< Chakruok 49 >

1 Eka Jakobo noluongo yawuote mowachonegi niya, “Biuru machiegni mondo anyisu gima biro timorenu e ndalo mabiro.
Pambuyo pake Yakobo anayitanitsa ana ake aamuna nati: Sonkhanani pamodzi kuti ndikuwuzeni zimene zidzakuchitikireni mʼmasiku a mʼtsogolo.
2 “Un yawuot Jakobo chokreuru buta kendo uchik itu; winjuru Israel wuonu.
“Bwerani ndipo imvani mawu anga, inu ana a Yakobo; mverani abambo anu Israeli.
3 “Reuben, in e wuoda makayo, kendo in e tekona kendo in e ranyisi mokwongo mar tekra, bende in giluor mangʼeny kod teko mangʼeny.
“Rubeni, ndiwe woyamba kubadwa; mphamvu yanga ndiponso chizindikiro choyamba cha mphamvu zanga, wopambana pa ulemerero ndi mphamvu.
4 Ijamuomri ka pi aora, to ok inibed gi duongʼ, nikech isedonjori, gi kitanda wuonu ma ichido.
Wokokoma ngati madzi a chigumula, koma sudzakhalanso wopambana, iwe unagona pa bedi la abambo ako, ndithu unayipitsa bedi la mdzakazi wake.
5 “Simeon gi Lawi gin owete, gisetimo timbe mag lweny gi liganglagi.
“Simeoni ndi Levi ndi pachibale pawo, anachitira nkhanza anthu amene anachita nawo pangano.
6 Ok nariwra kodgi e buchegi, ok nariwra kodgi e chokruogegi, nikech ka mirima omakogi to ginego ji kendo gingʼado odond dhok sa asaya ka gihero.
Iwe moyo wanga, usakhale nawo pa misonkhano yawo ya mseri, kapena kugwirizana nawo mʼmabwalo awo, pakuti anapha anthu mu mkwiyo wawo ndipo anapundula ngʼombe zamphongo monga kunawakomera.
7 Okwongʼ mirimbgi nikech en mirima mager kendo makwiny. Anakegi e kind joka Jakobo kendo akegi e piny Israel duto.
Matemberero awagwere chifukwa cha mkwiyo wawo woopsa chonchi ndi ukali wawo wankhanza choterewu! Ine ndidzawabalalitsa mʼdziko la Yakobo ndi kuwamwaza iwo mʼdziko la Israeli.
8 “Juda, oweteni biro paki; bende inimak wasiki gi ngʼutgi, kendo oweteni biro kuloreni.
“Yuda, ndiwe amene abale ako adzatamanda; dzanja lako lidzagwira pa khosi pa adani ako; abale ako adzakugwadira iwe.
9 Yaye Juda nyathina, ichalo nyathi sibuor, modwogo koa dwar. Obuto ka sibuor madhako monindo piny, maonge ngʼama nyalo chiewo.
Yuda ali ngati mwana wa mkango; umabwerera ku malo ako ndi zofunkha, mwana wanga. Monga mkango, amadziwongola ndi kugona pansi, ndipo ngati mkango waukazi, ndani angalimbe mtima kumudzutsa?
10 Ludh duongʼ ok noa e lwet Juda kata odunga mar teko ok noa e tiende, nyaka wuon loch ma biro rito ogendini duto chopi kendo luor mar ogendini nobed kuome.
Ndodo yaufumu sidzachoka mwa Yuda, udzawupanirira ulamuliro motero kuti palibe amene adzawuchotse, mpaka mwini wake weniweni atabwera ndipo mitundu yonse ya anthu idzamumvera.
11 Obiro tweyo pundane e kor mzabibu, enotue nyathi pundane e mzabibu moyier; kendo obiro luoko lepe gi divai makwar.
Ndiye amene amamangirira bulu wake wamkazi kumtengo wa mpesa, ndi mwana wa bulu ku nthambi ya mpesa wabwino. Ndi iye amene amachapa zovala zake mu vinyo; ndi mkanjo wake mu vinyo wofiira ngati magazi.
12 Wangʼe nobed makwar moloyo divai kendo lake nobed matar ka chak.
Maso ake adzakhala akuda chifukwa cha vinyo, mano ake woyera chifukwa cha mkaka.
13 “Zebulun nodag e dho nam kama yiedhi gowe, kendo tongʼ mare nodhi nyaka Sidon.
“Zebuloni adzakhala mʼmphepete mwa nyanja; adzakhala pa dooko la sitima zapamadzi; malire ake adzafika ku Sidoni.
14 “Isakar en punda maratego ma nindo piny e dier misikene.
“Isakara ali ngati bulu wamphamvu wogona pansi pakati pa makola.
15 Kane oneno kaka dalane ber, kendo kaka pinyno ber, noyie tingʼo misigo modoko misumba matiyo tich matek.
Ataona ubwino wake wa pamalo pake popumira ndi kukongola kwa dziko lake, iye anaweramutsa msana kuti anyamule katundu wake ndipo anasanduka wogwira ntchito ya ukapolo.
16 “Dan nobed jangʼad bura ne joge mana kaka achiel kuom oganda Israel.
“Dani adzaweruza mwachilungamo anthu ake monga limodzi mwa mafuko a anthu a mu Israeli.
17 Dan nobed ka thuol man e dir yo, thuol man-gi kwiri mager e yo, ma kayo ombongʼ Faras mondo ngʼama oidhe ochwanyre magore piny gi kangʼeye.
Dani adzakhala ngati njoka ya mʼmphepete mwa msewu, songo yokhala mʼnjira imene imaluma chidendene cha kavalo kuti wokwerapoyo agwe chagada.
18 “Aserito warruok yaye Jehova Nyasaye.
“Ndikuyembekeza chipulumutso chanu Yehova.
19 “Gad to nomonj gi jomecho, to noriembgi kolawogi matek.
“Gadi adzachitidwa chiwembu ndi gulu la amaliwongo, koma iye adzawathamangitsa.
20 “Asher nobed gi chiemo mamit; nobed gi chiemo moromo ruoth chamo.
“Dziko la Aseri lidzabereka chakudya chokoma, ndipo iye adzapereka chakudya kwa mafumu.
21 “Naftali to en mwanda mogony, ma nywolo nyithindo mabeyo.
“Nafutali ali ngati mbawala yayikazi yokhala ndi ana okongola kwambiri.
22 “Josef en mzabibu manyago olemo mopidh e bath thidhna, ma bedene ogawore e kor ot.
“Yosefe ali ngati mtengo wobereka zipatso, mtengo wobereka zipatso pafupi ndi kasupe, nthambi zake zimayanga pa chipupa cha mwala.
23 Jodir asere nolawe matek kokecho, ne gibaye gi asere ka igi owangʼ.
Alenje a uta anamuchita chiwembu mwankhanza; anamuthamangitsa ndi mauta awo.
24 Kata kamano, Nyasaye Maratego ma Nyasach Jakobo noturo atungegi, kendo Jakwath, ma Lwanda mar Israel, nochodo leche mag ogich bedegi.
Koma uta wake sunagwedezeke, ndi manja ake amphamvu aja analimbika, chifukwa cha mphamvu za Mulungu Wamphamvu wa Yakobo, chifukwa ali Mʼbusa ndi Thanthwe la Israeli.
25 Nyasach wuonuno ma en Nyasaye Maratego, mondo ogwedhi gi gweth mag polo gi gweth mag nyak mag lowo, gi gweth mag nyithindo.
Chifukwa cha Mulungu wa makolo ako amene amakuthandiza; chifukwa cha Mulungu Wamphamvu, amene amakudalitsa ndi mvula yochokera kumwamba, ndi madzi otumphuka pansi pa nthaka, ndipo amakudalitsa pokupatsa ana ambiri ndi ngʼombe zambiri.
26 Gweth mag wuoro dongo moloyo gweth mag gode madongo machon, kendo moloyo gik mabeyo duto mag gode mosiko. Gwethgi mondo obi ne Josef, ngʼat mane opog gi jowetene.
Madalitso a kholo lako ndi amphamvu kuposa madalitso a mapiri akale oposa zabwino za ku zitunda zamgonagona. Zonse izi zikhale pamutu pa Yosefe, pa mphumi pa wopatulika uja amene anapatulidwa pakati pa abale ake.
27 “Benjamin en ondiek ma kech kayo; gima osenego ochamo gokinyi, kendo godhiambo okidho matindo tindo gima osemako.”
“Benjamini ali ngati mʼmbulu wolusa; umene mmawa umapha ndi kudya zofunkha, ndipo madzulo umagawa zofunkhazo,”
28 Magi e dhout Israel apar gariyo duto kendo mae gima ne wuon-gi owachonegi kane ogwedhogi, ka omiyo moro ka moro gweth moromore kode.
Onse awa ndi mafuko khumi ndi awiri a Israeli, ndipo zimenezi ndi zomwe abambo awo ananena pamene anawadalitsa, kuwapatsa aliyense madalitso ake womuyenera iye.
29 Eka Jakobo nochiko yawuote kowachonegi niya, “An koro achiegni tho mondo adhi ariwra gi jowetena, yikauru but kwerena e rogo man e puoth Efron ja-Hiti.
Kenaka Yakobo analamula ana ake nati: “Ine ndatsala pangʼono kufa. Tsono mukandiyike pamodzi ndi makolo anga mʼphanga la mʼmunda wa Efroni Mhiti.
30 Rogo man e puodho man Makpela, machiegni gi Mamre e piny Kanaan, ema ne Ibrahim ongʼiewo kaka kar yiko kaachiel gi puodhono duto koa kuom Efron ja-Hiti.
Ili ndi phanga la mʼmunda wa Makipela, pafupi ndi Mamre mʼdziko la Kanaani. Abrahamu anagula phangalo pamodzi ndi munda womwe kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda.
31 Kanyo ema ne oike Ibrahim kod Sara chiege, kanyo bende ema ne oikie Isaka kod Rebeka chiege, kendo kanyo ema ne aikoe Lea.
Kumeneko kunayikidwa Abrahamu ndi mkazi wake Sara, Isake ndi mkazi wake Rebeka ndipo ndinayikakonso Leya.
32 Puodhono kod rogo duto mane ni e iye nongʼiew koa kuom jo-Hiti.”
Munda ndi manda amene ali mʼmenemo zinagulidwa kwa Ahiti.”
33 Kane Jakobo osetieko wacho wechegi ni yawuote kamano nodwoko tiende e kitanda, mi chunye nochot kendo noluwo kwerene.
Yakobo atamaliza kupereka malangizo kwa ana ake, anabwezera miyendo yake pa bedi, namwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.

< Chakruok 49 >