< Isaya 53 >

1 En ngʼa moseyie wach ma walando, koso en ngʼa ma Jehova Nyasaye osenyiso tekone?
Ndani wakhulupirira zimene tanenazi; kapena ndani amene Yehova wamuzindikiritsa mphamvu zake?
2 Nodongo e nyime mana ka chuny yath mayom matwi; kendo mana ka tiend yath madongo kaa e lowo motwo. Ne oonge gi chia kata duongʼ moro mane nyalo lombo wangʼwa kuome, kendo onge gima ne nenore kuome maber mane nyalo miyo wahere.
Iye anakula ngati mphukira pamaso pake, ndiponso ngati muzu mʼnthaka yowuma. Iye analibe thupi labwino kapena nkhope yokongola yoti ife nʼkumamuchewukira, analibe maonekedwe woti ife nʼkumamukhumbira.
3 Ne ojare mokwede gi oganda, en ngʼat mane neno chandruok mangʼeny, kendo mosiko kawinjo rem. Ji nojare kendo wan bende ne ok wamiye luor, mana ka ngʼama ok dwar neno.
Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu, munthu amene moyo wake unali wamasautso, wozolowera zowawa, ndipo anali ngati munthu amene anzake amaphimba nkhope zawo akamuona. Iye ananyozedwa, ndipo ife sitinamuyese kanthu.
4 Adier, notingʼo sandruok-wa kendo chandruokwa ema ne ture, kata kamano wan to ne waparo ni kum mane oyudo, sandruok kod chandruok noa kuom Nyasaye.
Ndithudi, iye anamva zowawa mʼmalo mwa ife; ndipo anasautsidwa mʼmalo mwathu. Koma ife tinkaganiza kuti ndi Mulungu amene akumulanga, kumukantha ndi kumusautsa.
5 To kare ne ochwowe mana nikech kethowa, nosande malit nikech richowa; kum mane oyudo kuome ema nokelnwa kwe, kendo moriemo mage ema nochangowa.
Koma iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu, ndipo anamuzunza chifukwa cha zoyipa zathu; iye analangidwa kuti ife tikhale ndi mtendere, ndipo ndi mabala ake ife tinachiritsidwa.
6 Wan duto, waselal mana ka rombe, ka ngʼato ochomo mana yore owuon; kendo Jehova Nyasaye oseketo kuome richowa duto.
Ife tonse, ngati nkhosa, tasochera, aliyense mwa ife akungodziyendera; ndipo Yehova wamusenzetsa zoyipa zathu zonse.
7 Nosande kichwade malit to ne ok otingʼo dhoge; notere kar thone mana ka rombo mitero kar yengʼo, kendo nolingʼ ka rombo manie lwet joma ngʼado yiere, omiyo en bende ne ok otingʼo dhoge.
Anthu anamuzunza ndi kumusautsa, koma sanayankhule kanthu. Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira, kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta, momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.
8 Ne oyale angʼaya kendo nongʼadne bura molal kode. To en ngʼa manyalo wuoyo kuom gunde? Nimar nogole e piny joma ngima, kendo nolal kode nikech richo mag jowa.
Atatha kumugwira mwankhanza ndikumuyimba mlandu, kenaka anapita naye kukamupha. Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake, poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo? Ndani anaganizirapo poona kuti iye anakanthidwa chifukwa cha zolakwa za anthu anga?
9 Ne okete e bur e kind joricho kendo gi jo-mwandu e thone, kata obedo ni ne ok otimo tim mahundu moro amora bende miriambo nine ok owuok e dhoge.
Anamukonzera manda ake pamodzi ndi anthu oyipa ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi anthu achuma, ngakhale kuti iye sanachite za chiwawa, kapena kuyankhula za chinyengo.
10 To kata kamano ne en dwaro Jehova Nyasaye mondo sande malit koyudo chandruok, kendo Jehova Nyasaye nochiwo ngimane mondo obed misango mar pwodhruok e ketho, to enone nyikwaye kendo omedne ndalo, kendo dwaro mar Nyasaye nochop kare nikech en.
Komatu ndi Yehova amene anafuna kuti amuzunze ndi kumusautsa. Yehova anapereka moyo wa mtumiki wake kuti ukhale nsembe yoperekedwa chifukwa cha zolakwa. Tsono iye adzaona zidzukulu zake ndipo adzakhala ndi moyo wautali, ndipo chifuniro cha Yehova chidzachitika mwa iye.
11 Bangʼ chandruokne duto enone ler mar ngima kendo noyud mor e chunye; kuom riekone, jatichna makare nongʼad bura makare ne ji mangʼeny kendo notingʼ richogi.
Atatha mazunzo a moyo wake, adzaona kuwala, ndipo adzakhutira. Mwa nzeru zake mtumiki wanga wolungamayo adzalungamitsa anthu ambiri, popeza adzasenza zolakwa zawo.
12 Kuom mano abiro miye pok e kind thuondi kendo enopog gik moyaki gi rateke, nikech ne ochiwo ngimane nyaka tho mine okwane kod joketho. Nimar notingʼo richo ji mangʼeny kendo nochungʼ kar joricho e nyim Nyasaye.
Motero Ine ndidzamupatsa ulemu pamodzi ndi akuluakulu, adzagawana zofunkha ndi ankhondo amphamvu, popeza anapereka moyo wake mpaka kufa, ndipo anamuyika mʼgulu la anthu olakwa kuti akhululukidwe. Pakuti iye anasenza machimo a anthu ambiri, ndipo anawapempherera anthu olakwa.

< Isaya 53 >