< Jeremia 13 >

1 Ma e gima Jehova Nyasaye nowachona: “Dhi kendo ingʼiew kamba mar law kendo itweye e nungoni, to kik iweye omak pi.”
Yehova anandiwuza kuti, “Pita kagule lamba wansalu yosalala ndipo ukavale mʼchiwuno mwako, koma usakamuviyike mʼmadzi.”
2 Omiyo nangʼiewo kamba, kaka Jehova Nyasaye nochika, mi atweye e nungona.
Choncho ndinakagula lambayo, monga momwe anandiwuzira Yehova, ndipo ndinamanga mʼchiwuno mwanga.
3 Wach Jehova Nyasaye nobirona kendo mar ariyo:
Kenaka Yehova anandiyankhulanso kachiwiri kuti,
4 “Kaw kamba mane ingʼiewo kendo itweyo e nungoni, kendo idhi Perath mi ipande kanyo e bur manie kind lwanda.”
“Tenga lamba amene unagula ndi kuvala mʼchiwuno mwako uja. Tsono pita ku mtsinje wa Yufurate ndipo ukamubise lambayo mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.”
5 Omiyo ne adhi mi apande Perath, mana kaka Jehova Nyasaye nonyisa.
Ndipo ndinapitadi ndi kukabisa lambayo ku Yufurate, monga anenera Yehova.
6 Bangʼ ndalo mangʼeny Jehova Nyasaye nowachona niya, “Dhi sani Perath kendo ikaw kamba mane anyisi ni ipand kanyo.”
Patapita masiku ambiri Yehova anandiwuzanso kuti, “Pitanso ku Yufurate ndipo ukatenge lamba amene ndinakuwuza kuti ukamubise kumeneko.”
7 Omiyo ne adhi Perath mi akunyo kambano kendo akawe kama ne apande, makmana nosekethore kendo obedo maonge tich chuth.
Choncho ndinapita ku Yufurate kukafukula lambayo ndi kumuchotsa pamalo pamene ndinamubisa, koma nthawi imeneyi nʼkuti lambayo atawonongeka kotheratu ndipo analibenso ntchito.
8 Eka wach Jehova Nyasaye nobirona:
Pamenepo Yehova anandiwuza kuti,
9 “Ma e gima Jehova Nyasaye wacho: ‘Anatiek sunga mar Juda kod sunga malich mar Jerusalem mana e yo machalre kamano.
“Izi ndi zimene ine ndikunena: ‘Umu ndi mmene ndidzawonongere zimene akunyadira kwambiri a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
10 Joma timbegi mono gi, motamore winjo wechega, matimo gima chunygi ema ohero, ma bende luwo bangʼ nyiseche manono mondo gitine kendo gilamgi, biro chalo gi kambani makoro onge tich chuth!’
Anthuwa ndi oyipa. Iwo akana kumvera mawu anga. Mʼmalo mwake amawumirira kutsata milungu ina, kuyitumikira ndi kuyipembedza. Anthu amenewa adzakhala ngati lamba wopanda ntchitoyu.
11 Jehova Nyasaye owacho niya, ‘Nimar kaka okanda itweyo e nungo dhano, omiyo ne atweyo od Israel duto kod od Juda duto kuoma, mondo gibed joga miluongo gi nyinga, ma kelona pak kod duongʼ. To kata kamano negitamore winja.’
Monga momwe lamba amakanirira mʼchiwuno cha munthu, momwemonso ndinakonza kuti nyumba yonse ya Israeli ndi nyumba yonse ya Yuda indikangamire Ine kuti akhale anthu anga, kuti azitamanda dzina langa ndi kulemekeza Ine. Koma iwo sanamvere,’ akutero Yehova.
12 “Wachnegi ni: ‘Ma e gima Jehova Nyasaye, ma Nyasach Israel, wacho: Ndede duto mag divai onego opongʼ gi divai.’ To kagiwacho ni, ‘Donge wangʼeyo ni ndede mag divai onego pongʼ gi divai?’
“Awuze anthuwo kuti, ‘Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Mtsuko uliwonse adzawudzaza ndi vinyo.’ Ndipo ngati iwo anena kwa iwe kuti, ‘Kodi ngati ife sitikudziwa kuti mtsuko uliwonse udzadzazidwa ndi vinyo?’
13 To nyisgi ni, ‘Ma e gima Jehova Nyasaye wacho: Anami ji duto modak e pinyni njawre gi mer, kaachiel gi ruodhi mobet e kom duongʼ mar Daudi, jodolo, jonabi kod jogo duto modak Jerusalem.
Tsono iwe uwawuze kuti, Yehova akuti ‘Ine ndidzaledzeretsa anthu onse okhala mʼdziko muno, kuyambira mafumu amene amakhala pa mpando waufumu wa Davide, ansembe, aneneri, pamodzi ndi anthu onse amene akukhala mu Yerusalemu.
14 Jehova Nyasaye owacho niya, Anami ji duto tuomre ngʼato gi ngʼato, wuone kod yawuotgi machalre. Kechna gi herana kod ngʼwonona ok nomona tiekogi.’”
Ndidzawagundanitsa mitu kuti aphwanyane okhaokha ngati mitsuko, makolo ndi ana awo, akutero Yehova. Sindidzawamvera chisoni kapena kuwachitira chifundo kapena kukhudzidwa nawo kuti ndileke kuwawononga.’”
15 Winji kendo ichik iti, kik ibed jangʼayi, nimar Jehova Nyasaye osewuoyo.
Imvani inu Aisraeli ndipo tcherani khutu, musadzitukumule, pakuti ndi Yehova amene akuyankhula.
16 Mi Jehova Nyasaye, ma Nyasachi duongʼ ka pod ok okelo mudho, kapok tiendeni ochwanyore, e gode matindo motimo mudho. Ugombo ler, to enoloke mudho mandiwa mi oloke kuyo malich.
Lemekezani Yehova Mulungu wanu asanagwetse mdima, mapazi anu asanayambe kupunthwa mʼchisisira chamʼmapiri. Asanasandutse kuwala mukuyembekezerako kukhala mdima wandiweyani.
17 To ka ok uchiko itu, anaywagi apanda nikech sunga magu; wengena noywagi malit, ka gipongʼ gi pi wangʼ, nikech rombe mag Jehova Nyasaye noter e twech.
Koma ngati simumvera, ndidzalira kwambiri chifukwa cha kunyada kwanu. Mʼmaso mwanga mwadzaza ndi misozi yowawa chifukwa nkhosa za Yehova zatengedwa ukapolo.
18 Wachne ruoth kod min ruoth niya, “Loruru uaye kombeu mag duongʼ, nimar osimbo mau mag duongʼ nolwar koa e wiyeu.”
Uza mfumu pamodzi ndi amayi ake kuti, “Tsikani pa mipando yaufumuyo, pakuti zipewa zanu zaufumu zokongolazo zagwa pansi.”
19 Mier madongo man Negev nolor, kendo onge ngʼama noyawgi. Juda duto noter e twech, notergi mabor chuth.
Mizinda ya ku Negevi yatsekedwa ndipo palibe wina woti nʼkuyitsekula. Yuda yense watengedwa kupita ku ukapolo, watengedwa yense ukapolo.
20 Tingʼuru wangʼu malo kendo une joma aa yo nyandwat. Ere kweth mane oket e lwetu, rombe mane usungorugo?
Tukula maso ako kuti uwone amene akubwera kuchokera kumpoto. Kodi nkhosa zimene anakusungitsa zili kuti, nkhosa zanu zokongola zija?
21 Unuwach angʼo ka Jehova Nyasaye oketo ewiu, jogo mane uparo ni osiepeu kaka jotendu? Donge rem nokayi kaka dhako mamuoch kayo?
Kodi udzanena chiyani pamene [Yehova] adzakuyikira anthu amene unkanena kuti ndi abale ako akukugonjetsa ndi kukulamulira? Kodi sudzamva zowawa ngati za mayi pa nthawi yake yochira?
22 Kendo ka ipenjori iwuon, “Angʼo momiyo ma osetimorena?” En nikech richo mau mangʼeny omiyo dugu oseneno kendo dendu osekethore.
Ndipo ngati udzadzifunsa kuti, “Kodi zimenezi zandichitikira chifukwa chiyani?” Ndi chifukwa cha machimo anu ambiri kuti zovala zanu zingʼambike ndiponso kuti akuchitireni nkhanza.
23 Bende ja-Kush nyalo loko kit piene kata kwach nyalo loko kido man kuome? Kamano bende ok inyal timo maber, in ngʼatno mongʼiyo gi timbe maricho.
Kodi wa dziko la Kusi nʼkusintha khungu lake, kapena kambuku kusintha mawanga ake? Inunso amene munazolowera kuchita zoyipa simungathe kusintha.
24 “Anakeu ka mihudhwe miriembo gi yamb kalausi.
“Ine ndidzakumwazani ngati mankhusu amene amawuluka ndi mphepo ya ku chipululu.
25 Ma e pokni ma asechiwoni,” Jehova Nyasaye ema owacho, “nikech wiu osewil koda kendo useketo genou kuom nyiseche manono.
Limeneli ndiye gawo lanu, chilango chimene ndakukonzerani chifukwa chondiyiwala Ine ndi kutumikira milungu yabodza, akutero Yehova.
26 Anaelu duge mi aum wengeu mondo omi wichkuot mau onere,
Ine ndidzakwinya zovala zanu mpaka ku maso kuti umaliseche wanu uwonekere.
27 kaka terruok mau kod gombo mau mandhaga, kod chode mau maonge wichkuot! Aseneno timbeu mamono ewi gode matindo kod e pewe. Mano kaka nine malit, yaye Jerusalem! Nyaka karangʼo mibiro bedo mochido?”
Ndaona zonyansa zanu: zigololo zanu, kutchetcherera kwanu ndi ziwerewere zanu, zochitika pa mapiri ndi mʼminda. Tsoka iwe Yerusalemu! Udzakhala wosayeretsedwa pa zachipembedzo mpaka liti?”

< Jeremia 13 >