< Tim Jo-Lawi 23 >

1 Jehova Nyasaye nowacho ne Musa niya,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 “Wuo gi jo-Israel kendo inyisgi ni: ‘Magi e sewni moyier mag Jehova Nyasaye, magin chokruok mage maler, ma onego ulandi kuonde duto ma uchokorue.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Awa ndi masiku anga osankhika a chikondwerero, masiku osankhika olemekeza Yehova amene uyenera kulengeza kuti akhale masiku opatulika a misonkhano.
3 “‘Nitie ndalo auchiel munyalo tiyoe tijeu; to chiengʼ mar abiriyo en odiechieng Sabato mar yweyo, ma en odiechiengʼ mowal mar chokruok. Ok oyienu timo gimoro amora, kamoro amora mudakie, nikech en Sabato mar Jehova Nyasaye.
“‘Pa masiku asanu ndi limodzi muzigwira ntchito, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata lopuma, tsiku la msonkhano wopatulika. Kulikonse kumene inu mukukhala musamagwire ntchito iliyonse tsiku limeneli popeza ndi tsiku la Sabata la Yehova.
4 “‘Magi e sewni moyier mag Jehova Nyasaye, ma gin chokruok maler, manyaka ulandi e kindegi mowinjore.
“‘Awa ndiwo masiku osankhidwa a zikondwerero za Yehova, masiku woyera a misonkhano amene muti mudzalengeze pa nthawi yake:
5 Pasaka mar Jehova Nyasaye chakore godhiambo tarik apar gangʼwen mar dwe mokwongo.
Chikondwerero cha Paska chiziyamba madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba.
6 To tarik apar gabich mar dweno en Sap Makati ma ok oketie Thowi mar Jehova Nyasaye kendo nyaka ucham makati motedi ma ok oketie thowi kuom ndalo abiriyo.
Tsiku la 15 la mwezi womwewo ndi tsiku lolemekeza Yehova ndipo muziyamba Chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
7 Chiengʼ mokwongo mar jumano nyaka ubed gi chokruok mowal, kendo kik uti tich moro amora ma utiyo pile.
Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika. Musamagwire ntchito iliyonse.
8 Kuom ndalo abiriyo, chiwuru ne Jehova Nyasaye misengini miwangʼo pep. Chiengʼ mar abiriyo beduru gi chokruok mar jomaler, kendo kik uti tich moro amora ma utiyo pile.’”
Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Ndipo tsiku lachisanu ndi chiwiri muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito yolemetsa.’”
9 Jehova Nyasaye nowacho ne Musa niya,
Yehova anawuza Mose kuti,
10 “Wuo gi jo-Israel kendo inyisgi ni: ‘Ka uchopo e piny ma asesingonu mi ukayo cham, to nyaka ukelne jadolo cham ma ukwongo kayo.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo ndi kukolola za mʼminda mwanu, mudzabwere kwa wansembe ndi mtolo wa tirigu woyambirira kucha wa mʼminda mwanu.
11 E odiechiengʼ mokwongo bangʼ Sabato, jadolo biro fwayo e nyim Jehova Nyasaye cham mukwongo kayo kaka mich moyiedhi, eka Jehova Nyasaye noyie kodu.
Wansembeyo auweyule mtolowo pamaso pa Yehova kotero mtolowo udzalandiridwa mʼmalo mwanu. Wansembe auweyule tsiku lotsatana ndi la Sabata.
12 To chiengʼono muchiewoe cham mifwayo to nyaka uchiwe ne Jehova Nyasaye gi nyaim ma pod hike achiel kendo maonge songa mondo timgo misango miwangʼo pep,
Pa tsiku limene muweyula mtolowo, muperekenso mwana wankhosa wa mwamuna wa chaka chimodzi, wopanda chilema kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
13 kaachiel gi misango mar cham gi mogo mayom madirom kilo abiriyo moruw gi mo. Kendo misangono mondo owangʼe modungʼ tik mangʼwe ngʼar ni Jehova Nyasaye. Misango miolo piny to obed divai maromo lita achiel.
Chopereka chachakudya chake chikhale cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta kuti chikhale nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova, ya fungo lokoma. Ndipo chopereka cha chakumwa chake chikhale vinyo wa malita anayi ndi theka.
14 Kik ucham makati, kata makati mowangʼ kata cham manyien ma pod numu, kapok ochopo chiengʼ ma uchiwone Nyasachu michni. Kendo mae en chik momakou kaachiel gi nyikwau nyaka chiengʼ kamoro amora manudagie.
Musadye buledi aliyense kapena tirigu wokazinga, kapena wamuwisi mpaka tsiku limene mwabwera ndi chopereka ichi kwa Mulungu wanu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
15 “‘Chakre odiechiengʼ moluwo Sabato, mane ukeloe mich mar cham moyiedhi, to nyaka ukwan ma une ni oromo jumbe abiriyo.
“‘Kuyambira tsiku lotsatana ndi la Sabata lija, tsiku limene munabwera ndi mtolo wa nsembe yoweyula, muziwerenga masabata asanu ndi awiri athunthu.
16 Kwanuru ndalo piero abich bangʼ Sabato mar abiriyo, kendo chiengʼno unutim misango ni Jehova Nyasaye gi cham manyien.
Ndiye kuti muwerenge masiku makumi asanu kuchokera pa tsiku lotsatana ndi Sabata la chisanu ndi chiwiri, ndipo kenaka mupereke nsembe ya tirigu watsopano kwa Yehova.
17 Keluru makati ariyo mugolo e miechu kaka misango mifwayo, kendo ulosgi gi mogo mayom moromo kilo abiriyo moketie thowi, mondo uchiwgi ne Jehova Nyasaye kaka chiwo mar cham mokwongo.
Kuchokera kulikonse kumene mukukhala, mubwere pamaso pa Yehova ndi buledi muwiri wa ufa wosalala wa makilogalamu awiri, ophikidwa ndi yisiti kuti akhale nsembe yoweyula ya zakudya zoyamba kucha.
18 Kaachiel gi makatino chiwne Jehova Nyasaye nyirombe abiriyo machwo maonge songa mahikgi en achiel, gi nyarwath matin kod imbe ariyo. Ginibed misango miwangʼo pep ni Jehova Nyasaye kaachiel gi misango mar cham gi misango miolo piny mondo obed misango miwangʼo pep madungʼ tik mangʼwe ngʼar ni Jehova.
Pamodzi ndi bulediyu muperekenso ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, aliyense akhale wa chaka chimodzi ndi wopanda chilema. Pakhalenso ngʼombe yayingʼono yayimuna ndi nkhosa zazimuna ziwiri. Zimenezi zidzakhala nsembe zopsereza zopereka kwa Yehova pamodzi ndi nsembe za zakudya ndi nsembe za zakumwa. Zonsezi zikhale nsembe zopsereza za fungo lokomera Yehova.
19 Bangʼe chiw nywok achiel mitimogo misango mar golo richo, kaachiel gi nyiimbe ariyo ma jo-higa achiel mitimogo misango mar lalruok.
Kenaka mupereke mbuzi imodzi yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ndiponso ana ankhosa awiri, aliyense wa chaka chimodzi kuti akhale nsembe yachiyanjano.
20 Jadolo nyaka chiw nyiimbe ariyogo e nyim Jehova Nyasaye kaka misango mifwayo, kaachiel gi makati mag cham mokwongo. Magi nobed mich mowal michiwo e nyim Jehova Nyasaye, kendo ginidongʼ ni jadolo.
Wansembe aweyule ana ankhosa awiriwo pamaso pa Yehova monga nsembe yoweyula, pamodzi ndi buledi wa tirigu woyambirira kucha. Zimenezi ndi zopereka zopatulika za Yehova zopatsidwa kwa ansembe.
21 To odiechiengʼno unugo tungʼ kulando chokruok maler, kendo kik uti tijeu mapile. Maeni en chik momakou kaachiel gi nyikwau kamoro amora manudagie.
Pa tsiku lomwelo mulengeze za msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
22 “‘Ka ukeyo e puotheu, to kik uka nyaka cham manie giko puodho, kata kik uhul cham modongʼ, mago weuru ni joma odhier kod jodak. An e Jehova Nyasaye ma Nyasachu.’”
“‘Pamene mukukolola zinthu mʼmunda mwanu, musakolole munda wanu mpaka mʼmalire mwenimweni, ndipo musatole khunkha lake. Zimenezo musiyire anthu osauka ndi alendo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
23 Jehova Nyasaye nowacho ne Musa niya,
Yehova anawuza Mose kuti,
24 “Wach ni jo-Israel ni: ‘E odiechiengʼ mokwongo mar dwe mar abiriyo, nyaka ubed gi odiechieng yweyo; ma en odiechieng chokruok mowal kaka rapar kugoyo turumbete.
“Uza Aisraeli kuti, ‘Tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, likhale tsiku lopumula, la msonkhano wopatulika, mulilengeze poyimba lipenga.
25 Chiengʼni kik utim tijeu mapile, to chiwuru misango miwangʼo pep ni Jehova Nyasaye.’”
Musagwire ntchito zolemetsa koma mupereke nsembe yopsereza kwa Yehova.’”
26 Jehova Nyasaye nowacho ne Musa niya,
Yehova anawuza Mose kuti,
27 “E odiechiengʼ mar apar mar dwe mar abiriyo nobednu Chiengʼ Pwodhruok. Beduru gi chokruok maler ka uriyo kech, kendo uchiw ni Jehova Nyasaye misango miwangʼo pep.
“Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri ndi tsiku lochita Mwambo Wopepesera Machimo. Muzichita msonkhano wopatulika. Muzidzichepetsa pamaso pa Yehova ndi kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova.
28 Odiechiengʼno kik ngʼato kuomu mul tich moro amora nikech en Chiengʼ Pwodhruok, migolonue richo e nyim Jehova Nyasaye ma Nyasachu.
Tsiku limeneli musamagwire ntchito chifukwa ndi tsiku la Mwambo Wopepesera Machimo, kupepesera machimo anu pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
29 Ngʼato angʼata ma ok nyal riyo kech odiechiengʼno to nongʼad kare oko chuth e kind ogandane.
Munthu aliyense amene sasala zakudya pa tsiku limeneli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
30 Kendo anatiek ngʼato angʼata momulo tich moro amora chiengʼno, kendo anagole e kind ogandane.
Aliyense wogwira ntchito tsiku limeneli ndidzamuwononga pakati pa anthu a mtundu wake.
31 Kik umul tich moro amora. Ma en chik ma omakou nyaka nyikwau duto kamoro amora ma unudagie.
Inu musadzagwire ntchito iliyonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
32 Chiengʼno nobednu Sabato mar yweyo, kendo nyaka une ni uriyo kech. Chakre odhiambo mar odiechiengʼ mar ochiko mar dwe nyaka kinyne godhiambo, nyaka urit Sabato maru.”
Limeneli kwa inu ndi tsiku la Sabata lopumula, ndipo muyenera kusala zakudya. Kuyambira madzulo a tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi mpaka madzulo ena otsatirawo muzisunga tsikulo ngati Sabata lanu.”
33 Jehova Nyasaye nowacho ne Musa niya,
Yehova anawuza Mose kuti,
34 “Wach ni jo-Israel ni: ‘Chakre tarik apar gabich e dwe mar abiriyo en Sawo mar Kiche mar Jehova Nyasaye kendo nobedi kuom ndalo abiriyo.
“Uwawuze Aisraeli kuti pa masiku asanu ndi awiri kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri pazikhala Chikondwerero cha Misasa cholemekeza Yehova.
35 Odiechiengʼ mokwongo nobed chokruok maler ma kik uti tijeu mapile.
Tsiku loyamba ndi la msonkhano wopatulika, musagwire ntchito zolemetsa.
36 Kuom ndalo abiriyo chiwuru ni Jehova Nyasaye misengini miwangʼo pep, eka chiengʼ mar aboro to ubedi gi chokruok maler kendo chiengʼno uchiwni Jehova Nyasaye misango miwangʼo pep. En chokruok mitiekogo nyasi, omiyo kik uti tijeu mapile.
Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Kumeneku ndi kutsekera kwa msonkhano waukulu. Musagwire ntchito zolemetsa.
37 (“‘Magi e sewni moyier mag Jehova Nyasaye manyaka ulandi ni gin e chokruok maler michiwone Jehova Nyasaye gi mach kaka misengini miwangʼo pep, gi misengini mag cham gi misengini miolo piny kendo moro ka moro nigi odiechienge mowinjore.
(“‘Amenewa ndi masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova, amene muziwalengeza kuti ndi nthawi ya msonkhano wopatulika. Masiku amenewa muzipereka nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, nsembe zanyama ndi zopereka zachakumwa za tsiku ndi tsiku.
38 To ewi mago nitie Sabato mag Jehova Nyasaye gi chiwo mamoko to gi gimoro amora misesingori kaachiel gi chiwo mar hera michiwo ni Jehova Nyasaye.)
Zopereka zimenezi ndi zowonjezera pa zopereka za Yehova za pa Sabata, zopereka zanu zolumbira ndiponso mphatso zanu zaufulu zopereka kwa Yehova.)
39 “‘Omiyo kochakore e odiechiengʼ mar apar gabich mar dwe mar abiriyo bangʼ keyo to nyaka utim Sap Jehova Nyasaye kuom ndalo abiriyo. Chiengʼ mokwongo en odiechiengʼ mowal mar yweyo, kendo chiengʼ mar aboro bende en kamano.
“‘Choncho kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mutakolola zinthu mʼmunda mwanu, muchite chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Tsiku loyamba ndi tsiku lopumula, ndipo tsiku lachisanu ndi chitatu ndi lopumulanso.
40 Chiengʼ mokwongo kawuru olembe yien mabeyo gi bede othidhe, gi bede yien motimo otiep, gi omburi, kendo ubed mamor e nyim Jehova Nyasaye ma Nyasachu kuom ndalo abiriyo.
Pa tsiku loyamba muzitenga zipatso zabwino kwambiri zothyola mʼmitengo, nthambi za kanjedza, nthambi zazikulu za mitengo ya masamba ambiri, ndi za misondozi yakumtsinje, ndipo muzikondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu kwa masiku asanu ndi awiri.
41 Timuru sawoni ni Jehova Nyasaye kuom ndalo abiriyo higa ka higa. Mae en chik momakou gi nyikwau nyaka chiengʼ. Paruru ni kochopo dwe mar abiriyo to nyaka ubed gi sawoni.
Chaka chilichonse muzichita chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse. Muzichita chikondwerero chimenechi mwezi wachisanu ndi chiwiri.
42 Un jo-Israel nyaka udagi e kiche kuom ndalo abiriyo,
Muzikhala mʼmisasa masiku asanu ndi awiri. Onse amene ali mbadwa mʼdziko la Israeli azikhala mʼmisasa
43 mae ema biro miyo nyikwau nopar kaka namiyo jo-Israel odak e kiche kinde mane agologi e piny Misri. An e Jehova Nyasaye ma Nyasachu.’”
kuti zidzukulu zanu zidzadziwe kuti ndine amene ndinakhazika Aisraeli mʼmisasa nditawatulutsa ku Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
44 Kamano e kaka Musa nolando ni jo-Israel sewni moyier mag Jehova Nyasaye.
Choncho Mose analengeza kwa Aisraeli masiku osankhika a zikondwerero za Yehova.

< Tim Jo-Lawi 23 >