< Ayub 13 >

1 “Wengena oseneno magi duto, kendo ita osewinjo tiendgi maber.
“Ndaziona ndi maso anga zonsezi, ndazimva ndi makutu anga ndipo ndazimvetsa.
2 Gima ungʼeyo, an bende angʼeyo; kik upar ni afuwo.
Zimene inu mukudziwa, inenso ndimazidziwa; ineyo sindine munthu wamba kwa inu.
3 To Jehova Nyasaye Maratego ema daher mondo awuogo kendo mondo anyis Nyasaye gik mane chunya.
Koma ine ndikulakalaka nditayankhula ndi Wamphamvuzonse ndi kukamba mlandu wanga ndi Mulungu.
4 Un to uumo adiera gi miriambo; uchalo jothieth ma ok nyal thiedho tuo!
Koma inu mukundipaka mabodza; nonsenu ndinu asingʼanga opanda phindu!
5 Kudwaro nyiso ni uriek to mad koro ulingʼ alingʼa kar wuoyo!
Achikhala munangokhala chete nonsenu! Apo mukanachita zanzeru.
6 Koro winjuru ane gima awacho; chikuru itu ne ywakna.
Tsopano imvani kudzikanira kwanga; imvani kudandaula kwa pakamwa panga.
7 Ere gima omiyo uwuoyo marach kuom Nyasaye? Koso uparo ni miriambou biro konyo Nyasaye?
Kodi inu mudzayankhula moyipa kuyankhulira Mulungu? Kodi mudzayankhulira Iyeyo mwachinyengo?
8 Bende Nyasaye nyalo yie kodu kudwaro loko adiera bedo miriambo?
Kodi mudzaonetsa kuti Iyeyo ngokondera? Kodi inu mudzamuteteza Mulungu pa mlandu wake?
9 Bende doyud adiera kuomu kononou? Bende duwuonde kaka uwuondo dhano?
Mulungu atayangʼanitsitsa, inu nʼkukupezani wosalakwa? Kodi inu mungamunamize Iye monga momwe munganamizire munthu?
10 Obiro kwerou ratiro kapo ni udew wangʼ ji.
Ndithudi, Iye angathe kukudzudzulani ngati muchita zokondera mseri.
11 Donge tekone biro goyou gi kihondko? Donge mbi mare biro bwogou?
Kodi ulemerero wake sungakuopseni? Kodi kuopsa kwake sikungakuchititseni mantha?
12 Ngeche muthoro mangʼenygo onge tich mana ka buch kendo; wecheu yomyom mana ka agulni mag lowo.
Mawu anu anzeru ali ngati miyambi yopanda tanthauzo; mawu anu odzitchinjirizira ali ngati mpanda wadothi.
13 “Lingʼuru kendo weyauru awuo; mondo gima dwaro timorenano otimre.
“Khalani chete ndipo ndilekeni ndiyankhule; tsono zimene zindichitikire zichitike.
14 Angʼo madimi abed e chandruok, ka atiyo gi ngimana mana kaka an ema ahero?
Chifukwa chiyani ndikuyika moyo wanga pa chiswe ndi kutengera mʼmanja moyo wangawu?
15 Kata ka onega, to pod abiro keto genona kuome; omiyo pod abiro mana wacho wechena e nyime.
Ngakhale Iye andiphe, komabe ndidzamukhulupirira; ndithu, ndidzafotokoza mlandu wanga pamaso pake.
16 Chutho, mano ema biro kelona resruok nikech onge ngʼama okia Nyasaye, manyalo hedhore michopi e nyime.
Zoonadi, ichi ndiye chidzakhala chipulumutso changa pakuti palibe munthu wosapembedza amene angafike pamaso pake!
17 Chik iti mos mondo iwinj wechena; kendo yie mondo iwinj gik ma awacho.
Mvetserani mosamala mawu anga; makutu anu amve zimene ndikunena.
18 Kaka koro aseikora dwoko wach makora, angʼeyo ni ubiro kwana kaka ngʼama kare.
Pakuti tsopano ndawukonzekera mlandu wanga, ndikudziwa ndipo adzandipeza wolungama.
19 Bende ngʼato kuomu nyalo donjona ni an jaketho? Ka en kamano, to abiro lingʼ kendo kata tho ayie tho.
Kodi alipo wina amene angatsutsane nane? ngati zili choncho, ndidzakhala chete ndi kufa.
20 “Yaye Nyasaye, yie itimna mana gik moko ariyogi mondo kik apondni.
“Inu Mulungu, ndipatseni zinthu ziwiri izi, ndipo pamenepo ine sindidzakubisalirani:
21 Gol lweti oko kuoma kendo iyie igolna masichegi mabwoga.
Muchotse dzanja lanu pa ine, ndipo muleke kundichititsa mantha ndi kuopsa kwanuko.
22 Eka iluonga e nyimi kendo abiro dwoki, kata iyiena awuo mondo idwoka.
Tsono muyitane ndipo ndidzayankha, kapena mulole kuti ine ndiyankhule ndipo Inu muyankhe.
23 Richo gi ketho adi ma asetimo? Nyisa kethona gi richona.
Kodi zolakwa zanga ndi zingati ndipo machimo anga ndi angati? Wonetseni kulakwa kwanga ndi machimo anga.
24 Angʼo momiyo ipando wangʼi kendo ikawa kaka jasiki?
Chifukwa chiyani mukundifulatira ndi kundiyesa ine mdani wanu?
25 It yien ayiena ma yamo teroni to isando nangʼo? Mihudhi motwo ma yamo tero, to ilawo nangʼo?
Kodi mudzazunza tsamba lowuluka ndi mphepo? Kodi mudzathamangitsa mungu wowuma?
26 Idonjona gi weche malit, moriw koda ka richo mane atimo kapod an rawera.
Pakuti Inu mwalemba zinthu zowawa zonditsutsa nazo ndipo mukundipaka machimo a pa ubwana wanga.
27 Irido tiendena gi nyororo; kendo iluwo bangʼa e yorena maluwo duto, koketo kido e bwo tienda mondo onyis kamoro amora maluwo.
Inu mwamanga miyendo yanga ndi maunyolo. Mumayangʼanitsitsa mayendedwe anga onse poyika zizindikiro pamene mapazi anga apondapo.
28 “Omiyo koro dhano rumo mos mos kaka gima otop, mana ka nanga ma olwenda ochamo.”
“Motero munthu amatha ngati chinthu chofumbwa, ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.

< Ayub 13 >