< Chakruok 29 >

1 Eka Jakobo nodhi nyime gi wuoth kendo nochopo e piny ogendini man yo wuok chiengʼ.
Yakobo anapitiriza ulendo wake kupita ku dziko la anthu a kummawa.
2 Nopo koneno soko ei pap kod kweth adek mag rombe konindo machiegni kanyo nikech kwethgo ne modho e sokono. To kidi mane nitie e dho sokono ne duongʼ.
Atafika kumeneko anaona chitsime ku busa ndipo panali magulu atatu a nkhosa zitagona pafupi ndi chitsimecho chifukwa nkhosazo zimamwetsedwa madzi ochokera mʼchitsimecho. Pamwamba pa chitsimecho panali mwala waukulu.
3 Jokwath nengʼielo kidi kane jamni osechokore kanyo mondo gimodhi. Bangʼ ka jamni duto osemodho, to ne gingʼielo kidino mondo odog oum dho soko.
Amati nkhosa zonse zikasonkhana, abusawo ankagudubuza mwalawo, kuwuchotsa ndi kumwetsa madzi nkhosazo. Kenaka ankawubwezera mwalawo pamalo pake, pakamwa pa chitsimepo.
4 Jakobo nopenjo jokwath niya, “Owetena ua kanye?” Negidwoke niya, “Waa Haran.”
Yakobo anafunsa abusawo kuti, “Abale anga, mwachokera kuti?” Iwo anayankha, “Tachokera ku Harani.”
5 Nowachonegi niya, “Bende ungʼeyo Laban nyakwar Nahor?” Negidwoke niya, “Ee, wangʼeye.”
Iye anawafunsanso kuti, “Kodi Labani, mdzukulu wa Nahori mukumudziwa?” Iwo anayankha, “Inde tikumudziwa?”
6 Eka Jakobo nopenjogi niya, “Ongima?” Negidwoke niya, “Ee, ongima, kendo mabiro gi rombe cha en Rael ma nyare.”
Ndipo Yakobo anawafunsanso, “Kodi ali bwino?” Iwo anati, “Inde ali bwino. Nayu Rakele mwana wake akubwera apoyu ndi nkhosa.”
7 Nowachonegi niya, “Neuru, piny pod chon, sa michokoe jamni podi. Weuru rombe omodhi bangʼe uduokgi e lek.”
Iye anati, “Taonani, dzuwa likanalipo ndipo nthawi yosonkhanitsa nkhosa sinakwane. Bwanji osazimwetsa madzi nkhosazi.”
8 Negidwoke niya, “Ok wanyal timo kamano kapok jokwath duto ochokore ma wangʼielo kidi manie dho soko oko mondo jamni omodhi.”
Iwo anayankha, “Ayi sitingatero. Tidikira mpaka nkhosa zonse zisonkhane. Zikatero, tigubuduza mwalawu kuwuchotsa pamwamba pa chitsimepo, kenaka nʼkuzimwetsa madzi nkhosazo.”
9 Kane pod oyudo owuoyo kodgi, Rael nochopo gi romb wuon-gi nikech en ema nokwayogi.
Ali chiyankhulire nawo, Rakele anafika ndi nkhosa za abambo ake popeza ndiye amene ankaweta nkhosazo.
10 Kane Jakobo oneno Rael, nyar Laban ner mare kod romb Laban, nodhi mongʼielo kidi oko e dho soko kendo omiyo romb ner mare omodho.
Yakobo ataona Rakele mwana wa Labani, mlongo wa amayi ake, ali ndi nkhosa za Labani, anapita nawugudubuza mwala uja nazimwetsa madzi nkhosa za amalume akezo.
11 Eka Jakobo nonyodho Rael kendo noywak gi dwol maduongʼ.
Kenaka Yakobo anapsompsona Rakele nayamba kulira mokweza.
12 Noyudo osenyiso Rael ni en wat wuon Rael kendo ni en wuod Rebeka. Kuom mano Rael nodhi monyiso wuon mare.
Kenaka Yakobo anawuza Rakele kuti iye ndi mwana wa Rebeka, mlongo wa abambo a Rakele uja. Choncho Rakele anathamanga nakawuza abambo ake.
13 To kane Laban owinjo wach mar Jakobo, wuod nyamin noringo mondo odhi oromne. Nokwake kendo omose gimor mi orwake dalane kendo Jakobo nonyise gik moko duto.
Labani atamva za Yakobo, mwana wa mlongo wake, anafulumira kukakumana naye. Anamukupatira napsompsona, napita naye ku nyumba kwake. Yakobo anafotokozera Labani zonse zinachitika.
14 Eka Laban nowachone niya, “In ringra awuon kendo remba.” Kane Jakobo ne osedak kod Laban kuom dwe achiel,
Ndipo, Labani anati kwa iye, “Iwe ndiwe ndithu fupa ndi mnofu wanga.” Yakobo anakhala ndi Labani mwezi umodzi.
15 Laban nowachone niya, “Mana nikech in watna, bende en gima ber tiyona maonge chudo? Nyisa gima dachul.”
Tsono Labani anawuza Yakobo kuti, “Zoona iwe ndi ife ndi abale. Koma suyenera kundigwirira ntchito popanda malipiro. Ndiwuze kuti malipiro ako azikhala wotani?”
16 To Laban ne nigi nyiri ariyo: nyako maduongʼ ne nyinge Lea kendo nyako matin ne nyinge Rael.
Tsono Labani anali ndi ana aakazi awiri; dzina la wamkulu linali Leya, ndipo dzina la wamngʼono linali Rakele.
17 Lea ne nigi wangʼ ma ok nenre maber, to Rael ne nigi chia kendo jaber.
Leya anali ndi maonekedwe wofowoka koma Rakele anali wa maonekedwe wokongola kwambiri.
18 Jakobo nohero Rael, kendo nowacho ni Laban niya, “Abiro tiyoni kuom higni abiriyo kuom Rael nyari matin.”
Yakobo anakonda Rakele ndipo anati, “Ndidzakugwirirani ntchito kwa zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha mwana wanu wamngʼono, Rakele.”
19 Laban nowacho niya, “Ber mondo amiyi godo moloyo chiwe ni jomoko. Koro dag mana koda ka.”
Labani anati, “Kuli bwino kuti ndimupereke kwa iwe ameneyu kusiyana ndi munthu wina. Khala ndi ine kuno.”
20 Omiyo Jakobo notiyone Laban higni abiriyo mondo oyud Rael, to hignigo nonenorene mana ka ndalo matin nikech hera manoherogo Rael.
Choncho Yakobo anagwira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele. Koma kwa iye zaka zonsezi zinakhala ngati masiku wochepa chifukwa anamukonda Rakele.
21 Eka Jakobo nowacho ne Laban, “Asetieko ndalo mane iketona, omiyo koro miya nyari mondo obed chiega.”
Kenaka Yakobo anati kwa Labani, “Nthawi yanga ndakwanitsa, ndipatseni mwana wanu kuti ndimukwatire.”
22 Kuom mano Laban noloso nyasi kendo nogwelo ji duto mae pinyno.
Pamenepo Labani anakonza phwando la ukwati, nayitana anthu onse a pamalopo.
23 To kane ochopo odhiambo, Laban nokawo nyare ma Lea mi omiyo Jakobo mondo obed chiege.
Koma pokwana usiku, Labani anatenga mwana wake wamkazi Leya namupatsa Yakobo, ndipo Yakobo anagona naye.
24 Kendo Laban nochiwo Zilpa jatichne ma nyako ne nyare, Lea, mondo obed jatichne.
Ndipo Labani anapereka wantchito wake wamkazi Zilipa kwa Leya kuti akhale wantchito wake.
25 Kane piny oru, Jakobo nofwenyo mana ni en Lea! Omiyo nopenjo Laban niya, “Angʼo momiyo isetimona kama? Donge natiyoni mondo imiya Rael? To angʼo momiyo isewuonda?”
Pakucha mmawa, Yakobo anaona kuti anagona ndi Leya. Choncho Yakobo anafunsa Labani, “Nʼchiyani mwandichitirachi? Kodi ine sindinakugwirireni ntchito chifukwa cha Rakele? Bwanji mwandinyenga?”
26 Laban nodwoke niya, “Ok en timwa mondo nyako matin okuong odhi tedo ne nyako maduongʼ.
Labani anayankha, “Si mwambo wathu kuno kupereka wamngʼono ku banja, wamkulu asanakwatiwe.
27 Rit nyaka watiek juma achiel mar nyasi mar nyakoni; eka abiro miyi Rael kiyie tiyona kuom higni abiriyo mamoko.”
Yamba watsiriza sabata ya chikondwerero cha ukwati wa Leya; kenaka ndidzakupatsanso Rakele. Koma udzayenera kundigwirira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri.”
28 Kendo Jakobo notimo kamano. Notieko jumb kend mar Lea. Eka Laban nomiye Rael nyare mondo obed chiege.
Yakobo anachitadi momwemo. Anamaliza sabata ya chikondwerero cha Leya, ndipo Labani anamupatsa Rakele kuti akhale mkazi wake.
29 Laban nochiwo Bilha jatichne ma nyako ne Rael nyare kaka jatichne.
Labani anapereka wantchito wake wamkazi Biliha kwa Rakele kuti akhale wantchito wake.
30 Jakobo nobedoe achiel gi Rael bende kendo nohero Rael moloyo Lea. Kendo notiyone Laban higni abiriyo moko kendo.
Yakobo analowana ndi mkazi wake Rakele, ndipo Yakobo anakonda Rakele kuposa Leya. Ndipo anamugwirira ntchito Labani zaka zina zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele.
31 Kane Jehova Nyasaye oneno ni Lea ne ok oher, ne oyawo iye to Rael noketo obedo migumba.
Pamene Mulungu anaona kuti Yakobo sankamukonda Leya kwambiri, Iye analola kuti Leya uja akhale ndi ana, ndi kuti Rakele akhale wosabala.
32 Lea nomako ich kendo nonywolo wuowi. Nowacho niya, “Jehova Nyasaye oseneno chandruokna, kendo koro chwora biro hera.” Omiyo nochake ni Reuben.
Leya anakhala ndi pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Anamutcha Rubeni pakuti anati, “Yehova waona kusauka kwanga. Zoonadi, mwamuna wanga adzandikonda tsopano.”
33 Nochako omako ich, monywolo wuowi moro. Nowacho niya, “Jehova Nyasaye osemiya wuowi machielo nimar nowinjo ka chwora ok ohera.” Omiyo nochake ni Simeon.
Anakhalanso ndi pathupi ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Yehova anamva kuti mwamuna wanga sakundikonda, choncho wandipatsanso mwana winayu.” Ndipo anamutcha dzina lake Simeoni.
34 Nochako omako ich, kendo ochako onywolo wuowi. Nowacho niya, “Koro chwora biro padore kuoma nikech asenywolone yawuowi adek.” Omiyo nochake ni Lawi.
Anatenganso pathupi kachitatu, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Pano pokha tidzaphatikana kwambiri ndi mwamuna wanga, chifukwa ndamubalira ana aamuna atatu.” Kotero anamutcha dzina lake Levi.
35 Nochako omako ich, kendo kane ochako onywolo wuowi nowacho niya, “Koro abiro pako Jehova Nyasaye.” Omiyo nochake ni Juda. Bangʼ mano noweyo nywolo nyithindo.
Anatenganso pathupi pena, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna, iye anati, “Nthawi ino ndidzalemekeza Yehova.” Choncho anamutcha Yuda. Kenaka analeka kubereka.

< Chakruok 29 >