< Chakruok 4 >

1 Adam nobedo e achiel gi chiege Hawa kendo nomako ich mi nonywolo Kain mowacho niya, “Kuom ngʼwono mar Jehova Nyasaye asenywolo wuowi.”
Adamu anagona malo amodzi ndi Hava mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Kaini, ndipo anati, “Ndi thandizo la Yehova ndapeza mwana wamwamuna.”
2 Bangʼe nonywolo owadgi miluongi ni Abel. Abel ne en jakwadh jamni to Kain ne en japur.
Kenaka anabereka mʼbale wake Abele. Abele anali woweta nkhosa ndipo Kaini anali mlimi.
3 Bangʼ ndalo moko Kain nokelo nyak mag lowo kaka misango ne Jehova Nyasaye.
Patapita nthawi, Kaini anatenga zipatso za ku munda nakazipereka kwa Yehova monga nsembe.
4 To Abel nokelo ringʼo machwe koa kuom achiel mag jambe makayo. Jehova Nyasaye noyie gi Abel kod misango mare,
Nayenso Abele anatenga ana ankhosa oyamba kubadwa pamodzi ndi mafuta ake nakazipereka ngati nsembe kwa Yehova. Yehova anakondwera ndi Abele ndi nsembe yake.
5 to Kain kod misango mare to ne ok oyiego. Kuom mano Kain mirima nomako kendo wangʼe nojuol.
Koma sanakondwere ndi Kaini ndi nsembe yake. Kotero Kaini anakwiya kwambiri ndipo nkhope yake inagwa.
6 Eka Jehova Nyasaye nopenjo Kain niya, “Angʼo ma omiyo in-gi mirima? Angʼo ma omiyo wangʼi ojuol?
Choncho Yehova anati kwa Kaini, “Chifukwa chiyani wakwiya ndipo bwanji nkhope yako yagwa?
7 Kitimo maber donge diyieni? To ka itimo marach to richo okichore e dhoodi, kendo ogomboni mondo okawi, to in nyaka iloye.”
Ukanachita zabwino sindikanakulandira kodi? Koma tsopano wachita zoyipa ndipo tchimo likukudikira pa khomo pako, likufuna kukugwira; koma iwe uyenera kugonjetsa tchimolo.”
8 Eka Kain nowacho ne owadgi Abel niya, “Wadhi waba e pap oko.” To kane gin e pap, Kain nogoyo owadgi ma Abel mi onege.
Tsiku lina Kaini anati kwa mʼbale wake Abele, “Tiye tipite ku munda.” Ndipo ali ku mundako, Kaini anawukira mʼbale wake namupha.
9 Eka Jehova Nyasaye nopenjo Kain niya, “Ere owadu Abel?” Nodwoke niya, “Ok angʼeyo. An jakwadhe?”
Ndipo Yehova anamufunsa Kaini kuti, “Ali kuti mʼbale wako Abele?” Iye anayankha kuti, “Sindikudziwa. Kodi ine ndine wosunga mʼbale wanga?”
10 Jehova Nyasaye nowachone niya, “Isetimo angʼoni? Winji! Remb owadu ywakna koa e lowo.
Yehova anati, “Kodi wachita chiyani? Tamvera! Magazi a mʼbale wako akulirira kwa Ine kuchokera mʼnthaka.
11 Omiyo koro in e bwo kwongʼ kendo oseriembi e piny mosengʼamo dhoge mondo omwony remb owadu koa e lweti.
Ndipo tsopano ndiwe wotembereredwa ndipo wachotsedwa mʼdziko limene nthaka yake inatsekula pakamwa pake kulandira magazi a mʼbale wako amene unakhetsa.
12 Ka ipuro lowo, to ok obi nyagoni cham. Ibiro bedo ngʼat maonge kar dak mabayo abaya e piny.”
Udzalima munda koma nthakayo sidzakupatsanso zokolola zake. Udzakhala wosakhazikika; womangoyendayenda pa dziko lapansi.”
13 Kain nowacho ne Jehova Nyasaye niya, “Kum mi miyano ohinga.
Kaini anati kwa Yehova, “Chilango changa ndi chachikulu kuposera mphamvu zanga.
14 Kawuono iseriemba e lowo kendo ibiro pandona wangʼi; abiro bet ngʼat maonge kar dak mabayo abaya e piny kendo ngʼato angʼata moyuda nonega.”
Lero mukundipirikitsa pa dziko ndi pamaso panu; ndidzakhala wosakhazikika, woyendayenda, ndipo aliyense amene adzandipeze adzandipha.”
15 To Jehova Nyasaye nowachone niya, “Ok kamano, ka ngʼato onegi, nochul ne kuor nyadibiriyo moloyo.” Eka Jehova Nyasaye noketo ranyisi kuom Kain mondo ngʼato moromo kode kik nege.
Koma Yehova anamuwuza kuti, “Sizidzatero ayi; aliyense amene adzaphe Kaini adzalangidwa ndi kulipiritsidwa kasanu ndi kawiri.” Pamenepo Yehova anayika chizindikiro pa Kaini kuti aliyense womupeza asamuphe.
16 Omiyo Kain noa e nyim Jehova Nyasaye kendo nodak e piny Nod, mantie yo wuok chiengʼ mar Eden.
Ndipo Kaini anachoka pamaso pa Yehova nakakhala ku dziko la Nodi, kummawa kwa Edeni.
17 Kain nobedoe achiel gi chiege mi chiege nomako ich kendo nonywolo Enok. Noyudo Kain gero dala maduongʼ kendo nochako dalano nying wuode ma Enok.
Kaini anagona malo amodzi ndi mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Enoki. Kaini nthawi imeneyo nʼkuti akumanga mzinda ndipo anawutcha dzina la mwana wake Enoki.
18 Enok nonywolo Irad: Kendo Irad ema ne wuon Mehujael, kendo Mehujael nonywolo Methushael kendo Methushael nonywolo Lamek.
Enoki anabereka Iradi; Iradi anabereka Mehuyaeli, ndipo Mehuyaeli anabereka Metusela, ndipo Metusela anabereka Lameki.
19 Lamek nokendo mon ariyo, achiel ne nyinge Ada to machielo Zila.
Lameki anakwatira akazi awiri, wina dzina lake linali Ada ndi winayo dzina lake linali Zila.
20 Ada nonywolo Jabal, mane wuon jokwath mane odak e hembe kendo ne nigi jamni.
Ada anabereka Yabala; iyeyu anali kholo la onse okhala mʼmatenti ndi oweta ziweto.
21 Owadgi ne nyinge Jubal, ma en ema nokwongo chako goyo thumbe mag nyatiti gi asili.
Dzina la mʼbale wake linali Yubala; iyeyu anali kholo la onse oyimba zeze ndi chitoliro.
22 Zila bende nonywolo wuowi ma nyinge Jubal-Kain, mane jatheth chumbe duto mag mula kod nyinyo. Nyamin Tubal-Kain nyinge ne Naama.
Zila nayenso anali ndi mwana wamwamuna, dzina lake Tubala-Kaini. Iyeyu anali kholo la amisiri onse osula zida za mkuwa ndi chitsulo. Mlongo wake wa Tubala-Kaini anali Naama.
23 Lamek nowachone monde ariyo-ka niya, “Ada kod Zila, winjauru, un monda winjuru wechena. Asenego ngʼato, nikech nogoya, wuowi matin nikech nohinya.
Lameki anawuza akazi akewo kuti, “Ada ndi Zila, ndimvereni; inu akazi anga imvani mawu anga. Ine ndinapha munthu chifukwa anandipweteka. Ndinapha mnyamatayo chifukwa anandimenya.
24 Ka Kain ochulne kuor nyadibiriyo to kara Lamek to nochul ne kuor nyadi piero abiriyo gabiriyo.”
Ngati wopha Kaini amulipsira kasanu nʼkawiri, ndiye kuti wopha ine Lameki adzamulipsira kokwanira 77.”
25 Adam nobedoe achiel gi chiege, kendo chiege nonywolo wuowi mi nochake ni Seth, mowacho niya, “Nyasaye osemiya nyathi machielo kar Abel mane Kain onego.”
Adamu anagonanso malo amodzi ndi mkazi wake, ndipo anabereka mwana wamwamuna namutcha Seti, kutanthauza kuti, “Mulungu wandipatsa mwana wina mʼmalo mwa Abele, popeza Kaini anamupha.”
26 Seth bende nonywolo wuowi, kendo nochake ni Enosh. E ndalono ema ne ji ochako luongo nying Jehova Nyasaye.
Seti naye anali ndi mwana wa mwamuna, ndipo anamutcha Enosi. Pa nthawi imeneyi anthu anayamba kupemphera mʼdzina la Yehova.

< Chakruok 4 >