< Isaya 13 >

1 Ma e wach mane Nyasaye onyiso Isaya wuod Amoz e fweny kuom Babulon:
Uthenga onena za Babuloni umene Yesaya mwana wa Amozi anawulandira:
2 Chunguru bandera ewi got motwo kendo gouru koko, gwelgiuru mondo gidonj e dhorangeye joma ogen.
Kwezani mbendera yankhondo pa phiri loti see, muwafuwulire ankhondo; muwakodole kuti adzalowe pa zipata za anthu olemekezeka.
3 Asegolo chik ne joga maler; asechiko joga ma jolweny kakecho mondo gitim gima adwaro, jogo mamor kaloyo.
Ine Yehova, ndalamulira ankhondo anga; ndasonkhanitsa ankhondo anga kuti akhale zida zanga zolangira amene amadzikuza ndi chipambano changa.
4 Winjuru kaka koko wuok e gode; machalo mar oganda mangʼongo, en koko maduongʼ magore e kind pinjeruodhi, machalo mana gi ogendini mangʼeny mochokore kaachiel! Jehova Nyasaye Maratego choko oganda mangʼongo mar lweny.
Tamvani phokoso ku mapiri, likumveka ngati phokoso la gulu lalikulu la anthu! Tamvani phokoso pakati pa maufumu, ngati kuti mitundu ya anthu ikusonkhana pamodzi! Yehova Wamphamvuzonse akukhazika asilikali ake mokonzekera kuchita nkhondo.
5 Gibiro ka gia e pinje man mabor, manie tungʼ piny mogik, Jehova Nyasaye kod gige mager mag lweny, biro mondo otiekgo pinyno duto.
Iwo akuchokera ku mayiko akutali, kuchokera kumalekezero a dziko Yehova ali ndi zida zake za nkhondo kuti adzawononge dziko la Babuloni.
6 Denguru nimar odiechieng Jehova Nyasaye chiegni; odiechiengno biro ka gir kethruok maduongʼ mawuok e lwet Jehova Nyasaye Maratego.
Lirani mofuwula, pakuti tsiku la Yehova layandikira; lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
7 Nikech wachni, lwet ngʼato ka ngʼato ne jony, kendo kihondko nogo chuny ji duto ma aa.
Zimenezi zinafowoketsa manja onse, mtima wa munthu aliyense udzachokamo.
8 Kibaji nogogi malich, rem gi kuyo bende noneg-gi; ginibed gi rem mana ka dhako mamuoch kayo. Ngʼato ka ngʼato nongʼi wadgi malich ka midhiero omako.
Anthu adzagwidwa ndi mantha aakulu, zowawa ndi masautso zidzawagwera; adzamva zowawa zonga amamva mayi pobereka. Adzayangʼanana mwamantha, nkhope zawo zikufiira ngati malawi amoto.
9 Neuru, odiechieng Jehova Nyasaye biro, en odiechiengʼ malich man-gi mirima kod kum mager, mabiro weyo piny gunda, kendo joricho manie iye.
Taonani, tsiku la Yehova likubwera, tsiku lopanda chisoni, lawukali ndi lamkwiyo; kudzasandutsa dziko kuti likhale chipululu ndi kuwononga anthu ochimwa a mʼmenemo.
10 Sulwe mag polo kod lergi ok nonenre. Wangʼ chiengʼ nolokre mudho, kawuok kendo dwe bende ok norieny.
Nyenyezi zakumwamba ndiponso zonse zamlengalenga sizidzaonetsa kuwala kwawo. Dzuwa lidzada potuluka, ndipo mwezi sudzawala konse.
11 Abiro kumo piny kuom timbene mamono, joricho kuom richogi. Abiro tieko wich teko ka mar josunga kendo abiro thiro sunga mar joma wangʼ-gi tek.
Ndidzalanga dziko lonse chifukwa cha zolakwa zake, anthu oyipa ndidzawalanga chifukwa cha machimo awo. Ndidzathetsa kunyada kwa odzikuza, ndipo ndidzatsitsa kudzitukumula kwa anthu ankhanza.
12 Abiro miyo ji doko manok moloyo dhahabu mopwodhi, manok mana ka dhahabu ma aa Ofir.
Ndidzasandutsa anthu kukhala ovuta kupeza kuposa mmene amasowera golide wabwino. Iwo sazidzapezekapezeka kuposa mmene amasowera golide wa ku Ofiri.
13 Kuom mano Jehova Nyasaye Maratego nomi polo tetni, kendo piny noyiengni milengʼre; e chiengʼ onogo mar mirimbe mager.
Tsono ndidzagwedeza miyamba ndipo dziko lapansi lidzachoka pa maziko ake. Izi zidzachitika chifukwa cha ukali wa Wamphamvuzonse pa tsiku la mkwiyo wake woopsa.
14 Mana kaka mwanda ma jodwar lawo, kod rombe maonge jakwath, e kaka ngʼato ka ngʼato kuomgi biro dok ir joodgi owuon kendo ngʼato ka ngʼato nodog e pinygi.
Ngati mbawala zosakidwa, ngati nkhosa zopanda wozikusa, munthu aliyense adzabwerera kwa anthu akwawo, aliyense adzathawira ku dziko lake.
15 Ngʼato angʼata manomaki nochwo matho, jogo duto momaki noneg gi ligangla.
Aliyense amene atadzapezeke ndi kugwidwa adzaphedwa momubaya ndi lupanga.
16 Nyithindgi madhoth nochwad piny e wangʼ-gi ka gineno, utegi noyaki, kendo mondegi nomak githuon.
Ana awo akhanda adzaphwanyidwa iwo akuona; nyumba zawo zidzafunkhidwa ndipo akazi awo adzagwiriridwa.
17 Neuru, anakel jo-Media, ma ok dew fedha kendo ok gomb dhahabu mondo omonjgi.
Taona, Ine ndidzadzutsa Amedi amene safuna siliva ndipo sasangalatsidwa ndi golide, kuti amenyane ndi Ababuloni.
18 Gibiro chielo yawuowi matindo gi asere; ok giningʼwon-ne nyithindo madhoth, bende ok ginikech nyithindo matindo.
Adzapha anyamata ndi mauta awo; sadzachitira chifundo ana ngakhale kumvera chisoni ana akhanda.
19 Babulon ma en piny maber moloyo pinjeruodhi duto, kendo ma jo-Babulon sungerego, Nyasaye nokethi mana kaka noketho Sodom gi Gomora.
Babuloni, ufumu wake ndi waulemerero kuposa mafumu onse. Anthu ake amawunyadira. Koma Yehova adzawuwononga ngati mmene anawonongera Sodomu ndi Gomora.
20 Onge ngʼat manochak obedi e iye kata dak kuno e tienge duto mabiro; onge ja-Arabu moro manodag kuno; bende onge jakwath mano kwa jambe kanyo.
Anthu sadzakhalamonso kapena kukhazikikamo pa mibado yonse; palibe Mwarabu amene adzayimike tenti yake, palibe mʼbusa amene adzawetamo ziweto zake.
21 To mana le mag thim ema nodag kanyo, kibwe nopongʼ utegi; tula bende nodag kanyo kendo nywok nolengʼre kanyo.
Koma nyama zakuthengo ndizo zidzakhale kumeneko, nyumba zake zidzadzaza ndi nkhandwe; mu mzindamo muzidzakhala akadzidzi, ndipo atonde akuthengo azidzalumphalumphamo.
22 Ondiegi noywagre kuondegi mane gigeno, kibwe to noywe e ute mabeyo mag ruoth. Ndalo mag Babulon osekayo machiegni ma ok notony.
Mu nsanja zake muzidzalira afisi, mʼnyumba zake zokongola muzidzalira nkhandwe. Nthawi yake yayandikira ndipo masiku ake ali pafupi kutha.

< Isaya 13 >