< Isaya 66 >

1 Ma e gima Jehova Nyasaye wacho: “Polo e koma mar duongʼ, to piny e raten tienda. Koro ere kama dugerna e ot? To kar yweyo mara nobed kanye?
Yehova akuti, “Kumwamba ndi mpando wanga waufumu ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga. Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire, ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
2 Donge lweta ema osechweyo gigi duto momiyo gibedo mangima?” Jehova Nyasaye ema owacho. “Ma e ngʼat ma ayiego ma en ngʼat ma hore kendo man-gi chuny motur, kendo ngʼama oluoro wachna.
Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi, motero zonsezi ndi zanga?” Akutero Yehova. “Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu: amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima, ndipo amamvera mawu anga.
3 To ngʼato angʼata moyangʼo rwath katimogo misango chal gi ngʼat monego dhano, kendo ngʼato angʼata motimo misango mar rombo, chal gi ngʼama oturo ngʼut guok, kendo ngʼato angʼata mochiwo misango mar cham chal gi ngʼat mochiwo remb anguro, bende ngʼato angʼata mowangʼo ubani mangʼwe ngʼar mar rapar, chal gi ngʼama lamo nyiseche manono. Giseyiero yoregi giwegi kendo chunygi mor gi timbegi mag rondogo;
Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna amaphanso munthu, ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa, amaphanso galu. Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya amaperekanso magazi a nkhumba. Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso amapembedzanso fano. Popeza iwo asankha njira zawozawo, ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.
4 omiyo an bende abiro yieronegi masiche mondo omakgi kendo abiro kelo kuomgi gik ma giluoro. Nimar kane aluongo, to onge ngʼat mane odwoka, kendo kane awuoyo, to onge ngʼat mane owinjo. Negitimo timbe mamono e nyima, kendo ne giyiero mana gik mamorogi.”
Inenso ndawasankhira chilango chowawa ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija. Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha, pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu. Anachita zoyipa pamaso panga ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”
5 Winjuru wach Jehova Nyasaye, un jogo matetni kuwinjo dwonde: “Oweteni mochai kendo ok kwani ka gimoro nikech ihero nyinga osewacho niya, ‘Mad Jehova Nyasaye mi duongʼ, mondo omi wane morni!’ Kata kamano gin giwegi ema ginine wichkuot.
Imvani mawu a Yehova, inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake: “Abale anu amene amakudani, ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti, ‘Yehova alemekezeke kuti ife tione chimwemwe chanu!’ Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.
6 Winjuru kaka nduru wuok e dala maduongʼ, kendo winjuru kaka kokono wuok e hekalu! Ma en dwond Jehova Nyasaye kochulogo kuor ne wasike moromo gi timbegi.
Imvani mfuwu mu mzinda, imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu! Limenelo ndi liwu la Yehova, kulanga adani ake onse.
7 “Kapok muoch ochako kaye, to osenywolo nyathi; kapok owinjo rem to osenywolo wuowi.
“Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa wachira kale; asanayambe kumva ululu, wabala kale mwana wamwamuna.
8 En ngʼa mosewinjo wach machal kamano? En ngʼa moseneno gik machalo kamano? Bende piny dichwe godiechiengʼ achiel koso ogendini dichok dichiel? To mana e seche mane muoch ochako kayo Sayun ema nonywoloe nyithinde.
Ndani anamvapo zinthu zoterezi? Ndani anazionapo zinthu zoterezi? Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi, kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi? Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa nthawi yomweyo anabereka ana ake.
9 Bende dawe sa ma dhako nywolie chopi mak amiye teko mar nywol?” Jehova Nyasaye owacho. “Bende dadin ich kochopo sa mar chiwo nyathi?” Nyasachi owacho.
Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira, koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova. “Kodi ndingatseke mimba pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.
10 “Moruru gi Jerusalem kendo bed mamor kode, un duto muhere; beduru gi ilo maduongʼ, un duto man-gi kuyo nikech en.
“Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye, inu nonse amene mumakonda Yerusalemu, kondwera nayeni kwambiri, nonse amene mumamulira.
11 Nimar ibiro piru maber kudhodho thunde; kendo unumethi gi ilo mi ubed gi mor mogundho.”
Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri wa mʼmawere a chitonthozo chake.”
12 Nimar ma e gima Jehova Nyasaye wacho: “Abiro miyo kwe ma en-go mol ka aora kendo mwandu mag pinje namiye mamol ka oula; unubed mamor ka odhodhou kotingʼou e bade kendo kopirou e chonge.
Yehova akuti, “Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi, ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira. Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa, kapena kumufungata pa miyendo yake.
13 Mana kaka miyo hoyo nyathine, e kaka abiro hoyou; kendo noho chunyu e Jerusalem.”
Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo, moteronso Ine ndidzakusangalatsani; ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”
14 Ka uneno ma, to chunyu nobed gi mor, kendo dendu nobed maber mana ka lum matwi ndalo chwiri; lwet Jehova Nyasaye nofwenyre ne jotichne, to mirimbe to none kuom wasike.
Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu. Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu. Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira ndi kuti ndimakwiyira adani anga.
15 To nee, Jehova Nyasaye biro gi mach, kendo gechene mag lweny chalo ka kalausi; obiro kelo mirimbe makakni, kendo chwat mare nopilre ka mach.
Taonani, Yehova akubwera ngati moto, ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu; Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake ndi malawi amoto.
16 Nimar mach kod ligangla ema Jehova Nyasaye noyalgo ji duto, kendo joma Jehova Nyasaye nonegi nobed mangʼeny.
Pakuti Yehova adzalanga anthu onse ndi moto ndi lupanga, Yehova adzapha anthu ambiri.
17 Jehova Nyasaye wacho niya, “Joma pwodhore kendo bedo maler mondo odhiye puothe, kamoro ka moro luwo wadgi kendo chamo ring anguro, oyieyo kod gik moko duto makwero norum duto dichiel.
Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”
18 “An Jehova Nyasaye angʼeyo timbeni gi paroni achiegni biro mondo achok ogendini duto kod dhoudi mawacho dhok mopogore opogore kendo ginibi mi ginine duongʼ mara maler.
“Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.
19 “Anatim ranyisi e kindgi kendo anaor jomoko manok ma notony mane pok owinjo humba kata mane pok oneno duongʼ mara maler ma gin: Tarshish, Libya, Lud (mongʼere gi nying mar jolweny mongʼeyo kedo gi asere), jo-Tubal kod jo-Yunani kaachiel gi joma odak e dho nembe man kuonde maboyo. Gibiro nyiso duongʼna e kind ogendini.
“Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina.
20 Kendo ginikel oweteni duto koa e ogendini duto, e goda maler ma en Jerusalem kaka gir misango ne Jehova Nyasaye ka moko oidho farese, geche lweny, pundane kod ngamia,” Jehova Nyasaye owacho. “Gibiro kelogi mana kaka jo-Israel kelo misengini e od Jehova Nyasaye, ka gitingʼogi e tewni maler.
Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo.
21 Kendo moko kuomgi bende nayier mondo obed jodolo kod jo-Lawi,” Jehova Nyasaye owacho.
Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.
22 Jehova Nyasaye wacho niya, “Mana kaka polo manyien machweyo gi piny manyien nosiki e nyima, e kaka nyingi kod nying nyikwayi nosiki.
“Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova.
23 Mana kaka dwe por kendo podho kendo machielo por, bende mana kaka chiengʼ Sabato nyaka chiengʼ Sabato machielo e kaka ji duto biro bedo kendo kulore e nyima,” Jehova Nyasaye owacho.
“Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova.
24 “Giniwuogi mi gine ringre joma otho mosepiem koda, kudni machamogi ok notho kata mach mawangʼogi ok notho kendo ginibed gik ma piny ngima ojokgo.”
“Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”

< Isaya 66 >