< Jeremia 14 >

1 Ma e wach Jehova Nyasaye mane omiyo Jeremia e wach oro:
Awa ndi mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya onena za chilala:
2 “Juda ywak, mieche madongo winjo lit; gidengo ne piny, kendo ywak winjore koa Jerusalem.
“Yuda akulira, mizinda yake ikuvutika; anthu ake adzigwetsa pansi mwachisoni, kulira kwa Yerusalemu kwakula.
3 Joka ruoth oro jotichgi manyo pi; gidhi e sokni to ok giyud pi. Gidwogo gi agulni mag-gi ka ok otuome pi, ka giluor kendo gibuok, giumo wiyegi.
Anthu awo wolemekezeka akutuma antchito awo kuti akatunge madzi. Apita ku zitsime osapezako madzi. Choncho amabwerera ndi mitsuko yopanda madzi. Amanyazi ndi othedwa nzeru adziphimba kumaso.
4 Lo nigi okak nikech onge koth e piny; jopur luoro omako kendo giumo wiyegi.
Popeza pansi pawumiratu chifukwa kulibe madzi, alimi ali ndi manyazi ndipo amphimba nkhope zawo.
5 Kata mwanda manie puodho jwangʼo nyathine nikech onge lum.
Ngakhale mbawala yayikazi ikusiya mwana wake wakhanda ku thengo chifukwa kulibe msipu.
6 Punde mag bungu chungʼ ka kuonde motwo motingʼore gi malo, kendo gigamo yweyo ka ondiegi; wengegi ok nyal neno nimar onge kar kwath.”
Mbidzi zikuyima pa zitunda zopanda kanthu nʼkumapuma wefuwefu ngati nkhandwe; maso awo achita chidima chifukwa chosowa msipu.”
7 Kata obedo ni richowa nyisowa ni wan joketho, yaye Jehova Nyasaye, tim gimoro nikech nyingi. Wasebaro waweyo yoreni; kendo wasetimo richo e nyimi.
Anthu akuti, “Ngakhale machimo athu akutitsutsa, koma Inu Yehova chitanipo kanthu chifukwa cha dzina lanu. Pakuti kusakhulupirika kwathu nʼkwakukulu; ife takuchimwirani.
8 Yaye geno mar Israel, Jares mare e kinde mag thagruok, en angʼo momiyo ichalo wendo e piny, kaka jawuoth mobuoro otieno achiel?
Inu Yehova amene Aisraeli amakukhulupirirani ndi amene mumawapulumutsa pa nthawi ya masautso, chifukwa chiyani mukukhala ngati mlendo mʼdziko muno? Chifukwa chiyani muli ngati wapaulendo amene akungogona tsiku limodzi?
9 Ere gima omiyo ichalo gi ngʼat mobuok, kata ka jalweny maonge gi teko ma dokonygo ngʼato? In e dierwa, yaye Jehova Nyasaye, kendo iluongowa kod nyingi; kik ijwangʼwa!
Chifukwa chiyani muli ngati munthu amene wadzidzimutsidwa, kapena ngati wankhondo amene alibe mphamvu yopulumutsa? Komabe Inu Yehova, muli pakati pathu, ndipo tikudziwika ndi dzina lanu; musatitaye ife!”
10 Ma e gima Jehova Nyasaye wacho kuom jogi: “Gihero bayo alanda kendo tiendegi ok ywe. Kuom mano, Jehova Nyasaye ok orwakogi; omiyo koro obiro paro timbegi mamono, kendo okumgi kuom richogi.”
Zimene Yehova akunena za anthuwa ndi izi: “Iwo amakonda kuyendayenda kwambiri; samatha kudziretsa. Nʼchifukwa chake Ine Yehova sindingawalandire, ndipo tsopano ndidzakumbukira zoyipa zawo ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo.”
11 Eka Jehova Nyasaye nowachona, “Kik ilam mondo jogi odhi maber.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Usawapempherere anthu awa kuti zinthu ziwayendere bwino.
12 Kata ka gitweyo chiemo; ok anawinj ywakgi; kata bed ni gichiwo misango miwangʼo pep kod chiwo mag cham, ok anarwakgi. To kata kamano ananeg-gi gi ligangla, kech kod dera.”
Ngakhale asale zakudya, Ine sindidzamva kulira kwawo; ngakhale apereke nsembe zopsereza ndi chopereka cha chakudya, sindidzazilandira. Mʼmalo mwake, ndidzawapha ndi lupanga, njala ndi mliri.”
13 To ne awacho niya, “Yaye, Jehova Nyasaye Manyalo Gik Moko Duto, jonabi osebedo kanyisogi ni, ‘Ok unune ligangla kata kech bende ok nokau. Adiera, anamiu kwe mochwere kaeni.’”
Koma ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova, aneneri amawawuza anthuwo kuti, sadzaphedwa ndi lupanga kapena kuvutika ndi njala. Koma kuti Inu mudzawapatsa mtendere wokhawokha pamalo pano.”
14 Eka Jehova Nyasaye nowachona, “Jonabigo koro miriambo e nyinga. Pok aorogi, kata walogi kata wuoyo kodgi. Ginyisou fweny manono, gikoro weche manono gilamo nyiseche manono kod pachgi giwegi morundore.
Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Ndi zabodza kuti aneneriwa akunenera mʼdzina langa. Ine sindinawatume kapena kuwasankha kapenanso kuyankhula nawo. Iwo amakuwuzani zinthu zabodza zomwe amati anaziona mʼmasomphenya, kapena pogwiritsa ntchito mawula achabechabe. Zimene amayankhula ndi zongopeka mʼmutu mwawo.
15 Emomiyo, ma e gima Jehova Nyasaye wacho kuom jonabi makoro e nyinga: Ne ok aorogi, kata bed ni giwacho niya, ‘Onge ligangla kata kech manobi e pinyni.’ Jonabi gogo-go notiek gi ligangla kod kech.
Nʼchifukwa chake Ine Yehova ndikuti aneneri amenewa akulosera mʼdzina langa pamene Ine sindinawatume. Iwo amati simudzafa pa nkhondo kapena ndi njala mʼdziko muno. Koma tsono ndi iwowo, aneneriwa amene adzafe pa nkhondo kapena ndi njala.
16 Kendo jogo ma gikorone nowit oko e yore mag Jerusalem nikech kech kod ligangla. Onge ngʼama noikgi kata mondegi, yawuotgi kata nyigi. Anaol kuomgi masiche mowinjore kodgi.
Ndipo anthu amene anawaloserawo adzaponyedwa mʼmisewu ya mu Yerusalemu atafa ndi njala ndi lupanga. Sipadzapezeka wowayika mʼmanda popeza iwowo, akazi awo, ana awo aamuna, onse adzakhala atafa. Ine ndidzawagwetsera chilango chowayenera.
17 “Wachnegi wachni: “‘Mad wangʼa pongʼ gi pi wangʼ otieno gi odiechiengʼ ma ok rum; ne nyara mangili, joga, osewinjo lit mar adhola, gi hinyruok mapek.
“Awuze mawu awa: “‘Maso anga akugwetsa misozi kosalekeza usana ndi usiku; chifukwa anthu anga okondedwa apwetekeka kwambiri, akanthidwa kwambiri.
18 Ka adhi e pinyno, aneno jogo monegi gi ligangla; ka adhi e dala maduongʼ, to aneno masiche ma kech okelo. Janabi kaachiel gi jadolo osedhi e piny ma ok gingʼeyo.’”
Ndikapita kuthengo, ndikuona amene aphedwa ndi lupanga; ndikapita mu mzinda, ndikuona amene asakazidwa ndi njala. Ngakhale aneneri pamodzi ndi ansembe onse atengedwa.’”
19 Bende isekwedo Juda chuth? Dibed ni ichayo Sayun? Angʼo momiyo isehinyowa ma ok wanyal chango? Ne wageno kwe to onge ber mosebiro, kinde mar chang to nitie mana thagruok.
Kodi anthu a ku Yuda mwawakana kwathunthu? Kodi mtima wanu wanyansidwa nawo anthu a ku Ziyoni? Chifukwa chiyani mwatikantha chotere kuti sitingathenso kuchira? Ife tinayembekezera mtendere koma palibe chabwino chomwe chabwera, tinayembekezera kuchira koma panali kuopsezedwa kokhakokha.
20 Yaye Jehova Nyasaye, wayie gi timbewa mamono kod ketho mag wuonewa; adiera wasetimoni richo.
Inu Yehova, ife tikuvomereza kuyipa kwathu ndiponso kulakwa kwa makolo athu; ndithu ife tinakuchimwiranidi.
21 Ne kuom nyingi kik ijarwa; kik ijwangʼ kom duongʼ mari malich. Par singruok mari kodwa kendo kik ikethe.
Musatikane kuopa kuti dzina lanu linganyozedwe; musanyoze mpando wanu waufumu waulemerero. Kumbukirani pangano lanu ndi ife ndipo musachiphwanye.
22 Bende nyiseche manono maonge tich mar ogendini bende nyalo kelo koth? Bende boche kendgi kelo ngʼidho? Ooyo, en in, yaye Jehova Nyasaye ma Nyasachwa. Emomiyo genowa ni kuomi, nimar in ema itimo magi duto.
Mwa milungu yachabechabe ya anthu a mitundu ina, kodi pali mulungu amene angagwetse mvula? Ife chikhulupiriro chathu chili pa Inu, popeza Inu nokha ndinu Yehova Mulungu wathu amene mukhoza kuchita zimenezi.

< Jeremia 14 >