< Jeremia 9 >

1 Yaye, mad wiya bed ka soko mar pi kendo pi wangʼa mol ka aora! Dwaywak odiechiengʼ kod otieno nikech nek mar joga.
Aa, ndikanakonda kuti mutu wanga ukanakhala chitsime cha madzi, ndi maso anga ngati kasupe wa misozi! Ndikanalira usana ndi usiku kulirira anthu anga amene aphedwa.
2 Yaye, mad ne abed gi kar nindo michulo ne jowuoth e piny ongoro, mondo omi awe joga kendo adhi mabor kodgi; nimar giduto gin jochode, kanyakla mar joma onge adiera.
Ndani adzandipatsa malo ogona mʼchipululu kuti ndiwasiye anthu anga ndi kuwachokera kupita kutali; pakuti onse ndi achigololo, ndiponso gulu la anthu onyenga.
3 “Giketo lewgi moikore ka atungʼ, mondo gidirgo miriambo; to dhigi maber e piny ok nikech giwacho adiera. Gitimo richo bangʼ moro ka moro; ok gidewa.” Jehova Nyasaye ema owacho.
“Amapinda lilime lawo ngati uta. Mʼdzikomo mwadzaza ndi mabodza okhaokha osati zoonadi. Amapitirirabe kuchita zoyipa; ndipo sandidziwa Ine.” Akutero Yehova.
4 “Beduru motangʼ gosiepeu; kik uket genou kuom oweteu. Nimar oweteu duto jo-miriambo, kendo osiep moro amora jakwoth.
“Aliyense achenjere ndi abwenzi ake; asadalire ngakhale abale ake. Aliyense amafuna kumudyera mʼbale wake masuku pa mutu. Choncho aliyense amachitira bwenzi lake ugogodi.
5 Osiep wuondo osiep, kendo onge ngʼama wacho adiera. Gisepuonjo lewgi wacho miriambo; kendo gisedonjo matut e richo ma ok ginyal wuokie.
Aliyense amamunamiza mʼbale wake ndipo palibe amene amayankhula choonadi. Anapazoloweza pakamwa pawo kunena zabodza; amalimbika kuchita machimo.
6 Idak e kind jo-miriambo; e wuondruokgino gisedagi yie kuoma.” Jehova Nyasaye ema owacho.
Iwe wakhalira mʼchinyengo ndipo ukukana kundidziwa Ine,” akutero Yehova.
7 Emomiyo ma e gima Jehova Nyasaye Maratego wacho: “Ne, abiro pwodhogi kendo temogi, nimar en angʼo machielo manyalo timo, nikech richo mar joga?
Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, Ine ndidzawasungunula ngati chitsulo ndi kuwayesa. Kodi ndingachite nawonso bwanji chifukwa cha machimo awo?
8 Lewgi en asere man-gi kwiri; owacho miriambo. Gi dhoge owuoyo mamuol ne jabathe, to e chunye oketone obadho.”
Lilime lawo lili ngati muvi wakuthwa; limayankhula zachinyengo. Aliyense ndi pakamwa pake amayankhula mawu achikondi kwa mnansi wake, koma mu mtima mwake amakonzekera zomuchita chiwembu.
9 Jehova Nyasaye wacho niya, “Donge dakumgi ne ma? Donge dachul kuor ne oganda ma kama?”
Kodi ndilekerenji kuwalanga chifukwa cha zimenezi? akutero Yehova. ‘Kodi ndisawulipsire mtundu wotere wa anthu?’”
10 Abiro ywak kendo dengo ne gode bende anaywag lege motwo, mosedongʼ nono, kendo onge gima wuothoe, bende ywak mar jamni ok winjie. Winy mafuyo e kor polo oseringo, kendo le osedhi.
Ndidzakhetsa misozi ndi kulira kwamphamvu chifukwa cha mapiri ndipo ndidzadandaula chifukwa cha msipu wa ku chipululu. Malo onsewo awonongeka ndipo palibe amene amapitako, ndipo sikumveka kulira kwa ngʼombe. Mbalame zamlengalenga zathawa ndipo nyama zakuthengo zachokako.
11 “Anami Jerusalem obed gunda, kama ondiegi ema odakie; kendo anaketh mier mag Juda mondo ngʼato kik dag kanyo.”
Ndipo Yehova anati, “Ndidzasandutsa Yerusalemu kukhala bwinja, malo okhalamo ankhandwe; ndipo ndidzawononga mizinda ya Yuda kotero kuti palibe munthu amene adzakhalemo.”
12 En ngʼa mariek manyalo winjo tiend ma? En ngʼa mosetiegi gi Jehova Nyasaye kendo nyalo lero tiende? Angʼo momiyo piny osekethi modongʼ nono ka kama otwo maonge ngʼama nyalo luwo?
Ine ndinati, “Kodi munthu wanzeru ndani woti nʼkumvetsa zimenezi? Kodi ndani amene Yehova anayankhula naye zimenezi kuti akafotokozere ena? Nʼchifukwa chiyani dziko lawonongeka ndi kusanduka chipululu, mʼmene anthu sadutsamo?”
13 Jehova Nyasaye nowacho niya, “Nikech gisejwangʼo chikna, mane amiyogi; omiyo ok giseluora kata luwo chikna.
Yehova anati, “Nʼchifukwa chakuti anthuwa analeka kutsata malamulo anga amene ndinawapatsa; sanandimvere kapena kuwasamala.
14 To giseluwo mana timbegi mag wich teko; bende giseluwo bangʼ Baal, mana kaka wuonegi nopuonjogi.”
Mʼmalo mwake, anatsatira zolakwa za mʼmitima yawo; anapembedza Abaala ngati momwe makolo awo anawaphunzitsira.”
15 Emomiyo, ma e gima Jehova Nyasaye Maratego ma Nyasach Israel, wacho: “Ne, anami jogi cham chiemo makech kendo modh pi sum.
Tsono chimene Ine Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli ndidzachite ndi anthu amenewa ndi ichi: “Ndidzawadyetsa chakudya cha ziphe ndi kuwamwetsa madzi a ndulu.
16 Anakegi e dier ogendini ma gin kata wuonegi ok ongʼeyo, kendo analawgi gi ligangla manyaka atiekgi.”
Ndidzawabalalitsa pakati pa mitundu ya anthu imene iwowo kapena makolo awo sanayidziwe, ndipo ndidzawalondola ndi ankhondo mpaka nditawawononga.”
17 Ma e gima Jehova Nyasaye Maratego wacho: “Parane! Luonguru mon madengo mondo obi; to moloyo mago man-gi lony mamalo e ywak.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsopano ganizirani! Muyitane akazi olira mwachisoni kuti abwere; itanani akazi odziwa kulira bwino.”
18 Giret piyo mondo gidengnwa, nyaka wengewa pongʼ gi pi wangʼ ma oo kendo pi wangʼwa mol ma luokwa.
Anthu akuti, “Abwere mofulumira kuti adzatilire mpaka mʼmaso mwathu mutatuluka misozi ndi kuti msidze zathu zinyowe ndi madzi.
19 Koko mar dengo iwinjo koa Sayun: ‘Mano kaka otiekowa! Mano kaka wichkuot marwa duongʼ! Nyaka waa e pinywa nikech utewa osemuki.’”
Kulira mwachisoni kukumveka kuchokera mu Ziyoni akuti, ‘Aa! Ife tawonongeka! Tachita manyazi kwambiri! Tiyenera kuchoka mʼdziko lathu chifukwa atipirikitsa mʼnyumba zathu.’”
20 Koro, yaye mon, winjuru wach Jehova Nyasaye; yawuru itu ne weche mawuok e dhoge. Puonjuru nyiu dengo; puonjreuru ywak uwegi.
Tsono inu amayi, imvani mawu a Yehova; tcherani makutu anu kuti mumve mawu a Yehova. Phunzitsani ana anu aakazi kulira mwachisoni; aliyense aphunzitse mnzake nyimbo ya maliro.
21 Tho oseidho gie dirisni magwa kendo osedonjo kuondewa mochiel motegno gohinga; osengʼado nyithindo oko e yore kendo rowere e kuonde budho mag galamoro.
Imfa yatifikira kudzera mʼmazenera athu ndipo yalowa mʼnyumba zathu zotetezedwa; yapha ana athu mʼmisewu, ndi achinyamata athu mʼmabwalo.
22 Wach niya, “Ma e gima Jehova Nyasaye owacho: “‘Ringre joma otho nopie ka owuoyo e pap alanga, kaka cham mokaa gi jakeyo, maonge ngʼama nyalo chokogi.’”
Yehova anandiwuza kuti ndinene izi kuti, “‘Mitembo ya anthu idzakhala ili lambalamba ngati ndowe mʼminda, ngati mapesi mʼmbuyo mwa wokolola, popanda munthu woyitola.’”
23 Ma e gima Jehova Nyasaye wacho: “Kik ngʼama riek sungre gi riekone kata ngʼama tek sungre gi tekone, kata ngʼama omewo sungre gi mwandu mage,
Yehova akuti, “Munthu wanzeru asanyadire nzeru zake, kapena munthu wamphamvu kunyadira nyonga zake, kapena munthu wolemera kunyadira chuma chake,
24 to ngʼat ma sungore mondo osungre kama: ni ongʼeya, kendo owinja, ni An e Jehova Nyasaye, matimo ngʼwono, kendo mangʼado bura mar adier, kendo matimo gik makare e piny, nikech magi ema amorgo,” Jehova Nyasaye ema owacho.
koma ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire chinthu ichi: kuti iye amamvetsa za Ine ndipo amandidziwa, kuti ndine Yehova, amene ndimakonda chifundo, chilungamo ndiponso ungwiro pa dziko lapansi. Zimenezi ndizo ndimakondwera nazo,” akutero Yehova.
25 Jehova Nyasaye wacho niya, “Ndalo biro ma anakumie joma oter nyangu e ringruok kende
“Nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzalanga onse amene anachita mdulidwe koma mu mtima sasamala nʼkomwe.
26 kaka Misri, Juda, Edom, Amon, Moab gi jogo duto modak kuonde motimo ongoro man maboyo. Nimar ogendinigi duto ok oter nyangu adier, kendo kata od Israel duto bende ok oter nyangu e chunygi.”
Ndidzalanga anthu a ku Igupto, Yuda, Edomu, Amoni, Mowabu, ndiponso onse amene amakhala kutali ku chipululu. Mitundu ina yonseyi ndi yosachita mdulidwe, ngakhalenso Aisraeli nawonso sanachite mdulidwe wa mu mtima.”

< Jeremia 9 >