< Isaya 34 >

1 Suduru machiegni, un ogendini kendo chikuru itu; winjuru, un ogendini! Mad piny kod gik moko manie iye winja!
Inu anthu a mitundu yonse, bwerani pafupi kuti mumve: tcherani khutu, inu anthu a mitundu ina yonse: Limvetsere dziko lapansi pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse pamodzi ndi zonse zochokera mʼmenemo!
2 Jehova Nyasaye nigi ich wangʼ kod ogendini duto; mirimbe ochomo jolweny mag-gi duto. Obiro tiekogi duto, mi nochiwgi mondo otiekgi.
Yehova wayipidwa ndi anthu a mitundu yonse; wapsera mtima magulu awo onse ankhondo. Iye adzawawononga kotheratu, nawapereka kuti aphedwe.
3 Jogi monegi nowit oko, mi ringregi nodungʼ kendo rembgi nopongʼ gode.
Anthu awo ophedwa adzatayidwa kunja, mitembo yawo idzawola ndi kununkha; mapiri adzafiira ndi magazi awo.
4 Sulwe duto manie polo noleny nono, polo noban mana ka kalatas, gik moko duto manie polo malo nolwar, mana ka it mzabibu moner, kata ka olemb ngʼowu ma kundi ochwowo.
Dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zidzasungunuka ndipo mlengalenga mudzakulungidwa ngati chipepala; nyenyezi zonse zidzayoyoka ngati masamba ofota a mphesa, ngati masamba onyala a mtengo wa mkuyu.
5 Liganglana osetieko tichne e kor lwasi, neuru, olor mondo ongʼad bura ne Edom, oganda ma asetieko chuth.
Yehova akuti, “Lupanga langa lakhutiratu magazi kumwamba; taonani, likutsika kudzalanga anthu a ku Edomu, anthu amene ndawawononga kotheratu.”
6 Ligangla mar Jehova Nyasaye opongʼ gi remo, kendo boche ogawore kuome ma gin, remb rombe kod diek, kaachiel gi boche moa e nyiroke mag imbe. Nimar Jehova Nyasaye nigi misango Bozra kod nek ei Edom.
Lupanga la Yehova lakhuta magazi, lakutidwa ndi mafuta; magazi a ana ankhosa onenepa ndi ambuzi, mafuta a ku impsyo za nkhosa zazimuna. Pakuti Yehova ali ndi nsembe mu Bozira ndiko kuphedwa kwa anthu ambiri mʼdziko la Edomu.
7 Kendo jope, gi nyirwedhi kod rwedhi madongo nopodh kodgi. Pinygi nopongʼ gi remo, kendo boche noum buru.
Pamodzi ndi anthuwo zidzaphedwanso njati, ngʼombe zazimuna zazingʼono ndi zazikulu zomwe. Dziko lawo lidzakhala magazi okhaokha, ndipo nthaka idzakutidwa ndi mafuta.
8 Nimar Jehova Nyasaye ni kod odiechienge mar chulo kuor, ma en higa mar chiwo kum ne jogo, mosetimo marach ne Sayun.
Iyi ndi nthawi imene Yehova adzalipsira ndi kulanga adani a Ziyoni.
9 Aore mag Edom nobar okak, lopene nolokre lot maliet mawengʼo, kendo pinye nowangʼ duto!
Madzi a mʼmitsinje ya Edomu adzasanduka phula, ndipo fumbi lake lidzasanduka sulufule; dziko lake lidzasanduka phula lamoto!
10 Ok nokwe odiechiengʼ gotieno; iro mare nodum kanyo nyaka chiengʼ. Koa e tiengʼ moro nyaka machielo nodongʼ gunda; onge ngʼat manochak oluwe kendo.
Motowo sudzazimitsidwa usiku ndi usana; utsi wake udzafuka kosalekeza. Dzikolo lidzakhala chipululu pa mibado ndi mibado; palibe ndi mmodzi yemwe amene adzadutsemo.
11 Nobed kama winj tula rutoe kendo agak odakie. Nyasaye nopim timbe maricho mag Edom kod ketho mage.
Mʼdzikomo mudzakhala akabawi ndi anungu; amantchichi ndi akhwangwala adzapanga zisa zawo mʼmenemo. Mulungu adzatambalitsa pa Edomu chingwe choyezera cha chisokonezo ndi chingwe chowongolera cha chiwonongeko.
12 Jodonge ok nobed gi gimoro miluongo ni pinyruoth, nyithi ruoth nolal nono.
Anthu olemekezeka ake sadzatchedwanso mfumu kumeneko; akalonga ake onse adzachotsedwa.
13 Kuthe ema noyugno e utege madongo, aila kod pedo nobed ohingane. Enobed piny mojwangʼ ma ondiegi ema odakie kendo kuonde ma tula odakie.
Minga idzamera mʼnyumba zake zankhondo zotetezedwa, khwisa ndi mitungwi zidzamera mʼmalinga ake. Ankhandwe azidzadya mʼmenemo; malo okhalamo akadzidzi.
14 Gi bungu norom gondiegi kuno, kendo diek mag bungu noywagne jowetegi; kanyo bende gik malich mag otieno noyud kar yweyo.
Avumbwe adzakumana ndi afisi, ndipo zirombo za mʼchipululu zizidzayitanizana. Kumeneko kudzafikanso mizimu yoyipa ndi kupeza malo opumulirako.
15 Tula noger ode kanyo monywol tongʼ, motogi kendo norit nyithinde, koumo e tipo mar bwombene; kanyo bende ema otenga nochokre, moro ka moro gi nyawadgi.
Kadzidzi adzamangako chisa chake nʼkuyikirako mazira, adzaswa ana ake ndi kusamalira ana ake mu mthunzi wa mapiko ake; akamtema adzasonkhananso kumeneko, awiriawiri.
16 Ngʼii e kitap Jehova Nyasaye kendo isom: Onge moro kuomgi kata achiel manobed maonge, kendo moro ka moro nobed gi nyawadgi. Nimar osegolo chik gi dhoge owuon, kendo Roho mare ema nochokgi kanyakla.
Funafunani mʼbuku la Yehova ndi kuwerenga: mwa zolengedwazi palibe chimene chidzasowa; sipadzakhala nʼchimodzi chomwe chopanda chinzake. Pakuti Yehova walamula kuti zitero, ndipo Mzimu wake udzawasonkhanitsa pamodzi.
17 Opogogi kuondegi; kendo lwetene chiwogi gi rapim. Enobed margi nyaka chiengʼ mi gidag kanyo ndalo duto mag ngimagi.
Yehova wagawa dziko lawo; wapatsa chilichonse chigawo chake. Dziko lidzakhala lawo mpaka muyaya ndipo zidzakhala mʼmenemo pa mibado yonse.

< Isaya 34 >