< Habakuk 2 >

1 Abiro chungʼ kara mar rito kendo abiro bedo ewi kuonde moger motingʼore mag rito. Abiro ngʼicho mondo ane gima obiro wachona, kendo kuom dwoko mabiro chiwo kuom ywagni.
Ndidzakhala pa malo anga aulonda, ndi kuyima pa mitumbira ya nkhondo; ndidzadikira kuti ndimve zimene Iye adzandiwuze, ndi yankho limene ndidzapatsidwe pa madandawulo anga.
2 Eka Jehova Nyasaye nodwoke niya, “Ndik fwenyni kendo iler tiende maber kama indike, mondo jaland wach oring katere.
Tsono Yehova anandiyankha, nati: “Lemba masomphenyawa ndipo uwalembe mooneka bwino pa mapale kuti wowerenga awawerenge mosavuta.
3 Nikech fwenyni rito kinde moketi; owuoyo kuom ndalo giko, kendo ok nobed miriambo. Kata obedo ni onyalo deko kapok ochopo, rite arita, adier obiro chopo ma ok odeko.
Pakuti masomphenyawa akudikira nthawi yake; masomphenyawa akunena zamʼtsogolo ndipo sizidzalephera kuchitika. Ngakhale achedwe kukwaniritsidwa, uwayembekezere; zidzachitika ndithu ndipo sadzachedwa.
4 “Ne kaka osungore; dwarone ok nikare. To ngʼat makare nobed mangima kuom yie mare,
“Taona, mdani wadzitukumula; zokhumba zake sizowongoka, koma wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.
5 chutho, divai momadho ndhoge; en jasunga kendo osiko otimo gik maricho ma ok ool. Nikech owuor ka liel mamuonyo ji kendo kaka tho ok rom e kaka en bende ok orom, ochoko ogendini duto mondo obi ire, kendo omako ji duto wasumbini. (Sheol h7585)
Ndithu, wasokonezeka ndi vinyo; ndi wodzitama ndiponso wosakhazikika. Pakuti ngodzikonda ngati manda, ngosakhutitsidwa ngati imfa, wadzisonkhanitsira mitundu yonse ya anthu ndipo wagwira ukapolo anthu a mitundu yonse. (Sheol h7585)
6 “To donge jogi biro kwede ka ngʼongʼone kendo jare kawacho niya, “‘Inine malit in ngʼama choko gik mokwal kendo mabedo ja-mwandu gi gige mecho. Nyaka karangʼo ma gigi nodhi nyime katimore?’
“Kodi onse ogwidwawo sadzamunyoza ndi kumunyogodola ponena kuti, “Tsoka kwa amene amadzikundikira katundu amene si wake ndipo amadzilemeretsa ndi chuma cholanda! Kodi izi zidzachitika mpaka liti?
7 To donge jogopeu biro poyou? Donge gibiro chiewo ma gimi utetni? Eka unubed wasumbinigi.
Kodi angongole ako sadzakuwukira mwadzidzidzi? Kodi sadzadzuka ndi kukuchititsa mantha? Pamenepo iwe udzalandidwa kalikonse.
8 Nikech useyako ogendini mangʼeny, joma odongʼ biro mayou. Nimar usechwero remb dhano, useketho pinje, mier madongo kod ji duto manie igi.
Pakuti unafunkha mitundu yambiri ya anthu, mitundu ina imene inatsala idzakufunkha iweyo. Pakuti wakhetsa magazi a anthu; wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.
9 “Ngʼat mayudo mwandu gi yore ma ok owinjore none malit kendo ogero ode kama otingʼore gi malo, mondo otony ne kethruok!
“Tsoka kwa amene amalemera ndi chuma chochipeza mwachinyengo, kukweza malo ake okhalapo, kuthawa mavuto!
10 Isechano kethruok mar ogendini mangʼeny, ma osemiyo odi owuon wichkuot kendo iwito ngimani.
Wakonzekera kuwononga mitundu yambiri ya anthu, kuchititsa manyazi nyumba yako yomwe ndi kuwononga moyo wako.
11 Kite mag kor ot noywagnu matek to yiend tado nokow ywagno.
Mwala pa khoma udzafuwula, ndipo mitanda ya matabwa idzavomereza zimenezi.
12 “Ngʼat magero dalane gi remo kendo guro dala maduongʼ gi gige mecho enone malit!
“Tsoka kwa amene amanga mzinda pokhetsa magazi ndi kukhazikitsa mzinda pochita zoyipa!
13 Donge Jehova Nyasaye Maratego osechiko ni tije ogendini maricho biro bedo ramok mach, ogendini tiyo ma ol kayiem nono?
Kodi Yehova Wamphamvuzonse sanatsimikize kuti ntchito za anthu zili ngati nkhuni pa moto, ndi kuti mitundu ya anthu imadzitopetsa popanda phindu?
14 Nimar piny biro pongʼ gi ngʼeyo mar duongʼ Jehova Nyasaye kaka pi kwako nam.
Pakuti dziko lapansi lidzadzaza ndi chidziwitso cha ulemerero wa Yehova, monga momwe madzi amadzazira nyanja.
15 “Enone malit ngʼat mamiyo jobathe math, ka omedogi ameda nyaka gimer, mondo one dug-gi.
“Tsoka kwa amene amamwetsa anzake zakumwa zoledzeretsa, kutsanula mʼbotolo mpaka ataledzera, kuti aone umaliseche wawo.
16 Wichkuot nomaki kar bedo gi pak. Koro en kindeni mar mer! Methi kendo dongʼ duk! Okombe moa e lwet Jehova Nyasaye ma korachwich bironi, kendo wichkuot biro umo duongʼ ma in-go.
Udzachita manyazi mʼmalo mokhala ndi ulemerero. Tsopano ino ndi nthawi yako! Imwa mpaka umaliseche wako uwonekere! Chikho chochokera mʼdzanja lamanja la Yehova chikubwera kwa iwe, ndipo manyazi adzaphimba ulemerero wako.
17 Timbe mahundu ma isetimone Lebanon nonyori kendo le mane inego marach biro miyi bwok. Nimar isechwero remb dhano, iseketho pinje gi mier madongo, kendo gi ji duto manie igi.
Udzathedwa nzeru ndi chiwawa chimene unachita ku Lebanoni, ndiponso udzachita mantha ndi nyama zimene unaziwononga. Pakuti wakhetsa magazi a anthu; wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.
18 “En ohala manade miyudo kuom nyiseche manono nimar dhano ema opayogi? Kata kido mapuonjo miriambo? Ngʼat malose oketo genone, kuom gima oloso owuon; oloso nyiseche manono ma ok nyal wuoyo.
“Kodi fano lili ndi phindu lanji, poti analisema ndi munthu, kapena chifanizo chimene chimaphunzitsa mabodza? Pakuti munthu amene walipanga amakhulupirira ntchito ya manja ake; amapanga mafano amene samatha kuyankhula.
19 Enone malit ngʼat mawachone yien ni, ‘Bed mangima!’ Kata ni kite maonge ngima ni, ‘Chiew!’ Bende gik ma kamago dingʼadnu rieko? Kata obedo ni obawgi gi dhahabu gi fedha; to gionge gi ngima nikech gin gik motho.”
Tsoka kwa amene amawuza mtengo kuti, ‘Khala wamoyo!’ Kapena mwala wopanda moyo kuti, ‘Dzuka!’ Kodi zimenezi zingathe kulangiza? Ndi zokutidwa ndi golide ndi siliva; mʼkati mwake mulibe mpweya.
20 To Jehova Nyasaye nitie e hekalune maler; piny duto mondo olingʼ e nyime.
Koma Yehova ali mʼNyumba yake yopatulika; dziko lonse lapansi likhale chete pamaso pake.”

< Habakuk 2 >