cham ma upidho ok nokonyu kata matin nikech jowasiku ema nochamgi.
Ine ndidzakuchitirani izi: ndidzabweretsa zoopsa zadzidzidzi monga chifuwa chachikulu chowondetsa ndiponso malungo amene adzawononga maso ndi kufowoketsa moyo wanu. Mudzangovutika kudzala mbewu zanu chifukwa adani anu adzazidya.
17 Anabed ka asin kodu mi wasiku nolou e lweny kendo gininegu; unubed e bwo loch jowasiku, kendo unubwogru gi ngʼwech kata kaonge joma lawou.
Ndidzakufulatirani, kotero kuti adani anu adzakugonjetsani. Odana nanu adzakulamulirani ndipo inu muzidzagothawa popanda wokupirikitsani.
18 Kata bangʼ timo magi duto kapod ok unyal winja, to anakumu nyadibiriyo kuom richo duto.
“‘Ngati simudzandimvera mutaona zonsezi, ndidzakulanganinso mochulukitsa kasanu ndi kawiri chifukwa cha kuchimwa kwanu.
19 Anatiek sunga mar wich teko ma un-go, kendo anami polo rieny ka chuma, kendo piny mwalo nodog matek ka mula.
Ndidzathyola mphamvu zanu zimene mukunyadirazo, ndipo ndidzasandutsa mitambo kuti ikhale yowuma ngati chitsulo, ndiponso nthaka yanu kuti ikhale ngati mkuwa.
20 Ubiro ketho tekreu kayiem nono, kuchwoyo cham nimar chambu ok nochiegi, kata yedheu bende ok nonyag olembe.
Mphamvu zanu zidzapita pachabe chifukwa nthaka yanu sidzabala kanthu, ngakhale mitengo yake sidzabala zipatso zake.
21 Kapod usikona mana gi wich teko kendo udagi winja, to anakelnu masiche moloyo nyadibiriyo maromre gi richou.
“‘Ngati mudzapitirira kutsutsana nane ndi kukana kundimvera, ndidzachulukitsa masautso anu kasanu ndi kawiri molingana ndi machimo anu.
22 Abiro oronu le mag bungu mondo oked kodu kendo ginineg nyithindo kaachiel gi jambu mi unudongʼ manok kendo yoreu nodongʼ nono maonge joma wuothoe.
Ndidzabweretsa zirombo zolusa pakati panu, ndipo zidzakulandani ana anu ndi kuwononga ngʼombe zanu. Choncho zidzachepetsa chiwerengero chanu kotero kuti mʼnjira mwanu simudzapita anthu.
23 Kobedo ni pod ok udwogo ira kata bangʼ timonu magi duto, kendo udhi mana nyime gi wich teko,
“‘Mukadzapanda kutembenukira kwa Ine ngakhale nditakulangani motere, ndi kumachitabe zotsutsana ndi Ine,
24 to an bende nanyisu wich teko, mi anamiu kum moloyo nyadibiriyo nikech richou.
Ine mwini ndidzalimbana nanu, ndipo ndidzakulangani mochulukitsa kasanu ndi kawiri chifukwa cha machimo anu.
25 Kendo anakel lweny e dieru mondo achulgo kuor kuom ketho singruok mane atimo kodu, kendo kinde duto manuchokru e miechu to nagou gi tuoche kendo wasiku nomaku.
Ndipo ndidzabweretsa lupanga pa inu ndi kukulangani chifukwa chophwanya pangano langa. Mukadzasonkhana mʼmizinda yanu, ndidzatumiza miliri pakati panu ndipo ndidzakuperekani mʼmanja mwa adani anu.
26 Anami chiembu doko manok kendo mon apar notedi e agulu achiel. Ginipimnu chiemo e rapim, kendo kata kuchiemo to onge ngʼama noyiengʼ.
Ndikadzachepetsa buledi wanu, akazi khumi adzaphika buledi wawo mu uvuni umodzi, ndipo adzakugawirani bulediyo pangʼonopangʼono. Choncho mudzadya koma wosakhuta.
27 Kobedo ni pod ok udwogo ira kata bangʼ timonu magi duto, kendo udhi mana nyime gi wich teko,
“‘Mukadzapanda kundimvera ngakhale nditakulangani motere, ndi kumatsutsanabe ndi Ine,
28 to an bende nasik kodu gi wich teko gi mirimba mager, kendo anakumu moloyo nyadibiriyo gi mirimba mager nikech richou.
pamenepo ndidzalimbana nanu mwaukali, ndipo Ine mwini ndidzakulangani mochulukitsa kasanu ndi kawiri chifukwa cha kuchimwa kwanu.
29 Unucham ring yawuotu kod nyiwu.
Mudzadya ana anu aamuna ndiponso mudzadya ana anu aakazi.
30 Anaketh kuondeu motingʼore gi malo, kendo anamuki kendeu muwangʼoe ubani. Anaket ringreu motho kuom nyiseche manono kendo anajwangʼu chuth.
Ine ndidzawononga malo anu opembedzera mafano a ku mapiri. Ndidzagwetsa maguwa anu ofukizira lubani, ndipo ndidzawunjika pamodzi mitembo ya mafano anu wopanda moyowo, ndipo ndidzanyansidwa nanu.
31 Miechu madongo biro bedo gundni, kuondeu maler mag lemo abiro ketho, kendo ok anayie winjo tik mangʼwe ngʼar mag misengini mau.
Ndidzasandutsa mizinda yanu kukhala mabwinja ndi kuwononga malo anu wopatulika. Sindidzakondweranso ndi fungo lokoma la zopereka zanu.
32 Anaketh pinyu kendo jowasiku mabiro dakie nohum nono.
Ndidzawononga dziko kotero kuti adani anu mʼmenemo adzadabwa.
33 Abiro keyou e kind ogendini, anagol ligangla mi alawu. Pinyu nodongʼ gunda, kendo miechu madongo nokethi chuth.
Ndidzakubalalitsani pakati pa mitundu ina ya anthu ndipo ndidzasolola lupanga langa ndi kukupirikitsani. Dziko lanu lidzawonongedwa, ndipo mizinda yanu idzasanduka mabwinja.
34 E kinde duto ma pinyu nodongʼ gunda, ka un to asekeyou udak e kind wasiku; pinyu nobed ma ok opur mondo ochulgo Sabato maga duto mane ok urito.
Nthawi imeneyo nthaka idzasangalalira kuyipumitsa kwake nthawi yonse imene idzakhala yosalimidwa, pamene inu mudzakhala muli mʼdziko la adani anu. Pa nthawi imeneyo dziko lidzapumula ndi kukondwerera kulipumuza kwake.
35 E kinde duto ma pinyu nodongʼ gunda kamano, enobed ma ok opure, ka oritogo Sabato duto mane ok oyweyoe e kinde mane udak kuno.
Nthawi zonse pamene dzikolo lidzakhala lopanda anthu, nthaka idzapumula. Mpumulo umenewu udzakhala umene nthakayo sinapumulepo pa nthawi zimene inu munkapumula muli mʼdzikomo.
36 To kuom jou modongʼ ka ngima e piny wasikgi, ginto anagogi kod kihondko e piny wasikgi, ma kata ka yamo okwadho it oboke maponi giwinjo, to giniwuog gi ngʼwech. Giniringi mana ka joma wasigu lawo gi ligangla mi gipodh piny kata obedo ni onge ngʼama lawogi.
“‘Kunena za amene adzatsale, ndidzayika mantha mʼmitima mwawo mʼdziko la adani awo kotero kuti adzathawa ngakhale mtswatswa wa tsamba lowuluka ndi mphepo. Adzathawa ngati akuthawa lupanga, ndipo adzagwa pansi ngakhale padzakhale wopanda kuwapirikitsa.
37 Ginituomre kendgi giwegi mana ka joma wasigu lawo gi ligangla, kata obedo ni onge ngʼama lawogi. Omiyo ok unuyud teko mar kedo gi wasiku.
Iwo adzaphunthwitsana ngati akuthawa nkhondo, ngakhale padzakhale popanda wowapirikitsa. Choncho simudzatha kuyima pamaso pa adani anu.
38 Unulal nono e kind ogendini, kendo wasiku notieku.
Mudzatheratu pakati pa mitundu ya anthu. Dziko la adani anu lidzakudyani.
39 Joma otony e dieru mane odongʼ kangima e pinje mag wasiku nobed ka dendgi dhi adhiya nikech richogi kendo nikech richo mag kweregi, mana machal kaka notimore ni kweregi.
Ngakhale iwo amene adzatsale adzatheratu mʼdziko la adani awo chifukwa cha machimo awo ndi machimo a makolo awo.
40 Bangʼ mae gibiro hulo richogi gi richo kweregi mane omiyo giweya kaachiel gi richo mane omiyo gibedo wasika,
“‘Tsono adzawulula machimo awo ndi machimo a makolo awo, kusakhulupirika kwawo ndi mayendedwe awo otsutsana nane,
41 mane omiyo abedo kodgi mamon kendo mane omiyo aterogi e piny wasikgi, eka bangʼe chunygi ma ok oyie kaka adwaro nobolre, mi giniyud kum kuom richogi,
zomwe zinandipangitsa kuwafulatira ndi kuwapereka mʼmanja mwa adani awo. Ndipo mitima yawo yowumayo ikadzadzichepetsa ndi kuvomera kulangidwa chifukwa cha machimo awo,
42 eka abiro paro singruok mane atimo gi Jakobo kendo gi Isaka kendo gi Ibrahim, kendo anapar pinyu.
Ine ndidzakumbukira pangano langa ndi Yakobo, pangano langa ndi Isake, pangano langa ndi Abrahamu. Ndidzakumbukiranso dzikolo.
43 Piny to nodongʼ gunda nikech joma odakie osea, kendo obiro nindo ka ok opure mondo ochulgo Sabato duto mane ok oyweyoe. Giniyud kum kuom richogi nikech ne gichayo chikena kod buchena.
Pakuti adzasiya dziko lawo lopanda anthu, nthaka idzakondwerera zaka zake zoyipumuza pamene iwo kudzakhala kulibe. Koma adzalangidwa chifukwa cha machimo awo popeza anakana malamulo anga ndipo mitima yawo inkayipidwa nawo malangizo anga.
44 “Kata kamano, kata obedo ni gin e piny wasikgi, to ka anawitgi kendo ok anajwangʼ-gi kata tiekogi chuth, mi aketh singruok mane atimo kodgi. An Jehova Nyasaye ma Nyasachgi.
Komabe ngakhale adzachite zonsezi ali mʼdziko la adani awo, Ine sindidzawakana kapena kuyipidwa nawo kwakuti nʼkuwawononga kwathunthu ndi kuthetsa pangano langa ndi iwo. Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
45 Nikech aherogi, omiyo anapar singruok mane atimo gi kweregi, mane agolo e piny Misri mana kane ogendini neno mondo an Jehova Nyasaye abed Nyasachgi.”
Koma powachitira chifundo, ndidzakumbukira pangano langa ndi makolo awo amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto mitundu ina ikuona kuti Ine ndikhale Mulungu wawo. Ine ndine Yehova.’”
46 Magi e buche, chike kod yore mane Jehova Nyasaye omiyo jo-Israel e Got Sinai kokadho kuom Musa.
Amenewa ndi malamulo ndi malangizo amene Yehova anawayika pakati pa Iye mwini ndi Aisraeli pa Phiri la Sinai kudzera mwa Mose.

< Tim Jo-Lawi 26 >