< Jeremia 46 >

1 Ma e wach Jehova Nyasaye mane obirone janabi Jeremia kuom ogendini:
Yehova anamupatsa Yeremiya uthenga wonena za anthu a mitundu ina.
2 Kuom Misri: Ma e ote ne jolwenj Farao Neko ruodh Misri, mane oloo Karkemish e Aora mar Yufrate gi Nebukadneza ruodh Babulon e higa mar angʼwen mar Jehoyakim wuod Josia ruodh Juda:
Kunena za Igupto: Yehova ananena za gulu lankhondo la Farao Neko mfumu ya ku Igupto limene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni analigonjetsa ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate mʼchaka cha chinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda,
3 “Ikuru okumba magu, madongo kod matindo, kendo uwuog udhi e kedo!
anati, “Konzani zishango zanu ndi malihawo, ndipo yambanipo kupita ku nkhondo!
4 Gauru farese, idhuru farese! Kawuru kereu kurwako oguteu mag lweny! Piaguru tongeu, rwakuru okumba mau!
Mangani akavalo, ndipo kwerani inu okwerapo! Khalani pa mzere mutavala zipewa! Nolani mikondo yanu, valani malaya anu ankhondo!
5 En angʼo ma aneno? Kihondko ogoyogi, kendo giringo ka gia kar lweny nikech thuondi mag-gi mag lweny oselo. Giringo ka luoro omakogi ma ok gingʼi ngʼegi, kendo gin-gi luoro malich koni gi koni,” Jehova Nyasaye wacho.
Yeremiya anati: Kodi ndikuona chiyani? Achita mantha akubwerera, ankhondo awo agonjetsedwa. Akuthawa mofulumirapo osayangʼananso mʼmbuyo, ndipo agwidwa ndi mantha ponseponse,” akutero Yehova.
6 “Joma yot ok nyal ringo kata joma otegno ok nyal tony. E yo nyandwat but Aora Yufrate gichwanyore kendo gipodho.
Waliwiro sangathe kuthawa ngakhale wankhondo wamphamvu sangathe kupulumuka. Akunka napunthwa ndi kugwa kumpoto kwa mtsinje wa Yufurate.
7 “Ma en ngʼa magingore ka aora Nael kendo mana ka aore ma pigegi bubni?
“Kodi ndani amene akukwera ngati Nailo, ngati mtsinje wa madzi amkokomo?
8 Misri bubni ka aora Nael kendo mana ka aore ma pigegi bubni. Owacho ni, ‘Abiro gingora kendo anapongʼ piny; anaketh mier madongo kod ji modakie.’
Igupto akusefukira ngati Nailo, ngati mitsinje ya madzi amkokomo. Iye akunena kuti, ‘Ndidzadzuka ndi kuphimba dziko lapansi; ndidzawononga mizinda ndi anthu ake.’
9 Wuoguru, yaye farese! Yaye, un joriemb geche, riembgiuru matek! Dhiuru nyime, yaye un jolweny machwo moa Kush, gi Put motingʼo okumbini, kaachiel gi chwo Lidia maywayo atungʼ.
Tiyeni, inu akavalo! Thamangani inu magaleta! Tulukani, inu ankhondo, ankhondo a ku Kusi ndi Puti amene mumanyamula zishango, ankhondo a ku Ludi amene mumaponya uta.
10 To odiechiengno en mar Ruoth, Jehova Nyasaye Maratego ma en odiechiengʼ, ma ochuloe kuor ni wasike. Ligangla noneki nyaka owinj ni orome, kendo nyaka otiek riyo mare gi remo. Nimar Ruoth, Jehova Nyasaye Maratego, nochiw misango e piny mantie yo nyandwat but Aora Yufrate.
Koma tsikulo ndi la Ambuye Yehova Wamphamvuzonse; tsiku lolipsira, lolipsira adani ake. Lupanga lake lidzawononga ndi kukhuta magazi, lidzaledzera ndi magazi. Pakuti Yehova, Yehova Wamphamvuzonse, adzapereka adani ake ngati nsembe mʼdziko la kumpoto mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
11 “Dhiyo nyaka Gilead kendo imany yath, yaye Nyar Misri Mangili. To kata obedo ni imedo manyo yedhe to imenyo kayiem kendo ok inichangi.
“Pita ku Giliyadi ukatenge mankhwala iwe namwali Igupto. Wayesayesa mankhwala ambiri koma osachira; palibe mankhwala okuchiritsa.
12 Ogendini nowinj wichkuot momaki; ywakni nopongʼ piny. Jolweny nochwanyre kuom moro ka moro; giduto ginipodhi kanyakla.”
Anthu a mitundu ina amva za manyazi ako; kulira kwako kwadzaza dziko lapansi. Ankhondo akunka nagwetsanagwetsana, onse awiri agwa pansi limodzi.”
13 Ma e ote mane Jehova Nyasaye owachone Jeremia janabi kuom biro Nebukadneza ruodh Babulon mondo omonj Misri:
Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za kubwera kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kudzathira nkhondo Igupto ndi uwu:
14 “Land wachni e piny Misri, kendo igo milome e Migdol; Memfis gi Tapanhes ni: ‘Kawuru kereu kendo ikreuru, nimar ligangla nego jogo molwori.’
“Mulengeze ku Igupto. Mulengeze ku Migidoli. Mulengezenso ku Mefisi ndi ku Tapanesi. Muwawuze anthu akumeneko kuti, ‘Imani pamalo panu ndi kukhala okonzeka kudziteteza, chifukwa lupanga lidzawononga zonse zimene muli nazo.’
15 En angʼo momiyo jolweny magu opie piny? Ok ginyal chungʼ, nimar Jehova Nyasaye nolwargi piny.
Chifukwa chiyani mulungu wanu wamphamvu uja Apisi wathawa? Iye sakanatha kulimba chifukwa Yehova anamugwetsa.
16 Ginichwanyre moluwore oluwore; giniluowre kuom jowetegi. Giniwachi ni, ‘Aa malo, wadog ir jowa wawegi; kendo e pinywa owuon, mabor gi ligangla mar joma thiro ji.’
Ankhondo anu apunthwa ndi kugwa. Aliyense akuwuza mnzake kuti, ‘Tiyeni tibwerere kwathu, ku dziko kumene tinabadwira, tithawe lupanga la adani athu.’
17 E kanyono giniwach ni, ‘Farao ruodh Misri en mana jakoko matek, nikech thuolo mane en-go nobaye.’”
Kumeneku iwo adzafuwula kuti, ‘Farao, mfumu ya ku Igupto mupatseni dzina lakuti, Waphokoso, Wotaya mwayi wake.’
18 Ruoth wacho niya, “Akwongʼora gi nyinga awuon, ma en Jehova Nyasaye Maratego, ngʼato achiel nobi machalo gi Tabor e dier gode, kata ka Got Karmel mantie but nam.
“Pali Ine wamoyo,” ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse, “wina adzabwera amene ali ngati Tabori phiri lopambana mapiri ena, ngati phiri la Karimeli loti njoo mʼmbali mwa nyanja.
19 Pang gigi mar dhiyoe twech, un joma odak Misri, nimar Memfis nowe gunda, kendo tieke chuth maonge ngʼama nodagie.”
Konzani katundu wanu wopita naye ku ukapolo inu anthu a ku Igupto, pakuti Mefisi adzasanduka chipululu ndipo adzakhala bwinja mopanda wokhalamo.
20 “Misri en nyaroya maber neno, to kalabugo birone koa yo nyandwat.
“Igupto ali ngati mwana wangʼombe wokongola, koma chimphanga chikubwera kuchokera kumpoto kudzalimbana naye.
21 Jolweny mondiki chal gi nyiroye machwe. Gin bende ginilokre kendo giring kanyakla, ok giniriti, nimar odiechiengʼ mar masira biro kuomgi, kinde margi mar kum.
Ngakhale ankhondo aganyu amene ali naye ali ngati ana angʼombe onenepa. Nawonso abwerera mʼmbuyo, nathawa pamodzi. Palibe amene wachirimika. Ndithu, tsiku la tsoka lawafikira; ndiyo nthawi yowalanga.
22 Misri nokudhi ka thuol maringo ka jasigu masudo machiegni gi teko; giniked kode gi ledhi, mana ka chwo matongʼo yiende.”
Aigupto akuthawa ndi liwu lawo lili ngati la njoka yothawa pamene adani abwera ndi zida zawo, abwera ndi nkhwangwa ngati anthu odula mitengo.
23 Jehova Nyasaye wacho niya, “Ginibet bungu mare, kata obedo ni oyugno kamano. Gingʼeny moloyo dede, ok nyal kwan-gi.
Iwo adzadula nkhalango ya Igupto,” akutero Yehova, “ngakhale kuti ndi yowirira. Anthuwo ndi ochuluka kupambana dzombe, moti sangatheke kuwerengeka.
24 Nyar Misri nomi wichkuot, kendo nochiwe ne jogo moa yo nyandwat.”
Anthu a ku Igupto achita manyazi atengedwa ukapolo ndi anthu a kumpoto.”
25 Jehova Nyasaye Maratego, ma Nyasach Israel, wacho niya, “Achiegni kelo kum kuom Amon ma nyasach Thebes, kuom Farao, kuom Misri gi nyisechene kod ruodhi mage, kod jogo mogeno kuom Farao.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, “Ndili pafupi kulanga Amoni mulungu wa Tebesi. Ndidzalanganso Farao ndi Igupto pamodzi ndi milungu yake yonse, mafumu ake ndi onse amene amamukhulupirira.
26 Anachiwgi ne jogo madwaro ngimagi, ne Nebukadneza ruodh Babulon gi jotende. To kata kamano ji nodhi nyime dak Misri kaka chon,” Jehova Nyasaye owacho.
Ndidzawapereka kwa amene akufuna kuwapha, ndiye kuti kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi atsogoleri ake ankhondo. Komabe, mʼtsogolomo Igupto adzakhalanso ndi anthu monga kale,” akutero Yehova.
27 “Kik iluor; yaye jatichna Jakobo; bende kik ibwogi, yaye Israel. Adiera abiro resi e piny mabor, kaachiel gi nyikwayi e piny mane otergie twech. Jakobo nodhi nyime ka nigi kwe gi dak maonge luoro, kendo onge ngʼama nobwoge.
“Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha; usataye mtima, iwe Israeli. Ndithu Ine ndidzakupulumutsa kuchokera ku mayiko akutali, ndidzapulumutsanso zidzukulu zako kuchokera ku mayiko kumene anapita nazo ku ukapolo. Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala motakasuka ndi pa mtendere, ndipo palibenso wina amene adzamuopsa.
28 Kik iluor, yaye Jakobo jatichna, nimar an kodi. Kata obedo ni atieko ogendini duto ma asekeyou e diergi, ok anatieku chuth. Anakumu to mana gi bura makare; ok anaweu ngangʼ ma ok akumou,” Jehova Nyasaye owacho.
Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe,” akutero Yehova. “Ndidzawonongeratu mitundu yonse ya anthu a ku mayiko kumene ndakupirikitsira, Koma iwe sindidzakuwononga kotheratu. Ndidzakulanga iwe ndithu koma moyenerera; sindidzakulekerera osakulanga.”

< Jeremia 46 >