< Jeremia 27 >

1 E chakruok mar loch Zedekia wuod Josia ruodh Juda, wachni nobiro ne Jeremia koa ir Jehova Nyasaye:
Zedekiya mwana wa Yosiya, mfumu ya ku Yuda, atangoyamba kulamulira, Yehova anawuza Yeremiya kuti,
2 Ma e gima Jehova Nyasaye nowachona: “Los jok gi tol kod lodi moriw kendo ikete e ngʼuti.
“Tenga zingwe zomangira ndi mitengo ya goli ndipo uzimangirire mʼkhosi mwako.
3 Eka ior wach ne ruodhi mag Edom, Moab, Amon, Turo kod Sidon kokalo kuom jombetre mosebiro Jerusalem ir Zedekia ruodh Juda.
Tsono utumize uthenga kwa mafumu a Edomu, Mowabu, Amoni, Turo ndi Sidoni kudzera mwa amithenga amene abwera ku Yerusalemu kwa Zedekiya, mfumu ya Yuda.
4 Migi ote mar jotendgi kendo iwachi ni, ‘Ma e gima Jehova Nyasaye Maratego ma, Nyasach Israel, wacho: “Nyisuru jotendu kama:
Uwapatse uthenga wokapereka kwa ambuye awo ndipo uwawuze kuti: Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Mukawuze ambuye anu kuti:
5 Kuom tekona maduongʼ asechweyo piny gi joge kod le duto manie iye, kendo achiwo gigagi ne ngʼato angʼata mahero.
Ndi mphamvu zanga ndi dzanja langa lamphamvu ndinalenga dziko lapansi ndi anthu ake onse pamodzi ndi nyama zili mʼmenemo, ndipo ndimalipereka kwa aliyense amene ndikufuna.
6 Koro anachiw pinjeu ne jatichna Nebukadneza ruodh Babulon; anami kata le mag bungu winje.
Tsopano ndidzapereka mayiko anu onse kwa mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni. Ndamupatsanso nyama zakuthengo zonse kuti zimutumikire.
7 Ogendini duto notine kod wuode kod nyakware ma wuowi nyaka kinde mar pinye chopi; eka pinje mangʼeny kod ruodhi maroteke nokete obed jatichgi.
Anthu a mitundu yonse adzamutumikira iyeyo, mwana wake ndi chidzukulu chake mpaka nthawi itakwana yoti dziko lake liwonongedwe. Pamenepo mitundu yambiri ndi mafumu amphamvu adzamugonjetsa.
8 “‘“Jehova Nyasaye wacho niya: Kapo ni piny kata gwengʼ moro amora ok noti ne Nebukadneza ruodh Babulon kata kulo wiye e bwo jok mare, to anakum pinyno gi ligangla, kech kod masira, nyaka ane ni atieke gi lwete.
“‘Koma ngati anthu a mtundu wina uliwonse kapena ufumu wina uliwonse adzakana kutumikira Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kapena kusenza goli lake, Ine ndidzalanga mtundu umenewo ndi lupanga, ndi njala ndi mliri, akutero Yehova, mpaka nditawapereka mʼmanja mwake kotheratu.
9 Omiyo kik uchik itu ne jonabi magu, jokor wach magu, joloknu lek, jo-nyakalondo kata ajuoke magu manyisou ni ok unutine ruodh Babulon.
Choncho musamvere aneneri anu, owombeza anu, otanthauza maloto anu, amawula anu kapena amatsenga anu akamakuwuzani kuti, ‘Simudzatumikira mfumu ya ku Babuloni.’
10 Gikoronu miriambo ma biro miyo idarou mabor gi pinyu; anariembu kendo unutho.
Iwo akukuloserani zabodza kotero kuti adani adzakuchotsani mʼdziko lanu nʼkupita nanu ku dziko lakutali. Ndidzakupirikitsani ndi kukuwonongani kotheratu.
11 To ka oganda moro amora enokulre e bwo jok mar ruodh Babulon mi otine, to anami ogandano odongʼ e pinye owuon mondo opure kendo mondo odagi kanyo, Jehova Nyasaye owacho.”’”
Koma ngati mtundu wina uliwonse udzagonjera mfumu ya ku Babuloni ndi kuyitumukira, ndidzawusiya kuti ukhale mʼdziko lake kuti uzilima ndi kukhalamo, akutero Yehova.’”
12 Ne amiyo Zedekia ruodh Juda wach achielni. Ne awacho niya, “Kul wiyi e bwo jok mar ruodh Babulon; tine kod joge, to ibiro dak.
Uthenga womwewu ndinawuzanso Hezekiya mfumu ya Yuda. Ndinati, “Gonjerani mfumu ya ku Babuloni. Itumikireni iyoyo pamodzi ndi anthu ake ndipo mudzakhala ndi moyo.
13 Angʼo madimi in kod jogi tho e dho ligangla, kech kod masira mano ma Jehova Nyasaye osechano timo ni ogendini ma ok bi tiyone ruodh Babulon?
Nanga inu ndi anthu anu, muferenji ndi lupanga, ndi njala, ndi mliri, zimene Yehova waopsezera mtundu wina uliwonse umene sudzatumikira mfumu ya ku Babuloni?
14 Kik uchik itu ne jonabi mawachonu ni, ‘Ok ubi tiyone ruodh Babulon,’ nimar gikoronu miriambo.
Musamvere mawu a aneneri akamakuwuzani kuti, ‘Simudzatumikira mfumu ya ku Babuloni,’ chifukwa zimene akukuloseranizo nʼzabodza.
15 Jehova Nyasaye wacho ni, ‘Ok aorogi. Gikoro miriambo e nyinga. Emomiyo, anariembu kendo unulal nono, un kaachiel gi jonabi ma koronu.’”
Sindinawatume ngakhale iwo akulosera mʼdzina langa. Nʼchifukwa chake, ndidzakupirikitsani ndipo mudzawonongeka kotheratu, inu pamodzi ndi aneneri amene akunenera zabodza kwa inu.”
16 Eka ne awachone jodolo kod jogi duto niya, “Ma e gima Jehova Nyasaye wacho: Kik uchik itu ne jonabi mawacho ni, ‘Machiegnini koro gigo duto moa e od Jehova Nyasaye ibiro duogi koa Babulon.’ Gikoronu miriambo.
Kenaka ndinawuza ansembe pamodzi ndi anthu ena onse kuti, “Yehova akuti: Musamvere aneneri amene akumanena kuti, ‘Posachedwapa ziwiya za mʼNyumba ya Yehova zibwera kuchokera ku Babuloni.’ Iwowo akunenera zabodza kwa inu.
17 Kik iwinjgi. Tine ruodh Babulon, to inibed mangima. Angʼo momiyo dala maduongʼni nyaka kethi?
Musawamvere. Tumikirani mfumu ya ku Babuloni, ndipo mudzakhala ndi moyo. Mzindawu usandukirenji bwinja?
18 Ka gin jonabi kendo gin-gi wach Jehova Nyasaye, to mondo gikwa Jehova Nyasaye Maratego gigo mabeyo modongʼ e od Jehova Nyasaye kod e kar dak mar ruodh Juda kod e Jerusalem kik ter Babulon.
Ngati iwo ndi aneneri ndipo ali ndi mawu a Yehova, apempheretu kwa Yehova Wamphamvuzonse kuti ziwiya zimene zatsala mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba ya mfumu ya Yuda ndiponso mu Yerusalemu zisatengedwe kupita ku Babuloni.
19 Nimar ma e gima Jehova Nyasaye Maratego wacho kuom sirni, Nam, gik minyalo tingʼ kod gik mamoko modongʼ e dala maduongʼni,
Pakuti Yehova akunena za zipilala, za mbiya ya madzi, maphaka ndi ziwiya zina zimene zatsala mu Yerusalemu.
20 mane Nebukadneza ruodh Babulon ne ok okawo sa mane otero Jehoyakin wuod Jehoyakim ruodh Juda e twech kogole Jerusalem nyaka Babulon kaachiel gi joka ruoth moa Juda gi Jerusalem,
Izi ndi zimene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni sanatenge pamene anatenga ukapolo Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya Yuda kupita ku Babuloni kuchokera ku Yerusalemu, pamodzi ndi anthu olemekezeka a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
21 ee, ma e gima Jehova Nyasaye Maratego, ma Nyasach Israel, wacho kuom gigo mane odongʼ e od Jehova Nyasaye kendo e kar dak mar ruodh Juda kod e Jerusalem:
Inde, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena za zinthu zimene zinatsala mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba ya mfumu ya Yuda ndi mu Yerusalemu kuti,
22 ‘Notergi Babulon kendo kanyo ginidongʼ nyaka odiechiengʼ ma anabi kawogie. Eka anadwog-gi kendo aketgi kae.’” Jehova Nyasaye owacho.
‘Zidzatengedwa kupita ku Babuloni ndipo zidzakhala kumeneko mpaka tsiku limene ndidzawakumbukirenso,’ akutero Yehova. ‘Pamenepo ndidzazitenganso ndi kuzibwezanso ku malo ano.’”

< Jeremia 27 >