< Tim Jo-Lawi 18 >

1 Jehova Nyasaye nowacho ne Musa niya:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 “Wuo gi jo-Israel kendo iwachnegi ni, ‘An e Jehova Nyasaye ma Nyasachu.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
3 Kik utim timbe ma jo-Misri mane udak e diergi timo kendo kik timbe moko mag jo-Kanaan makoro aterou e diergi yudre kuomu. Bende kik uluw timbe ma gitimo.
Musamachite zomwe amachita anthu a ku Igupto kumene munkakhala kuja, ndiponso musamachite zomwe amachita anthu a ku Kanaani kumene ndikukupititsani. Musatsatire miyambo yawo.
4 Nyaka urit chikena kendo luwuru yorena, nikech an Jehova Nyasaye ma Nyasachu.
Inu muzimvera malamulo anga ndipo muzisamalitsa kutsatira malangizo anga. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
5 Rituru yorena kod chikena, nimar ngʼat moluwogi nobed mangima kuomgi. An e Jehova Nyasaye.
Choncho sungani malangizo ndi malamulo anga, popeza munthu amene amvera zimenezi adzakhala ndi moyo. Ine ndine Yehova.
6 “‘Kik ngʼato terre gi dhako moluongo ni watne. An e Jehova Nyasaye.
“‘Munthu aliyense asagonane ndi wachibale wake. Ine ndine Yehova.
7 “‘Kik ikuod wi wuonu kuom terruok gi chiege, nikech en minu.
“‘Usachititse manyazi abambo ako pogonana ndi amayi ako. Iwo ndi amayi ako. Usagonane nawo.
8 “‘Kik iterri gi chi wuonu, nikech kitimo kamano to ikelone wuonu wichkuot.
“‘Usagonane ndi mkazi wa abambo ako (osakhala amayi okubala). Ukatero ukuchititsa manyazi abambo ako.
9 “‘Kik iterri gi nyaminu mahie, kata nyameru maka wuonu machielo kata maka minu machielo, bedni onywole e dala kae, kata kamoro machielo.
“‘Usagonane ndi mlongo wako, mwana wamkazi wa abambo ako, kapena mwana wamkazi wa amayi ako, kaya anabadwira mʼnyumba mwanu kapena kwina.
10 “‘Kik iterri gi nyakwari maka wuodi kata maka nyari, nikech kitimo kamano to ikelo wichkuot ni in iwuon.
“‘Usagonane ndi mdzukulu wako: mwana wa mwana wako wamwamuna kapena mwana wa mwana wako wamkazi. Kutero nʼkudzichotsa ulemu.
11 “‘Kik iterri gi nyaminu moa e ot machielo, nikech en nyaminu.
“‘Usagonane ndi mwana wamkazi wa mkazi wa abambo ako, amene abambo akowo anabereka; popeza ameneyo ndi mlongo wako.
12 “‘Kik iterri gi nyamin wuonu nikech en wayu.
“‘Usagonane ndi mlongo wa abambo ako; popeza ameneyo ndi thupi limodzi ndi abambo ako.
13 “‘Kik iterri gi nyamin mamau nikech en bende en mamau.
“‘Usagonane ndi mchemwali wa amayi ako chifukwa ameneyo ndi thupi limodzi ndi amayi ako.
14 “‘Kik igomb terori gi chi owadgi wuonu nikech en minu, kendo mano kelo wichkuot ne wuonuno.
“‘Usachititse manyazi mchimwene wa abambo ako pogonana ndi mkazi wake popeza amenewo ndi azakhali ako.
15 “‘Kik iterri gi chi wuodi nikech en maru, ok oyieni mondo itim kamano.
“‘Usagonane ndi mpongozi wako popeza ameneyo ndi mkazi wa mwana wako. Choncho usamuchititse manyazi.
16 “‘Kik iterri gi chi owadu nikech mano nyalo kelo wichkuot ne owaduno.
“‘Usagonane ndi mkazi wa mchimwene wako popeza potero ukuchititsa manyazi mʼbale wakoyo.
17 “‘Kik iterri gi nyako kaachiel gi min-gi. Kik iterri gi nyakware ma ka wuode kata maka nyare, nikech gin wede dhakono. Mano en tim anjawo.
“‘Usagonane ndi mkazi ndiponso mwana wake wamkazi. Usagonane ndi mwana wamkazi wa mwana wake wamwamuna, kapena mwana wamkazi wa mwana wake wamkazi. Amenewo ndi thupi limodzi ndi mkaziyo. Kutero ndikuchita chinthu choyipa kwambiri.
18 “‘Kik ikend nyamin chiegi mondo obed nyieke ma iriwri kode ka nyamin pod ngima.
“‘Usakwatire mchemwali wa mkazi wako ndi kumagonana naye mkazi wakoyo ali moyo ngati wopikisana naye.
19 “‘Kik iterri gi dhako manie kindene mar neno malo.
“‘Usamuyandikire mkazi kuti ugonane naye pa nthawi yake yosamba.
20 “‘Kik iterri gi chi ngʼama udakgo mokiewo, dipo ka omiyo ibedo mogak.
“‘Usagonane ndi mkazi wa mnzako ndi kudziyipitsa naye.
21 “‘Kik ichiw nyathini moro amora ni nyasaye manono miluongo ni Molek, nimar ok onego iketh nying Nyasaye. An e Jehova Nyasaye.
“‘Usapereke mwana wako aliyense kuti akhale nsembe yamoto kwa Moleki ndi kuyipitsa dzina la Yehova. Ine ndine Yehova.
22 “‘Kik iterri gi dichwo wadu nikech mano en tim makwero.
“‘Usagonane ndi mwamuna ngati mkazi; chimenecho ndi chinthu chonyansa.
23 “‘Kik iterri gi chiayo nikech mano miyo ibedo mogak. Dhako bende kik yie mondo chiayo oterre kode, nikech mano en gima kwero.
“‘Usagonane ndi nyama ndi kudziyipitsa nayo. Mkazi asadzipereke kwa nyama kuti agonane nayo. Chimenecho ndi chisokonezo.
24 “‘Kik udwanyru kutimo timbe ma kamago nikech timbego ema ogendini mabiro riembo e nyimu ne timo.
“‘Musadzidetse ndi zinthu zimenezi chifukwa umo ndi mmene mitundu ina imene ndikuyithamangitsa pamaso panu inadzidetsera.
25 Kata mana piny bende nobedo mogak, omiyo ne akumogi nikech richo mag-gi, kendo piny nongʼogo joma nodakie iye.
Choncho dziko linayipa ndipo ndinalilanga chifukwa cha tchimo lake. Motero dzikolo linasanza anthu ake okhalamo.
26 To nyaka urit yorena kod chikena. Onge ngʼato kuomu manotim timbe makwerogo kata obed ja-Israel kata jadak e dieru,
Koma inu mukasunge malangizo ndi malamulo anga. Mbadwa ndiponso alendo amene akukhala pakati panu asakachite china chilichonse cha zinthu zonyansazi,
27 nikech magi e timbe ma joma nodak e pinyni kapok ubiro notimo kendo negiketho pinyni.
pakuti zinthu zonsezi ndi zomwe ankachita anthu amene ankakhala mʼdzikomo inu musanafike, ndipo dziko linayipitsidwa.
28 To ka udwanyo pinyno, to ngʼeuru ni onyalo ngʼogou oko mar oganda mane okwongonu dake kane gidwanye.
Koma inu musachite zimenezi kuti dziko lingakusanzeni mutaliyipitsa monga linasanzira mitundu imene imakhalamo inu musanafike.
29 “‘Jogo duto matim makwerogo noyud e ngimagi, ginto nyaka golgi oko ei ogandagi.
“‘Aliyense wochita zinthu zonyansa zimenezi achotsedwe pakati pa anthu anzake.
30 Emomiyo luwuru chikena kendo ritreuru ma kik uluw timbe makwero mane joma odak e pinyni otimo kapok ubiro, mondo kik ubed mogak. An e Jehova Nyasaye ma Nyasachu.’”
Choncho mverani malangizo anga oletsa kuchita miyambo yonyansayi imene ankatsatira anthu amene analipo inu musanafike ndi kudziyipitsa nayo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”

< Tim Jo-Lawi 18 >