< Jeremia 49 >

1 Wach kuom jo-Amon: Ma e gima Jehova Nyasaye wacho: “Onge yawuowi e Israel? Oonge gi jarit girkeni mage? To kare angʼo momiyo Molek osekawo mwandu Gad? Angʼo momiyo joge odak e dalane?”
Yehova ananena izi: Amoni, “Kodi Israeli alibe ana aamuna? Kapena alibe mlowamʼmalo? Tsono nʼchifukwa chiyani anthu opembedza Moleki alanda dziko la Gadi? Nʼchifukwa chiyani anthu ake akukhala mʼmizinda ya Gadi?
2 Jehova Nyasaye wacho niya, “To ndalo biro, ma anagoye koko mar lweny mondo oked gi Raba mar jo-Amon; enobed pith mar kethruok, kendo gwenge molworogi nowangʼ. Eka Israel noriemb jogo mane oriembogi,” Jehova Nyasaye ema owacho.
Koma nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzamveketse mfuwu wankhondo ku Raba, likulu la Amoni; ndipo malo awo opembedzera milungu yawo adzatenthedwa ndi moto. Choncho Aisraeli adzalandanso dziko lawo kuchokera kwa amene anawalanda poyamba dzikolo,” akutero Yehova.
3 “Dengi, yaye Heshbon, nimar Ai okethi! Ywaguru, yaye joma odak Raba! Rwakuru lepu mag ywak kendo uywagi; ringuru koni gi koni, e alwora mar dala, nimar Molek noter e twech, kaachiel gi jodolo mage kod jotelo mage.
“Lirani, inu anthu a ku Hesiboni chifukwa wowononga uja wafika! Fuwulani, inu anthu okhala ku Raba! Valani ziguduli ndi kulira mwamphamvu; thamangani uku ndi uku mʼkati mwa malinga, chifukwa mulungu wanu Moleki adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndiponso akuluakulu ake.
4 Angʼo momiyo usungoru kuom holo mau, sungruok kuom holo mau manyak? Yaye nyako ma ok ja-ratiro, igeno kuom mwandu magi kendo iwacho niya, Ngʼama biro monja?
Chifukwa chiyani mukunyadira chigwa chanu, inu anthu osakhulupirika amene munadalira chuma chanu nʼkumati: ‘Ndani angandithire nkhondo?’
5 Anakel luoro kuomu koa kuom jogo duto man butu,” Ruoth, Jehova Nyasaye Maratego ema owacho. “Un duto noriembu, kendo onge ngʼama nochok joma noringo moke.
Ndidzabweretsa zoopsa pa iwe zochokera kwa onse amene akuzungulira,” akutero Ambuye, Mulungu Wamphamvuzonse. “Mudzathawa, ndipo aliyense adzathawitsa moyo wake. Sipadzapezeka munthu wosonkhanitsanso othawawo.
6 “Kata kamano bangʼe, anaduog mwandu jo-Amon,” Jehova Nyasaye ema owacho.
“Komabe pambuyo pake, ndidzabwezera kwawo Aamoni,” akutero Yehova.
7 Ma e gima Jehova Nyasaye Maratego wacho kuom Edom: “Bende pod nitie rieko ei Teman? To puonj oselalne jorieko? To rieko mag-gi osetop?
Yehova Wamphamvuzonse ananena izi za Edomu: “Kodi nzeru sizikupezekanso ku Temani? Kodi anzeru analeka kupereka uphungu? Kodi nzeru zawo zinatheratu?
8 Lokreuru kendo uringi, ponduru e rogo mopandore, un joma odak Dedan, nimar anakel masira ne Esau e kinde ma anakume.
Inu anthu a ku Dedani, thawani, bwererani ndi kukabisala ku makwalala chifukwa ndidzagwetsa mavuto pa zidzukulu za Esau popeza nthawi yawo ya chiweruzo yafika.
9 Ka jopon olemb mzabibu obiro iru, donge digiwe olemb mzabibu matin? Ka jokwoge obiro gotieno, donge gibiro kwalo mwandu magu kaka ginyalo?
Kodi anthu othyola mphesa akanafika kwa inu akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha? Anthu akuba akanafika usiku akanangotengako zimene akuzifuna zokha?
10 To analony Esau duk; anael kuondege malingʼ-lingʼ, mondo omi kik opondi. Nyithinde, wedene gi jomodak bute nolal nono, kendo ok nochak obed chutho.
Koma ine ndazivula zidzukulu za Esau. Ndaonetsa poyera malo awo obisalamo, kotero kuti sadzathanso kubisala. Ana ake, abale ake pamodzi ndi anansi ake awonongeka. Palibe wonena kuti,
11 Weuru kiye mau; anares ngimagi. Mondu duto ma chwogi otho, bende nyalo keto geno mag-gi kuoma.”
‘Siyani ana anu amasiye; Ine ndidzawateteza. Amayi anu amasiye akhoza kudalira Ine.’”
12 Ma e gima Jehova Nyasaye wacho: “Ka jogo ma ok owinjore omadh kikombe nyaka madhe, to angʼo momiyo ok anyal kumi? Ok initony ma ok okumi, to nyaka imadhe.”
Yehova akuti, “Ngati iwo amene sanali oyenera kulangidwa adzamwa chikho cha chiweruzo, ndiye muyesa kuti inuyo simudzalangidwa? Ayi ndithu simudzakhala osalangidwa. Mudzamwa ndithu chikhocho.
13 Jehova Nyasaye wacho niya, “Akwongʼora gi nyinga awuon, ni Bozra nokethi kendo nobed gir bwogo ji, gir jaro kendo nobed gir kwongʼ, kendo mieche duto nokethi chuth.”
Ine ndikulumbira, akutero Yehova, kuti mzinda wa Bozira udzasanduka bwinja, chinthu chochititsa mantha, chomachiseka ndiponso chotembereredwa. Mizinda yake yonse idzakhala mabwinja mpaka muyaya.”
14 Asewinjo wach koa kuom Jehova Nyasaye kama: Jaote oseor mondo owach ne ogendini niya, “Chokreuru mondo umonje! Chungʼuru malo wadhi e kedo!”
Ndamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu ina kukanena kuti, “Sonkhanani pamodzi kuti muthire nkhondo Edomu! Konzekerani nkhondo!”
15 “Koro abiro miyo udok matin e kind ogendini, kendo joma ijaro e dier ji.
“Ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina. Mudzakhala anthu onyozeka pakati pa anthu.
16 Luoro musemiyo ji kod sunga manie chunyu osewuondou, un jogo modak e kind lwendni, modak kuonde motingʼore gi malo mar got. Kata obedo ni ugero uteu mabor ka od otenga, koa kuno abiro dwokou piny,” Jehova Nyasaye owacho.
Kuopseza kwako kwakunyenga; kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndi mʼmapiri. Ngakhale utamanga chisa chako pamwamba kwambiri ngati chiwombankhanga, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
17 “Edom nobed gima bwogo ji; jogo duto makalo bute nohum nono, kendo gininyiere ka gineno adhondene duto.”
“Dziko la Edomu lidzasanduka chinthu chochititsa mantha. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake.
18 Jehova Nyasaye wacho niya, “Mana kaka Sodom gi Gomora nokethi, kaachiel gi mier mokiewo kodgi, e kaka en bende nobedi maonge ngʼato angʼata modak kanyo kendo.
Monga momwe anawonongekera Sodomu ndi Gomora, pamodzi ndi mizinda yake yozungulira,” akutero Yehova, “motero palibe munthu amene adzakhala mu Edomu.
19 “Ka sibuor mabiro koa e bungu moyugno mar Jordan nyaka kar kwath man-gi lum, anariemb Edom oa e pinye kadiemo wangʼ. En ngʼa mowal manyalo yiero ne ma? En ngʼa machalo koda kendo manyalo chungʼ koda? Koso jakwath mane manyalo chungʼ koda?”
“Monga mkango wotuluka ku nkhalango za ku Yorodani kupita ku malo a msipu wobiriwira, Ine ndidzapirikitsa anthu a ku Edomu mwadzidzidzi kuchoka mʼdziko lawo. Pambuyo pake ndidzawayikira owalamulira amene ndamufuna Ine. Kodi ndani wofanana nane, ndipo angatsutsane nane ndani? Ndipo ndi mʼbusa uti amene angalimbane nane?”
20 Emomiyo, winj gima Jehova Nyasaye osechano timo ne Edom, gima oseramo ni nyaka otimne joma odak Teman: Nyithi rombe bende nokaw; enoketh chuth kuondegi mag kwath nikech gin.
Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Edomu ndi a ku Temani. Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
21 Piny noyiengni kowinjo ni ologi; ywakgi nowinjre nyaka e Nam Makwar.
Akadzagwa Edomu padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera; kulira kwawo kudzamveka mpaka ku Nyanja Yofiira.
22 Ne! Otenga nofu kochomo malo kendo piny koyaro bwombene ewi Bozra. E odiechiengno chunje jolweny mag Edom nochal gi chuny dhako mamuoch kayo.
Taonani, mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkudzatera pa Bozira ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Edomu idzagunda ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
23 Kuom Damaski: “Hamath gi Arpad luoro omako, nimar giwinjo wach marach, chunygi omoko, kendo nigi chandruok ka nam mogingore.
Mawu a Yehova onena za Damasiko ndi awa: “Anthu a ku Hamati ndi a ku Aripadi akuchita mantha chifukwa amva nkhani yoyipa. Mitima yawo yagwidwa ndi mantha ndipo ali ngati muja ichitira nyanja yosakhazikika.
24 Damaski osebedo maonge teko, osea gi ngʼwech, kendo achiedh-nade osemake; lit gi rem osemake, kaka rem mar dhako mamuoch kayo.
Anthu a ku Damasiko alefuka. Abwerera mʼmbuyo kufuna kuthawa chifukwa agwidwa ndi mantha aakulu. Ali ndi nkhawa komanso mantha ngati za mayi pa nthawi yake yochira.
25 Angʼo momiyo ok osejwangʼ dala maduongʼ mongʼere; dala mamor godo?
Mzinda wotchuka ndi wachikondwerero uja wasiyidwa!
26 Adiera, joge matindo nopodh e yore; jolweny mage duto nolingʼ thi odiechiengno,” Jehova Nyasaye Maratego owacho.
Nʼchifukwa chake anyamata ake adzagwa mʼmisewu ndi kufa; ankhondo ake onse adzawonongedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
27 “Anawangʼ ohingini mag Damaski; notiek kuonde mochiel motegno mag Ben-Hadad.”
“Ndidzatentha malinga a Damasiko; moto udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.”
28 Kuom Kedar gi pinyruodhi mag Hazor, mane Nebukadneza ruodh Babulon omonjo: Ma e gima Jehova Nyasaye wacho: “Chungʼuru malo, kendo umonj Keda, mi utiek joma aa yo wuok chiengʼ.
Mawu a Yehova onena za Kedara ndi maufumu a ku Hazori, amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawagonjetsa ndi awa: “Nyamukani mukathire nkhondo ku Kedara. Kawonongeni anthu a kummawako.
29 Hembegi gi jambgi nokaw; kar dak margi nowal oko, kaachiel gi mwandugi duto kod ngamia. Ji nogonegi koko ni, ‘Masira maduongʼ koni gi koni!’”
Landani matenti awo ndi nkhosa zawo, ndiye kuti, mutenge nsalu zawo ndi katundu wawo. Mutengenso ngamira zawo. Anthu adzafuwula kwa iwo kuti, ‘Kuli zoopsa mbali zonse!’
30 Jehova Nyasaye wacho niya, “Ringuru piyo uayi! Daguru e rogo matut, un joma odak Hazor. Nebukadneza ruodh Babulon nigi paro marach kuomu; osechano timonu marach.
“Thawani mofulumira! Kabisaleni mʼmakhwawa, inu anthu ku Hazori,” akutero Yehova. “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni wakukonzerani chiwembu; wakonzekera zoti alimbane nanu.
31 “Chunguru kendo umonj pinyni momewo, modak kodhil,” Jehova Nyasaye owacho, “piny maonge dhorangeye kata lodi; joge odak kendgi.
“Nyamukani kathireni nkhondo mtundu wa anthu umene uli pamtendere, umene ukukhala mosatekeseka,” akutero Yehova, “mzindawo ulibe zipata ngakhalenso mipiringidzo; anthu ake amakhala pa okha.
32 Ngamia mag-gi noyaki kendo kweth mag dhogi nope. Anake joge mantie kuma bor e tunge piny kendo anakelnegi masira koa koni gi koni,” Jehova Nyasaye owacho.
Ngamira zawo zidzafunkhidwa, ndipo makola a ngʼombe zawo adzalandidwa. Ndidzabalalitsira ku mphepo zinayi onse amene amameta tsitsi lawo chamʼmbali. Ndidzawagwetsera mavuto kuchokera ku mbali zonse,” akutero Yehova.
33 “Hazor nobed thim mar ondiegi, kama ojwangʼ nyaka chiengʼ. Onge ngʼama nodag kanyo; onge ngʼama nodag e iye.”
“Hazori adzasanduka bwinja, malo okhalamo nkhandwe mpaka muyaya. Palibe munthu amene adzayendemo.”
34 Ma e wach Jehova Nyasaye mane obirone janabi Jeremia kuom Elam, e ndalo chakruok mar loch Zedekia ruodh Juda:
Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za Elamu, Zedekiya mfumu ya Yuda atangoyamba kulamulira ndi uwu:
35 Ma e gima Jehova Nyasaye Maratego, wacho: “Ne, anatur atung Elam, girgi maduongʼ mar tekogi.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, ndidzathyola uta wa Elamu, umene uli chida chawo champhamvu.
36 Anamonj Elam gi yembe angʼwen moa e tunge angʼwen mar polo; anakegi e yembe angʼwen-go kendo onge piny ma jo-Elam momaki ok nodhiye.
Ndidzabweretsa mphepo zinayi pa Elamu kuchokera ku zigawo zinayi zamlengalenga; ndidzawabalalitsira ku mphepo zinayi, ndipo sipadzakhala dziko limene anthu a ku Elamu sadzafikako.
37 Anami Elam ongʼengʼ e nyim wasike, e nyim jogo madwaro tieko ngimagi; anakel masiche kuomgi, ma en mirimba mager,” Jehova Nyasaye ema owacho. “Analawgi gi ligangla manyaka atiekgi.”
A ku Elamuwo ndidzachititsa mantha pamaso pa adani awo komanso pamaso pa iwo amene akufuna kuwononga moyo wawo. Ndidzawagwetsera mkwiyo wanga ndipo adzakhala pa mavuto,” akutero Yehova. “Ndidzawapirikitsa ndi lupanga mpaka nditawatheratu.
38 Jehova Nyasaye wacho niya, “Anaket koma mar duongʼ ei Elam, kendo atiek ruodhe kod jotende.”
Ndidzakhazika mpando wanga waufumu ku Elamu ndipo ndidzawononga mfumu yake pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.
39 “Kata kamano anaduog mwandu Elam e ndalo ma biro,” Jehova Nyasaye ema owacho.
“Komabe mʼtsogolomo ndidzabwezera anthu a ku Elamu dziko lawo,” akutero Yehova.

< Jeremia 49 >