< Isaya 21 >

1 Wach mokor kuom piny Ongoro manie dho Nam: Mana kaka kalausi mager kudho koluwo piny man yo milambo, e kaka joma monjou biro wuok e piny motwo, piny masira.
Uthenga wonena za chipululu cha mʼmbali mwa Nyanja. Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya adzabwera ngati kamvuluvulu amene akuwomba modutsa mʼmbali ya nyanja, kuchokera ku chipululu, dziko lochititsa mantha.
2 Fweny malich osenyisa ni: Jandhoko biro ndhoko, to jayeko biro yeko. Elam mondo omonje! Media mondo olwore koni gi koni! Abiro tieko lit duto mane okelo.
Ine ndaona zinthu zoopsa mʼmasomphenya: Wonyenga akunyenga, wofunkha akufunkha komanso owononga akuwononga. Elamu, yambani nkhondo! Mediya, zingani mzinda! Ine ndidzathetsa mavuto onse amene anayambitsa Ababuloni.
3 Kaneno magi to apuodora ka rem rama e ringra, rem rama mana ka dhako mamuoch kayo; kibaji goya kuom gik mawinjo kendo midhiero omaka kuom gik ma aneno.
Chifukwa cha zimenezi thupi langa likunjenjemera ndi mantha, ndikumva ululu ngati wa mayi amene akubereka; ndikuvutika kwambiri ndi zimene ndikumva, ndathedwa nzeru ndi zimene ndikuziona.
4 Chunya bwok, denda tetni nikech luoro; gombo ma an-go mondo piny imre oselokorena masira.
Mtima wanga ukugunda, ndipo ndikunjenjemera ndi mantha; chisisira chimene ndakhala ndikuchifuna chasanduka chinthu choopsa kwa ine.
5 Negiiko mesa mondo gimethi kendo gichiem, to apoya nono negipo kinyisogi, ni mondo giik gigegi mag lweny.
Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya akukonza matebulo, akuyala mphasa, akudya komanso kumwa! Mwadzidzidzi anamva mawu akuti, “Dzukani inu ankhondo, pakani mafuta zishango zanu!”
6 Ruoth Nyasaye wachona niya, “Dhiyo mondo iket jangʼicho mondo odwok wach kuom gik moneno.
Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi; “Pita, kayike mlonda kuti azinena zimene akuziona.
7 Ka oneno geche lweny miywayo gi farese, gi joma oidho punde kata ngamia, to oikre kendo obed motangʼ.”
Taonani, anthu akubwera ali pa akavalo ndipo akuyenda awiriawiri, okwera pa bulu kapena okwera pa ngamira, mlondayo akhale tcheru kwambiri.”
8 Kendo jangʼicho nokok niya, “Yaye Ruoth Nyasacha pile ka pile asebedo kar ngʼicho, kendo otieno asiko e kara mar tich.
Ndipo mlondayo anafuwula kuti, “Ambuye anga, tsiku ndi tsiku ndimakhala pa nsanja yolondera; Usiku uliwonse ndimakhala pa malo anga olondera.
9 Ero ngʼato biro koidho gach lweny miywayo gi farese. To ngʼatno nowacho niya, ‘Babulon osepodho, adier osepodho, adier osepodho, kendo nyisechene manono osetur matindo tindo!’”
Taonani, uyo munthu akubwera atakwera pa galeta ali ndi gulu la akavalo. Mmodzi wa iwo akuti, ‘Babuloni wagwa, wagwa! Mafano onse a milungu yake agwa pansi ndipo aphwanyika!’”
10 Yaye ogandana mosenyon piny ka cham midino anyisou gima asewinjo koa kuom Jehova Nyasaye Maratego, ma Nyasach Israel.
Inu anthu anga opunthidwa ndi kupetedwa ngati tirigu, ine ndikukuwuzani zimene ndamva ndikukuwuzani Uthenga wochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli.
11 Wach mokor kuom Duma: Ngʼato obiro ira koa Seir, kendo openja monwore niya, “Jarito odongʼ seche adi mondo piny oru? Jarito odongʼ seche adi mondo piny oru?”
Uthenga wonena za Duma: Munthu wina akundiyitana kuchokera ku Seiri kuti, “Iwe mlonda, usikuwu utha liti? Iwe mlonda, utha liti kodi usikuwu?”
12 Eka jarito nodwoko niya, “Piny chiegni ru, to otieno bende biro chopo. Kidwaro penjo, to penji kendo imed penjo.”
Mlonda akuyankha kuti, “Kukucha, koma kudanso. Ngati ukufuna kufunsa, funsa tsopano; ndipo ubwerenso udzafunse.”
13 Wach mokor kuom jo-Arabu: Un jo-Dedan ma jo-ohala mawuotho ka gi kacha ka bworo e thim jo-Arabu,
Uthenga wonena za Arabiya: Inu anthu amalonda a ku Dedani, amene usiku mumagona mʼzithukuluzi za ku Arabiya,
14 keluru pi ne joma riyo oloyo, to un mudak Tema, keluru chiemo ne joma oseringo ka pondone lweny.
perekani madzi kwa anthu aludzu. Inu anthu a ku Tema perekani chakudya kwa anthu othawa nkhondo.
15 Giseringone ligangla, ne ligangla mowuodhi, ne atungʼ moywa kendo ne lweny mager.
Iwo akuthawa malupanga, lupanga losololedwa, akuthawa uta wokokakoka ndiponso nkhondo yoopsa.
16 Ruoth Nyasaye wachona niya, “Mana kaka ja-otongʼo kwano hike achiel ma tije rumogo e kaka duongʼ mar Kedar norum.
Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi: “Chaka chimodzi chisanathe, potsata mmene amawerengera munthu waganyu, ulemerero wonse wa Kedara udzatheratu.
17 Joma nok ma gin jolweny mag asere ma gin thuondi man Kedar ema notony. Jehova Nyasaye ma en Nyasach Israel osewacho.”
Mwa anthu okoka uta, ankhondo a ku Kedara opulumuka adzakhala owerengeka.” Wayankhula ndi Yehova Mulungu wa Israeli.

< Isaya 21 >