< Ayub 40 >

1 Jehova Nyasaye nowachone Ayub kama:
Yehova anati kwa Yobu:
2 “Bende nitiere ngʼat mapiem gi Jehova Nyasaye Maratego manyalo kwere? Mad koro ngʼat mamino wach gi Nyasaye oduokeane!”
“Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse? Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
3 Eka Ayub nodwoko Jehova Nyasaye kama:
Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
4 “Yaye Jehova Nyasaye, ok aromo dwokora kodi omiyo mano ema omiyo alingʼ.
“Ine sindili kanthu konse, kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
5 Asewuoyo moromo, to ok ayudo dwoko omiyo koro ok abi wuoyo kendo.”
Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho, ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
6 Eka Jehova Nyasaye nodwoko Ayub gi ei yamo maduongʼ. Nowacho kama:
Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
7 “Chungʼ ane ka dichwo; mondo idwoka weche, ma adwaro penjigi.
“Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna; ndikufunsa mafunso ndipo iwe undiyankhe.
8 “Angʼo momiyo iketho adiera mara? Angʼo momiyo iketo rach kuoma mondo in inenri ka ngʼama ber?
“Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama? Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
9 Bende in gi teko machalo gi mar Nyasaye koso dwondi bende nyalo mor kaka mare?
Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu, ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
10 Ka kamano, to kare bidhriane, kirwakori gi duongʼ, luor kod ber.
Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola, ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
11 Bangʼ mano rang jogo ma sungore, kendo iol mirimbi mager kuomgi mondo omi gibolre.
Tsanula ukali wako wosefukirawo, uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
12 Ee, rang joma sungore duto kendo, ikumgi kama gichungoeno mondo omi gibolre.
Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse, uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
13 Ikgi duto e lowo; mondo ji kik negi kendo.
Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi; ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
14 Kinyalo timo kamano to an owuon ema anakuong paki ni tekri iwuon ema omiyo iloyo.
Ukatero Ine ndidzakuvomereza kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
15 “Parane rawo, mane achweyo kaka ne achweyi kendo machamo lum kaka rwadh pur chamo.
“Taganiza za mvuwu, imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe, ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
16 Parie teko mangʼeny ma en-go, kendo parie teko maduongʼ manie leche mag dende!
Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri, thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
17 Iwe yamo tero ka yiend sida; kendo leche manie bembene omoko kuome maber.
Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza; mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
18 Chokene otegno ka mula, kendo tiendene otegno ka chuma.
Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa, nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
19 Ikwane kaka chwech maberie moloyo mar Nyasaye e kind le duto, kendo en mana Jachwechne kende ema nyalo chome gi ligangla.
Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu, komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
20 Ochamo lumbe motwi ewi got, kuonde ma le mager ema kwayoe.
Imapeza chakudya chake ku mtunda ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
21 Onindo piny ei saka kendo opondo e dier odundu motwi e thidhna.
Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta, imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
22 Saka oime gi tipone; kendo omburi motwi e tie aora olwore.
Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta; imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
23 Kata ka aora opongʼ moo oko, to ok bwoge; chunye ngʼich angʼicha kata ka aora Jordan opongʼ kendo mwomore marach.
Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha, iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
24 En ngʼa manyalo dino wangʼe mi make, kata madi duode mi tuch ume?
Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza kapena kuyikola mu msampha?

< Ayub 40 >