< Hosea 2 >

1 “Luonguru oweteu ni ‘Joga,’ kendo luonguru nyimineu ni ‘Joma ahero.’”
“Nena kwa abale ako kuti, ‘Ndinu anthu anga,’ kwa alongo ako kuti ‘Ndinu okondedwa anga.’”
2 “Kwer minu, kwere, nikech ok en jaoda, kendo ok an chwore. Onego owe wangʼ maneno mar chode kendo gi yorene mag dwanyruok.
“Dzudzulani amayi anu, adzudzuleni iwo, pakuti si mkazi wanga, ndipo ine sindine mwamuna wake. Iyeyo achotse maonekedwe adama pa nkhope yake, ndi kusakhulupirika pa mawere ake.
3 Ka ok kamano to abiro lonye duk modongʼ kaka ne onywole; anakete ochal kaka lop ongoro, analoke kaka lowo motwo mobaro okak, kendo ananege kod riyo mar pi.
Akapanda kutero ndidzamuvula, ndipo adzakhala wamaliseche monga tsiku limene anabadwa; ndidzamuwumitsa ngati chipululu, adzakhala ngati dziko lopanda madzi, ndi kumupha ndi ludzu.
4 Ok anaher nyithinde, nikech gin nyithindo mane oyud e yor chode.
Sindidzaonetsa chikondi changa pa ana ake, chifukwa ndi ana a mʼchiwerewere.
5 Min-gi ok osebedo ja-ratiro kendo osemako ich gi anjawo. Owacho ni, ‘Abiro luwo bangʼ joherana, mamiya chiemba kod piga, yie rombe gi pamba michweyogo lewni, mo kod math.’
Amayi awo akhala akuchita zachiwerewere ndipo anawabereka anawo akuchita zinthu zochititsa manyazi. Iwo anati, ‘Ine ndidzatsatira zibwenzi zanga, zimene zimandipatsa chakudya ndi madzi, ubweya ndi thonje, mafuta ndi chakumwa.’
6 Omiyo anagengʼ yore kod bungu maduongʼ mar kudho; abiro dinone chuth ma ok noyud yo mowuok godo oko.
Choncho njira yake ndidzayitseka ndi minga; ndidzamuzinga ndi khoma kotero kuti sadzapezanso njira yotulukira.
7 Enolaw bangʼ jochodenego to ok nomakgi; enomanygi to ok noyudgi. Bangʼe to enowachi niya, Abiro dokne chwora mokwongo, nimar ndalono ne awinjo maber moloyo sani.
Adzathamangira zibwenzi zake koma sadzazipeza; adzazifunafuna koma sadzazipeza. Pamenepo iye adzati, ‘Ndibwerera kwa mwamuna wanga woyamba uja, pakuti ndinali pabwino ndi iyeyo kusiyanitsa ndi pano.’
8 Ok osengʼeyo adier ni an ema ne amiye cham, divai manyien kod mo, an bende ema ne adhiale gi fedha gi dhahabu mangʼenygo mane gitiyo nego Baal.
Iye sanazindikire kuti ndine amene ndinkamupatsa tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta. Ndine amene ndinkamukhuthulira siliva ndi golide, zimene ankapangira mafano a Baala.
9 “Kuom mano abiro kawo chamba ka osechiek, gi divaina manyien ka oseikore. Bende anakaw yie rombona gi pambana mitwangʼo godo lewni mane onego oum-go duge.
“Choncho Ine ndidzamulanda tirigu wanga pa nthawi yokolola, ndi vinyo wanga watsopano pa nthawi yopsinya mphesa. Ndidzamulanda ubweya ndi thonje langa, zomwe akanaphimba nazo umaliseche wake.
10 Koro abiro nyiso ayanga gombo mare mar chode e lela e nyim joherane; kendo onge ngʼama nogole e lweta.
Motero tsopano ndidzaonetsa maliseche ake pamaso pa zibwenzi zake; palibe ndi mmodzi yemwe adzamupulumutse mʼmanja mwanga.
11 Nyasi duto ma en-go anakethi: nyasi mar higa ka higa, mar dwe ka dwe, mar Sabato kod nyasi motimo juma ka juma.
Ndidzathetsa zikondwerero zake zonse: zikondwerero zake za chaka ndi chaka, za mwezi watsopano, za pa masiku a Sabata ndi maphwando ake onse a pa masiku okhazikitsidwa.
12 Anaketh yiendene mag mzabibu gi yiend ngʼopene mane owacho ni ne chudone moa kuom joherane. Abiro ketogi bunge, kendo le mag bungu nokethgi.”
Ndidzawononga mitengo yake ya mpesa ndi mitengo yake yamkuyu, imene iye ankanena kuti inali malipiro ake ochokera kwa zibwenzi zake. Ndidzayisandutsa chithukuluzi, ndipo zirombo zakuthengo zidzadya zipatsozo.
13 Jehova Nyasaye wacho niya, “Anakume kuom ndalo duto mane owangʼo ubani ne Baal; korwakore gi gik mabeyo ahinya kolombogo joherane, to an ne wiye owil koda.
Ndidzamulanga chifukwa cha masiku amene anafukiza lubani kwa Abaala; anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali ndipo anathamangira zibwenzi zake, koma Ine anandiyiwala,” akutero Yehova.
14 “Kuom mano abiro hoye, mi adhi kode e piny motimo ongoro, kendo abiro wuoyo kode gi muolo.
“Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo; ndidzapita naye ku chipululu ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.
15 Kanyo abiro dwokone puothe mar mzabibu, Kendo analos holo mar Akor obed dhood geno. Kanyo nowerie mana kaka nower kapod otin, mana ka chiengʼ mane owuok koa Misri.”
Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa, ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo. Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake, monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.
16 Jehova Nyasaye owacho niya, “Odiechiengʼno iniluonga ni ‘chwora,’ to ok inichak iluonga ni ‘jatenda.’
“Tsiku limeneli,” Yehova akuti, “udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’ sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’
17 Abiro golo nyinge mag Baal oa e dhoge. Nying Baal ok nochak owuo kuomgi kendo.
Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake; sadzatchulanso mayina awo popemphera.
18 Chiengʼno anaketnegi singruok e kindgi gi le mag thim gi winy manie kor polo, gi chwech mamol e lowo, atungʼ gi ligangla to abiro turo, kendo lweny bende anatiek e piny, mondo gik moko duto obed gi kwe.
Tsiku limenelo ndidzachita pangano ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga. Ndidzachotsa mʼdzikomo uta, lupanga ndi zida zonse zankhondo, kuti onse apumule mwamtendere.
19 Abiro timo kodi singruok mar kend mondo ibed mara chuth; abiro timo kodi singruok mar kend e yo maler kendo maratiro, gihera kod kech.
Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya; ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro, mwachikondi ndi mwachifundo.
20 Abiro timo kodi singruok mar kend e yo mar adiera, kendo ibiro yie kuom Jehova Nyasaye.”
Ndidzakutomera mokhulupirika ndipo udzadziwa Yehova.
21 Jehova Nyasaye wacho niya, “E odiechiengno abiro dwoko kwayou ma boche polo, nochiw koth ne piny,
“Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,” akutero Yehova. “Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;
22 kendo cham biro nyak e piny, kaachiel gi divai manyien kod mo zeituni, mi giduto ginyag Jezreel.
ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu, vinyo ndi mafuta, ndipo zidzamvera Yezireeli.
23 Abiro pidhe e piny ne an awuon; abiro nyiso herana ni ngʼat mane aluongo ni ‘Ok jaherana.’ Anawach ni joma iluongo ni, ‘Joma ok joga,’ ni, ‘Un joga’; kendo ginidwoka ni, ‘In Nyasachwa.’”
Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga: ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’ Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’ ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’”

< Hosea 2 >