< Jeremia 42 >

1 Eka jotend lweny duto, kaachiel gi Johanan wuod Karea kod Jezania wuod Hoshaya, kod ji duto chakre matin nyaka maduongʼ nodhi ir
Atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi Yohanani mwana wa Kareya ndi Azariya mwana wa Hosayia, ndiponso anthu onse, ana ndi akuluakulu omwe, anapita
2 janabi Jeremia kendo owachone niya, “Kiyie to iwinj kwayowa kendo ilamnwa Jehova Nyasaye ma Nyasachi ne joma otonygi duto. Nimar kaka ineno sani, kata obedoni chon ne wangʼeny, to koro sani ji matin ema odongʼ.
kwa mneneri Yeremiya ndipo anamuwuza kuti, “Chonde imvani dandawulo lathu ndipo mutipempherere anthu otsalafe kwa Yehova Mulungu wanu. Pakuti monga tsopano mukuona, ngakhale kuti kale tinalipo ambiri, koma tsopano ochepa okha ndiye amene atsala.
3 Lem mondo Jehova Nyasaye ma Nyasachi onyiswa kuma wanyalo dhiyoe kendo gima wanyalo timo.”
Mupemphere kuti Yehova Mulungu wanu atiwuze kumene tiyenera kupita ndi chimene tiyenera kuchita.”
4 Janabi Jeremia nodwoko niya, “Asewinjou. Adier nyaka analamnu Jehova Nyasaye ma Nyasacha kaka usekwayo; ananyisu gimoro amora ma Jehova Nyasaye owacho kendo onge gima anapandnu.”
Mneneri Yeremiya anawayankha kuti, “Ndamva zimene mwanenazi. Ndithu ndidzapemphera kwa Yehova Mulungu wanu monga momwe mwandipemphera. Ndidzakuwuzani chilichonse chimene Yehova anene ndipo sindidzakubisirani kanthu kalikonse.”
5 Eka negiwachone Jeremia, “Mad Jehova Nyasaye bed ja-adiera kendo janeno makare kuomwa ka dipo ni timbewa ok oluwore gi gimoro ma Jehova Nyasaye ma Nyasachi ooroi godo irwa.
Ndipo iwo anawuza Yeremiya kuti, “Yehova akhale mboni yoona ndi yokhulupirika yodzatitsutsa ife ngati sitichita mogwirizana ndi chilichonse chimene Yehova Mulungu adzakutumani kuti mutiwuze.
6 Kowinjore kata ka ok owinjore, wanaluor Jehova Nyasaye ma Nyasachwa, ma waori ire, mondo omi obed maber kodwa, nimar wanaluor Jehova Nyasaye ma Nyasachwa.”
Kaya ndi zotikomera kapena zosatikomera, ife tidzamvera Yehova Mulungu wathu, amene takutumaniko. Tidzamvera Yehova Mulungu wathu kuti zinthu zidzatiyendere bwino.”
7 Bangʼ ndalo apar wach Jehova Nyasaye nobiro ne Jeremia.
Patapita masiku khumi, Yehova anayankhula ndi Yeremiya.
8 Omiyo noluongo Johanan wuod Karea kod jotend lweny mane ni kode kod ji duto chakre matin nyaka maduongʼ.
Choncho Yeremiya anayitana Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye ndiponso anthu onse, ana ndi akulu omwe.
9 Nowachonegi niya, “Ma e gima Jehova Nyasaye, Nyasach Israel, mane uora ire mondo aterne kwayou, wacho:
Yehova, Mulungu wa Israeli amene munanditumako kuti ndikapereke madandawulo mʼdzina lanu akuti,
10 ‘Ka idak e pinyni, anageru kendo ok anatieku; anapidhu to ok pudhou oko, nimar asebedo gi lit kuom masiche masekelo kuomu.
“Ngati mukhala mʼdziko muno, ndiye kuti ndidzakukhazikitsani, osakuchotsani. Inde ndidzakudzalani osakuchotsani pakuti ndi kumva chisoni kwambiri chifukwa cha mavuto amene ndabweretsa pa inu.
11 Kik uluor ruodh Babulon, makoro uluoro. Kik uluore, Jehova Nyasaye wacho, nimar an kodu kendo anaresu ua e lwetene.
Musayiope mfumu ya ku Babuloni, imene mukuyiopa tsopano. Musachite nayo mantha, akutero Yehova, pakuti Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani ndi kukulanditsani mʼmanja mwake.
12 Anatimnu ngʼwono mondo omi en bende ongʼwonnu kendo odwoku e pinyu.’
Ndidzakuchitirani chifundo, ndipo mfumuyonso idzakuchitirani chifundo ndi kukulolani kuti mukhale mʼdziko mwanumwanu.
13 “To ka uwacho, ‘Ok wanadagie pinyni,’ mamano mi ubed ma ok uluoro Jehova Nyasaye ma Nyasachu,
“Koma mwina simudzamvera Yehova Mulungu wanu nʼkumanena kuti, ‘Ayi ife sitidzakhala mʼdziko muno,
14 kendo ka uwacho ni, ‘Ooyo, wanadhi kendo wadag Misri, kama ok wana neye lweny kata winjo turumbete kata bedo gi kech mar makati,’
ndipo ngati mukunena kuti, ‘Ayi, koma tidzapita ku Igupto kumene sitidzaonako nkhondo kapena kumva kulira kwa lipenga kapenanso kusowa chakudya.’
15 to uwinj wach Jehova Nyasaye, yaye joma otony modongʼ mag Juda. Ma e gima Jehova Nyasaye Maratego, ma Nyasach Israel, wacho: ‘Ka uramo ni nyaka udhi Misri kendo udhi udak kanyo,
Tsono, inu otsala a ku Yuda, imvani mawu a Yehova. Iye akuti, ngati mutsimikiza zopita ku Igupto, nʼkupitadi kukakhala kumeneko,
16 to ngʼeuru ni ligangla ma uluoro nomaku, kendo kech mabwogou noluu nyaka Misri, kendo kanyo ema unuthoe.
ndiye nkhondo imene mukuyiopayo idzakugonjetsani ku Igupto komweko. Njala imene mukuyiopayo idzakupezani ku Igupto komweko ndipo mudzafera kumeneko.
17 Adiera, jogo duto moramo mondo odhi odag Misri noneg gi ligangla, kech kod masira maonge ngʼato angʼata ma notony e chandruok mabiro kelo kuomgi.’
Kunena zoona, onse amene atsimikiza zopita ku Igupto kuti akakhale kumeneko adzafa ndi nkhondo njala ndi mliri. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzapulumuke kapena kuthawa mavuto amene ndidzawagwetsera.’
18 Ma e gima Jehova Nyasaye Maratego, ma Nyasach Israel, wacho: ‘Kaka ich wangʼ mara kod mirimba aseolo kuom jogo modak Jerusalem, e kaka mirimba ibiro olo kuomu ka udhi Misri. Inibed gir kwongʼ kendo mabwogo ji, gima ingʼadogo bura kendo gir ajara; ok unuchak une kaeni kendo.’
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Momwe ndinawakwiyira mwaukali anthu okhala mu Yerusalemu, koteronso ndidzakukwiyirani mukapita ku Igupto. Mudzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, choseketsa ndi chonyozeka. Malo ano simudzawaonanso.’
19 “Yaye jo-Juda modongʼ, Jehova Nyasaye osenyisou ni, ‘Kik udhi Misri.’ Beduru gadiera kuom ma: Asiemou kawuono
“Inu otsala a ku Yuda, Yehova wakuwuzani kuti, ‘Musapite ku Igupto.’ Dziwani chinthu ichi: Ine lero ndikukuchenjezani
20 ni ne uketho ketho malich kane uora ir Jehova Nyasaye ma Nyasachu kendo uwacho ni, ‘Lamnwa Jehova Nyasaye ma Nyasachwa; nyiswa gik moko duto mowacho kendo wanatim kamano.’
kuti munalakwitsa kwambiri. Inu munandituma kwa Yehova Mulungu wanu nʼkumati ‘Mukatipempherere kwa Yehova Mulungu wathu, nʼkudzatiwuza chimene afuna kuti tichite, ndipo ife tidzachita.’
21 Asewachonu kawuono, to pod ok uluoro Jehova Nyasaye ma Nyasachu kuom gigo duto mane oora mondo anyisu.
Ine lero ndakuwuzani, koma inu simukumverabe zonse zimene Yehova Mulungu anandituma kuti ndikuwuzeni.
22 Omiyo koro, beduru gadieri kuom ma: Nonegu gi ligangla, kech kod masira kuma udwaro dhiye mondo udagie.”
Tsono dziwani ichi: mudzafadi ndi nkhondo, njala ndi mliri kumalo kumene mukufuna mukakhaleko.”

< Jeremia 42 >