< Chakruok 3 >

1 To thuol ne riek moloyo le duto mag bungu mane Jehova Nyasaye ochweyo. Omiyo nopenjo dhako niya, “Bende en adier ni Nyasaye nowacho ni, ‘Kik ucham olemb yien moro amora manie puodho?’”
Ndipo njoka inali yochenjera kuposa nyama yakuthengo iliyonse imene Yehova Mulungu anapanga. Njokayo inati kwa mkaziyo, “Kodi Mulungu ananenadi kuti, ‘Inu musadye zipatso za mtengo uliwonse mʼmundamu?’”
2 Dhako nodwoko thuol niya, “Wanyalo chamo olembe mag yiende manie puodho duto,
Mkaziyo anati kwa njokayo, “Tikhoza kudya zipatso za mʼmitengo ya mʼmundawu,
3 makmana Nyasaye nosiemowa ni, ‘Kik ucham olemo mar yien man e dier puodhono, kendo kik umule nono to ubiro tho.’”
koma Mulungu anati, ‘Musadye zipatso za mu mtengo umene uli pakati pa munda, ndipo musadzawukhudze kuti mungadzafe.’”
4 Thuol nowacho ne dhako niya, “Adier ok unutho.
“Ndithudi simudzafa,” inatero njokayo kwa mkaziyo.
5 Nikech Nyasaye ongʼeyo ni sa ma unuchame wengeu noyepi kendo unubed machal gi Nyasaye, kungʼeyo ber gi rach.”
“Pakuti Mulungu akudziwa kuti tsiku limene mudzadye zipatso za mu mtengowo, maso anu adzatsekuka, ndipo mudzakhala ngati Mulungu, wodziwa zabwino ndi zoyipa.”
6 Kane dhako oneno ni olemb yien-no ne ber kuom chiemo kendo moro wangʼ kendo nyalo miyo ibed gi rieko, nokawo moko mochamo, to bangʼe nomiyo chwore ma en bende nochame.
Pamene mkaziyo anaona kuti mtengowo unali wabwino kudya ndi wokongola ndi kuti unali wopatsa nzeru, anatengako zipatso zake nadya. Zina anamupatsako mwamuna wake amene anali naye pomwepo ndipo naye anadyanso.
7 Eka wengegi noyepo kendo negifwenyo ni gin duge; kuom mano negikawo it ngʼowu kendo giumogo dugegi.
Kenaka maso awo anatsekuka, ndipo anazindikira kuti anali maliseche. Choncho anasoka masamba a mkuyu nadzipangira zovala.
8 Eka Adam kod chiege nowinjo dwond Jehova Nyasaye kawuotho e puodho e seche mag angʼich welo kendo ne gipondo ne Jehova Nyasaye e kind yiende manie puodho.
Kenaka munthu uja ndi mkazi wake anamva mtswatswa wa Yehova Mulungu akuyendayenda mʼmundamo madzulo a tsikulo, ndipo iwo anabisala pamaso pa Yehova Mulungu pakati pa mitengo ya mʼmundamo.
9 To Jehova Nyasaye noluongo Adam mopenje niya, “In kanye?”
Yehova Mulungu anayitana munthu uja kuti, “Uli kuti?”
10 Nodwoko niya, “Ne awinji e puodho kendo luoro nomaka nikech ne an duk, koro ne apondo.”
Iye anayankha, “Ndinakumvani mʼmundamo, ndipo ndimaopa chifukwa ndinali maliseche; choncho ndinabisala.”
11 Kendo Jehova Nyasaye nowachone niya, “En ngʼa manonyisi ni in duk? Dibed ni isechamo olemb yien mane akweri ni kik icham?”
Ndipo anamufunsa, “Ndani anakuwuza kuti uli maliseche? Kodi wadya zipatso za mtengo umene ndinakulamulira kuti usadye?”
12 Adam nodwoke niya, “Dhako mane imiya ema nomiya olemo moko moa e yien-no kendo achamo.”
Koma munthu uja anati, “Mkazi amene munandipatsa kuti ndizikhala nayeyu anandipatsako chipatso cha mtengowo ndipo ndinadya.”
13 Eka Jehova Nyasaye nopenjo dhako niya, “Ma en angʼo ma isetimo?” Dhako nodwoke niya, “Thuol nowuonda, mi achamo olemo.”
Tsono Yehova Mulungu anati kwa mkaziyo, “Wachitachi nʼchiyani?” Mkaziyo anati, “Njoka inandinamiza, ndipo ndinadya.”
14 Kuom mano Jehova Nyasaye nowacho ne thuol niya, “Nikech isetimo ma, “Okwongʼi moloyo le duto kendo gige buya duto! Ibiro lak gi bund iyi kendo ibiro chamo buru, ndalo duto mag ngimani.
Choncho Yehova Mulungu anati kwa njokayo, “Popeza wachita zimenezi, “Ndiwe wotembereredwa kuposa ziweto zonse ndi nyama zakuthengo zonse. Udzayenda chafufumimba ndipo udzadya fumbi masiku onse a moyo wako.
15 Kendo anaket sigu e kindi gi dhako, kendo e kind kothe gi kothi; en noto wiyi, to in to nika ofunj tiende.”
Ndipo ndidzayika chidani pakati pa iwe ndi mkaziyo, pakati pa mbewu yako ndi mbewu yake; Iye adzaphwanya mutu wako ndipo iwe udzaluma chidendene chake.”
16 Dhako to ne owachone niya, “Anamedni rem malich e kindeni mag nywol; adier ininywol nyithindo gi rem. Dwaroni nobed mana kuom chwori bende enobed gi teko kuomi.”
Kwa mkaziyo Iye anati, “Ndidzachulukitsa ululu wako kwambiri pamene uli ndi pakati; ndipo udzamva ululu pa nthawi yako yobereka ana. Udzakhumba mwamuna wako, ndipo adzakulamulira.”
17 To Adam to ne owachone niya, “Nikech ne iwinjo chiegi kendo ichamo olemb yath mane akweri ni, ‘Kik icham olembe,’ “Okwongʼ lowo nikech in, kuom tich matek, ibiro chiemo koa kuom lowo, ndalo duto mag ngimani.
Ndipo kwa Adamu Mulungu anati, “Chifukwa wamvera mkazi wako ndipo wadya zipatso za mu mtengo umene ndinakulamulira kuti, ‘Usadye.’ “Nthaka yatembereredwa chifukwa cha iwe, movutikira udzadya zochokera mʼnthakamo masiku onse a moyo wako.
18 Enonyagni kit kuthe mopogore opogore kendo ibiro chamo alode manie thim.
Mʼnthakamo mudzamera minga ndi nthula ndipo udzadya zomera zakuthengo.
19 Inicham chiembi mana kuom luchi, nyaka idog e lowo nikech kanyo ema ne ogolie, nimar in lowo kendo lowo ema nidogie.”
Kuti upeze chakudya udzayenera kukhetsa thukuta, mpaka utabwerera ku nthaka pakuti unachokera kumeneko; pakuti ndiwe fumbi ku fumbi komweko udzabwerera.”
20 Adam nochako chiege ni Hawa nikech nobiro bedo min ji duto.
Munthu uja anatcha mkazi wake Hava, chifukwa iyeyu adzakhala mayi wa anthu onse amoyo.
21 Jehova Nyasaye noloso lewni mag pien ne Adam kod chiege kendo noumogi.
Yehova Mulungu anapangira Adamu ndi mkazi wake zovala zachikopa ndipo anawaveka.
22 Kendo Jehova Nyasaye nowacho niya, “Dhano koro osebedo machal kodwa, kongʼeyo ber kod rach. Kik yiene mondo oter lwete kendo okaw olemb ngima kendo ocham madimi odag nyaka chiengʼ.”
Ndipo Yehova Mulungu anati, “Tsopano munthu uyu wasanduka mmodzi wa ife, wodziwa zabwino ndi zoyipa. Iyeyu asaloledwe kutambasula dzanja ndi kutengako zipatso za mu mtengo wopatsa moyo uja kuti angakhale ndi moyo mpaka muyaya.”
23 Omiyo Jehova Nyasaye noriembe e Puodho mar Eden mondo opur lowo kamane ogole.
Kotero Yehova Mulungu anatulutsa Adamu Mʼmunda wa Edeni kuti azilima mʼnthaka imene anachokera.
24 Bangʼ kane oseriembo Adam oko, ne oketo kerubi gi ligangla mamil koni gi koni yo wuok chiengʼ mar Puodho Mar Eden mondo orit yo mochomo yadh ngima.
Atamuthamangitsa munthu uja, Yehova anayika Akerubi mbali ya kummawa kwa Munda wa Edeni ndi lupanga lamoto limene limayendayenda ponsepo, kuteteza njira ya ku mtengo wopatsa moyo.

< Chakruok 3 >