< Jeremia 20 >

1 Ka jadolo Pashur wuod Imer, jatelo maduongʼ manie hekalu mar Jehova Nyasaye, nowinjo Jeremia kakoro gigie,
Wansembe Pasuri mwana wa Imeri, woyangʼanira wamkulu wa Nyumba ya Yehova, anamva Yeremiya akulosera zinthu zimenezi.
2 nomiyo Jeremia janabi ogo mi otweye e lodi mar Dhorangach Mamalo mar Benjamin mantiere e hekalu mar Jehova Nyasaye.
Tsono iye analamula kuti mneneri Yeremiyayo amenyedwe ndi kuyikidwa mʼndende pa Chipata chakumtunda kwa Benjamini ku Nyumba ya Yehova.
3 Kinyne, ka Pashur nogonye e lodi, Jeremia nowachone niya, “Jehova Nyasaye ok luongi ni Pashur, to oluongi ni Magor-Misabib.
Mmawa mwake, Pasuri anatulutsa Yeremiya mʼndende, ndipo Yeremiyayo anamuwuza kuti, “Pasuri, Yehova sadzakutchulanso dzina lako kuti Pasuri koma Zoopsa pa Mbali Zonse.
4 Nimar ma e gima Jehova Nyasaye wacho: ‘Anami ibed masira ni in iwuon kaachiel gi osiepeni duto; gi wengeni iwuon ininegi ka inegogi gi ligangla mar wasikgi. Anachiw jo-Juda duto ni ruodh Babulon, manotergi e piny Babulon kata negogi gi ligangla.
Pakuti Yehova akuti, ‘Ndidzakusandutsa choopsa kwa mwiniwakewe ndi kwa abwenzi ako onse; iweyo ukuona. Anthu a ku Yuda ndidzawapereka onse mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ena adzatengedwa ukapolo ku Babuloni ndipo ena adzaphedwa pa nkhondo.
5 Anami wasikgi mwandu duto mar dala maduongʼni gige duto moloso, gige duto ma nengogi tek kod mwandu duto mokan mag ruodhi Juda. Ginikawgi kaka gima opee mi notingʼ-gi ka iterogi Babulon.
Ndidzapereka kwa adani awo chuma chonse cha mu mzinda uno, phindu lonse la ntchito yake, zinthu zake zonse za mtengowapatali ndiponso katundu yense wa mafumu a ku Yuda. Iwo adzazitenga monga zinthu zolanda ku nkhondo ndi kupita nazo ku Babuloni.
6 To in, Pashur, kod jogo duto modak e odi noteru e twech Babulon. Kanyo unuthoe kendo noyiku, in kod osiepeni duto mane isekoronegi miriambo.’”
Ndipo iwe, Pasuri, pamodzi ndi onse a pa banja pako mudzapita ku ukapolo ku Babuloni. Mudzafera kumeneko ndi kuyikidwa mʼmanda, iweyo pamodzi ndi abwenzi ako amene unawalosera zabodza.’”
7 Yaye Jehova Nyasaye, ne iwuonda kendo nowuonda; ne ihewa kendo iloya giteko. Itugo koda odiechiengʼ mangima; kendo ji duto nyiera.
Inu Yehova, mwandinamiza, ndipo ndinapusadi; Inu ndi wamphamvu kuposa ine ndipo munandipambana. Anthu akundinyoza tsiku lonse. Aliyense akundiseka kosalekeza.
8 Sa moro amora ma awuoyo, aywak ka goyo milome mar lweny kod kethruok. Omiyo wach Jehova Nyasaye osekelona ayany kod wichkuot odiechiengʼ mangima.
Nthawi iliyonse ndikamayankhula, ndimafuwula kunena kuti, ziwawa kuno! Tikuwonongeka! Mawu anu Yehova andisandutsa chinthu chonyozeka ndipo ndimachitidwa chipongwe tsiku lonse.
9 To ka awacho. “Ok analuonge kata wuoyo kendo e nyinge,” wachne chalo mach e chunya, mana ka mach marewo chokega. Aol gi tingʼe e chunya; adier, ok anyal.
Koma ndikanena kuti, “Sindidzalalikiranso za Iye kapena kuyankhulanso mʼdzina lake,” mawu anu amayaka ngati moto mu mtima mwanga, amakhaladi ngati moto wotsekeredwa mʼmafupa anga. Ndapirira kusunga mawu anu mu mtima mwanga osawatulutsa, koma sindingathe kupirirabe.
10 Awinjo ji mangʼeny kakwodho wach, “Bwok nitie koni gi koni! Wadonjneuru! Wadonjneuru!” Osiepena duto rito mondo dhoga okier, kagiwacho, “Sa moro inyalo wuonde; eka bangʼe wanapodh kuome kendo wanachul kuor kuome.”
Ndimamva anthu ambiri akunongʼona kuti, “Zoopsa ku mbali zonse! Kamunenezeni! Tiyeni tikamuneneze!” Onse amene anali abwenzi anga akuyembekezera kuti ndigwa pansi, akumanena kuti, “Mwina mwake adzanyengedwa; tidzamugwira ndi kulipsira pa iye.”
11 To Jehova Nyasaye ni koda kaka jalweny maratego; omiyo jogo masanda nochwanyre kendo ok giniloya. Ok ginilo kendo ginibedi gi wichkuot malich; wichkuot margi wich ok nowil godo.
Koma Yehova ali nane, ndiye wankhondo wamphamvu. Nʼchifukwa chake ondizunza adzalephera ndipo sadzandipambana. Adzachita manyazi kwambiri chifukwa sadzapambana. Manyazi awo sadzayiwalika konse.
12 Yaye Jehova Nyasaye Maratego, in ngʼatno manono joma ratiro, kendo manyo matut mar chuny kod paro, mad iol gero mari kuomgi, nimar ne in asetieko kora.
Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumayesa anthu molungama ndipo mupenya za mu mtima mwa munthu. Ndiloleni kuti ndione kuti mwalipsira adani anga popeza ndapereka mlandu wanga kwa Inu.
13 Werne Jehova Nyasaye! Pak Jehova Nyasaye! Oreso ngima joma nigidwaro, e lwet joma timbegi mono.
Imbirani Yehova! Mutamandeni Yehova! Iye amapulumutsa wosauka mʼmanja mwa anthu oyipa.
14 Okwongʼ chiengʼ mane onywola! Mad odiechiengʼ mane minwa onywola kik gwedhi!
Litembereredwe tsiku limene ndinabadwa! Tsiku limene amayi anga anandibereka lisatamandidwe!
15 Okwongʼ ngʼatno mane okelone wuonwa wach, manomiye obedo gi mor, kowacho, “Nyathi monywolni en wuowi!”
Wotembereredwa munthu amene anapita kukasangalatsa abambo anga ndi uthenga woti: “Kwabadwa mwana wamwamuna!”
16 Mad ngʼatno chal gi mier mane Jehova Nyasaye owito oko maonge ngʼwono. Mad owinj dengo gokinyi kod ywak mar kedo e dier odiechiengʼ tir.
Munthu ameneyo akhale ngati mizinda imene Yehova anayiwononga mopanda chisoni. Amve mfuwu mmawa, phokoso la nkhondo masana.
17 Nimar ne ok onega e ich, ka ii minwa bedo kaka bur miika, noyawre nyaka chiengʼ.
Chifukwa sanandiphere mʼmimba, kuti amayi anga asanduke manda anga, mimba yawo ikhale yayikulu mpaka kalekale.
18 Angʼo momiyo ne awuok e ich mondo ane thagruok kod lit, kendo atiek odiechiengega e wichkuot?
Kodi ndinabadwira mavuto ndi chisoni kuti moyo wanga ukhale wamanyazi wokhawokha?

< Jeremia 20 >