< Ayub 14 >

1 “Dhano ma dhako onywolo ndalone nok kendo oneno chandruok mathoth.
“Munthu wobadwa mwa amayi amakhala masiku owerengeka ndipo ndi odzaza ndi mavuto okhaokha.
2 Odongo piyo piyo ka maua bangʼe to oner; mana ka tipo makadho ma ok siki.
Amaphuka ngati duwa ndipo kenaka amafota; amathawa ngati mthunzi ndipo sakhalitsa.
3 Ngʼat machal kamano bende inyalo dewo? Bende dikele e nyimi adier mondo iyale?
Kodi munthu wotereyo nʼkumuyangʼanitsitsa? Kodi mungamubweretse pamaso panu kuti mumuzenge mlandu?
4 En ngʼa manyalo kelo gima ler kogolo kuom gima ochido? Onge kata achiel!
Ndani angatulutse chabwino mʼchoyipa? Palibe ndi mmodzi yemwe!
5 Ndalo dhano nosekwan chon; isechano kar romb dwechene, kendo iseketo gikone ma ok onyal kalo.
Masiku a munthu ndi odziwikiratu; munakhazikitsa chiwerengero cha miyezi yake ndipo munamulembera malire amene sangathe kuwalumpha.
6 Omiyo gol wangʼi kuome kendo weye mos, mondo ochamie luche gi mor kaka ngʼama ondiki timo.
Choncho Inu mumufulatire ndipo mumuleke apumule kufikira atakondwera nawo moyo ngati munthu waganyu.
7 “Yien ber nyalo bedo gi geno: ka osetongʼe to nitie geno ni onyalo loth, kendo chunye maloth manyien ok rem mak odongo.
“Mtengo uli nacho chiyembekezo: ngati wadulidwa, udzaphukiranso ndipo nthambi zake sizidzaleka kuphukira.
8 Kata obedo ni tiendene towo kendo miyo osikene tho,
Mizu yake ingathe kukalamba mʼnthaka ndipo chitsa chake nʼkuwola pa dothi,
9 to kata kamano, kowinjo much pi, to oloth, mana ka yien mochako dongo.
koma pamene chinyontho chafika udzaphukira ndipo udzaphuka nthambi ngati mtengo wanthete.
10 Dhano to tho kendo iike e bwo lowo; oyweyo mogik, kendo kare rumo chuth.
Koma munthu amafa nayikidwa mʼmanda, amapuma mpweya wotsiriza ndipo kutha kwake nʼkomweko.
11 Mana kaka pi dwono e nam kata kaka dier aora pi duone mi two,
Monga madzi amaphwera mʼnyanja kapena monga mtsinje umaphwera nuwuma,
12 e kaka dhano nindo piny kendo ok ochak ochungʼ; ok ochak onen kendo bende ok nochiewe e nindoneno.
momwemonso munthu amagona ndipo sadzukanso; mpaka zamlengalenga zidzathe, anthu sadzauka kapena kudzutsidwa ku tulo tawo.
13 “Mad ne ipanda ei liel mondo ne abed maonge nyaka chop mirimbi rum, bangʼe to iket kinde ma ibiro parae kendo! (Sheol h7585)
“Aa, Inu mukanangondibisa mʼmanda ndi kundiphimba kuti ndisaoneke mpaka mkwiyo wanu utapita! Achikhala munandiyikira nthawi, kuti pambuyo pake mundikumbukirenso. (Sheol h7585)
14 Ka ngʼato otho, bende dochak obed mangima kendo? Ndalona duto mag tichna matek abiro rito, an to abiro dhil gi thagruokna, nyaka kinde maber chopi.
Munthu akafa, kodi adzakhalanso ndi moyo? Masiku anga onse a moyo wovutikawu ndidzadikira mpaka itafika nthawi yomasulidwa.
15 Ibiro luongo, kendo abiro dwoki; ibiro gombo neno chwech ma lweti osechweyo.
Inu mudzandiyitane ndipo ndidzakuyankhani; inu mudzafunitsitsa kuona cholengedwa chimene munachipanga ndi manja anu.
16 Eka inikwan kuonde matienda onyono to ok inisik kinona mondo ikwan richo ka richo matimo.
Ndithudi pamenepo mudzayangʼana mayendedwe anga koma simudzalondola tchimo langa.
17 Kethoga ibiro ket ei ofuku mi din ma ok yawre, kendo inium richona.
Zolakwa zanga zidzakulungidwa mʼthumba; inu mudzaphimba tchimo langa.
18 “Mana kaka pi ywero got kendo barore kendo kaka lwanda chorore kawuok kare,
“Koma monga phiri limakokolokera ndi kuswekasweka ndipo monga thanthwe limasunthira kuchoka pa malo ake,
19 kendo kaka pi ywero kite kendo koth maduongʼ ywero lowo, kamano e kaka iketho geno ma dhano nigo.
monganso madzi oyenda amaperesera miyala ndipo madzi othamanga amakokololera nthaka, momwemonso Inu mumawononga chiyembekezo cha munthu.
20 Ihewe dichiel kendo mogik, kendo olal nono; iloko kit wangʼe, kendo igole e dier ji chuth.
Inu mumamugonjetsa kamodzinʼkamodzi ndipo munthuyo nʼkutheratu; Inu mumasintha maonekedwe a nkhope yake ndipo mumamutaya kutali.
21 Kata ka yawuote yudo duongʼ bangʼe, to en okia kendo kata ka giyudo wichkuot, to ok one gi wangʼe.
Ana ake akamalemekezedwa, iyeyo sazidziwa zimenezo; akamachititsidwa manyazi iye saziona zimenezo.
22 Gima owinjo en mana rem manie dende owuon kendo oywagore kende owuon.”
Iye amangomva zowawa za mʼthupi lake ndipo amangodzilirira yekha mwini wakeyo.”

< Ayub 14 >