< Jeremia 10 >

1 Winji gima Jehova Nyasaye wachoni, yaye od Israel.
Inu Aisraeli, imvani zimene Yehova akunena.
2 Ma e gima Jehova Nyasaye wacho: “Kik ipuonjri yore ogendini kata ibed gi bwok gi ranyisi manie kor polo, kata obedo ni gibwogo ogendini.
Yehova akuti, “Musatsatire makhalidwe a anthu a mitundu ina kapena kuchita mantha ndi zizindikiro zamlengalenga, ngakhale anthu a mitundu ina amachita nazo mantha.
3 Nimar kit jogi kod timbegi onge tiende; gingʼado yien koa e bungu, bangʼe japecho paye gi koyo mare.
Pakuti miyambo ya mitundu inayo ndiyachabechabe. Iwo amakadula mtengo ku nkhalango ndipo mmisiri amawusema ndi sompho.
4 Giwire gi fedha gi dhahabu; giriwe motegno gi musmal ka gigoye gi nyundo, mondo kik oyiengni.
Amakongoletsa chosemacho ndi siliva ndi golide; kenaka amachikhomerera ndi misomali kuti chisagwedezeke.
5 Mana kaka gima ibwogogo gik moko e puothe mag budho, e kaka nyisechegi manonogo ok nyal wuoyo; nyaka tingʼ-gi nikech ok ginyal wuotho. Kik uluorgi; ok ginyal hinyou kata timonu gima ber.”
Mafano awo ali ngati mtengo wakanjedza woopsezera mbalame mʼmunda wa minkhaka. Mafanowo sangathe nʼkuyankhula komwe ndipo ayenera kunyamulidwa popeza sangathe nʼkuyenda komwe. Musachite nawo mantha popeza sangathe kukuchitani choyipa ndiponso alibe mphamvu yochitira chabwino chilichonse.”
6 Onge ngʼama chalo kodi, yaye Jehova Nyasaye; iduongʼ, kendo nyingi maratego nigi teko.
Palibe wofanana nanu, Inu Yehova; Inu ndinu wamkulu, ndipo dzina lanu lili ndi mphamvu yayikulu.
7 En ngʼa ma ok onego miyi luor, yaye Ruodh ogendini? Ma gima iwinjori godo. Kuom jorieko duto mag ogendini kod kuom pinjeruodhigi duto, onge ngʼama chalo kodi.
Ndani amene angaleke kukuopani, inu Mfumu ya mitundu ya anthu? Chimenechi ndicho chokuyenerani. Pakati pa anthu anzeru onse komanso mafumu onse a mitundu ya anthu, palibe wina wofanana nanu.
8 Giduto gionge paro kendo gifuwo; ipuonjogi gi nyiseche manono mag bepe mopa maonge tich.
Onsewo ndi opusa ndi opanda nzeru; malangizo awo amawatenga kuchokera kwa mafano achabechabe opanga ndi mitengo.
9 Fedha mothedhi ikelo koa Tarshish kendo dhahabu koa Ufaz. Gima japecho kod jatheth oseloso irwako gi lewni marambulu gi maralik, giduto olosgi gi jotich molony.
Siliva wosula amabwera naye kuchokera ku Tarisisi ndipo golide amachokera naye ku Ufazi. Mafanowo ndi ntchito ya anthu aluso ndi odziwa kuzokota golide. Tsono mafanowo amawaveka zovala za mtundu wamtambo ndi pepo. Yonseyo ndi ntchito ya anthu a luso.
10 To Jehova Nyasaye e Nyasaye madieri; en e Nyasaye mangima, Ruoth manyaka chiengʼ. Ka iye owangʼ, to piny tetni; ogendini ok nyal mirimbe.
Koma Yehova ndiye Mulungu woona; Iyeyo ndiye Mulungu wamoyo, Mfumu yamuyaya. Akakwiya, dziko limagwedezeka; anthu a mitundu ina sangathe kupirira ukali wakewo.
11 “Nyisgi ma: ‘Nyiseche manonogi, mane ok ochweyo polo gi piny, nolal nono e piny kendo e bwo polo.’”
“Awuze anthu awa kuti, ‘Milungu iyi, imene sinalenge dziko lakumwamba ndi dziko lapansi, idzawonongeka pa dziko lapansi ndi pansi pa thambo.’”
12 To Nyasaye nochweyo piny gi tekone; ne ochako piny gi riekone, kendo oyaro polo gi ngʼeyo mare.
Koma Mulungu analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake; Iye anapanga dziko lonse ndi nzeru zake ndipo anayala thambo mwaluso lake.
13 Ka omor ka polo, to pige manie polo wuo; omiyo boche polo dhwolore koa e giko piny. Ooro mil polo gi koth kendo okelo yamo koa e kuondege mag keno.
Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba; Iyeyo amabweretsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Amabweretsa mphenzi pamodzi ndi mvula ndi kutulutsa mphepo yamkuntho kumalo kumene osungirako.
14 Ji duto parogi ok ti kendo gionge ngʼeyo; jotheth duto wigi kuot gi nyisechegi manono ma githedho. Kido mage moloso gin gik manono; gionge muya eigi.
Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru; mmisiri aliyense wosula golide akuchita manyazi ndi mafano ake. Mafano akewo ndi abodza; alibe moyo mʼkati mwawo.
15 Gionge tich, gin gik minyiero; ka ndalogi mar ngʼado bura ochopo, to ginilal nono.
Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo. Pamene anthuwo azidzaweruzidwa, mafanowo adzawonongedwa.
16 Jalno ma en Pok mar Jakobo ok chal kodgi, nimar en e Jachwech mar gik moko duto, nyaka Israel, ma en dhood girkeni mare, Jehova Nyasaye Maratego e nyinge.
Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo. Iyeyu ndi Mlengi wa zinthu zonse kuphatikizapo Israeli, mtundu umene anawusankha kuti ukhale anthu ake. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
17 Chokuru giu duto mondo ua e pinyno, un joma ogengʼnigi.
Sonkhanitsani katundu wanu, inu amene mukukhala mʼlinga la ankhondo.
18 Nimar ma e gima Jehova Nyasaye wacho: “E kindeni machalo kama, abiro daro ji modak e pinyni; anakel sandruok kuomgi mondo mi omakgi.”
Pakuti Yehova akuti, “Tsopano Ine ndidzachotsa anthu onse amene akukhala mʼdziko lino; adzakhala pa mavuto mpaka adzamvetsa.”
19 To mano kaka litna nikech hinyruok mara! Adhonda ok thiedhre! Kata kamano awacho ne an owuon ni, “Ma en twona, kendo nyaka angʼi kode.”
Aliyense ankangoti, “Mayo ine, chifukwa cha kupweteka kwanga! Chilonda changa nʼchachikulu!” Koma ine ndinkaganiza kuti, “Ndithu, ili ndi vuto langa basi, choncho ndingolipirira.”
20 Hemba okethi; tonde mitweyego duto ochodi. Yawuota oweya kendo ok gin koda; onge ngʼama odongʼ manyalo gurona hemba kata gerona kambi.
Tenti yanga yawonongeka, zingwe zake zonse zaduka. Ana anga andisiya ndipo kulibenso. Palibenso amene adzandimangire tenti, kapena kufunyulula nsalu yake.
21 Jokwath onge rieko to bende ok gipenj Jehova Nyasaye wach; mano emomiyo ok gidhi nyime maber kendo rombe mag-gi duto oke.
Abusa ndi opusa ndipo sanapemphe nzeru kwa Yehova; choncho palibe chimene anapindula ndipo nkhosa zawo zonse zabalalika.
22 Chik iti! Wach biro niya, tungni maduongʼ koa e piny man yo nyandwat! Anami dala mag Juda odongʼ nono, kama ondiegi ema odakie.
Tamvani! kukubwera mphekesera, phokoso lalikulu la gulu la a ankhondo likumveka kuchokera kumpoto! Lidzasandutsa bwinja mizinda ya ku Yuda, malo okhala nkhandwe.
23 Angʼeyo, yaye Jehova Nyasaye, ni ngima dhano ok en mare owuon; ok en mar dhano mondo ochik yorene.
Inu Yehova, ndikudziwa kuti moyo umene munthu ali nawo si wake; munthuyo sangathe kuwongolera mayendedwe ake.
24 Rieya, Jehova Nyasaye, to mana gi bura makare ma ok e ich wangʼ, ka ok kamano to ditieka chuth.
Inu Yehova, langizeni, komatu mwachilungamo, osati ndi mkwiyo wanu, mungandiwononge kotheratu.
25 Ol mirimbi kuom ogendini ma ok ongʼeyi, kuom ji ma ok luong nyingi. Nimar gisetieko Jakobo; gisetieke chuth kendo giseketho dalane.
Tsanulirani ukali wanu pa mitundu ya anthu amene sakudziwani, ndiye kuti mitundu ya anthu amene satama pa dzina lanu mopemba. Iwo aja anasakaza Yakobo; amusakaza kotheratu ndipo awononga dziko lake.

< Jeremia 10 >