< Chakruok 28 >

1 Kuom mano Isaka noluongo Jakobo mogwedhe kendo osieme konyise niya, “Kik ikend nyar jo-Kanaan.
Choncho Isake anayitanitsa Yakobo namudalitsa nʼkumuwuzitsa kuti, “Usakwatire mkazi wa kuno ku Kanaani.
2 Chak wuoth idhi Padan Aram, e od Bethuel ma kwaru. Kend achiel kuom nyi Laban ma neru.
Panopo upite ku Padanaramu, ku nyumba kwa Betueli abambo a amayi akowa, kumeneko ukakwatire mmodzi mwa ana aakazi a Labani, mlongo wa amayi akowa.
3 Mad Nyasaye Maratego gwedhi kendo inyaa mi kwanu medre nyaka ubed oganda mathoth.
Mulungu Wamphamvuzonse akudalitse iwe nakupatse ana ambiri mpaka udzasanduke gulu lalikulu la mitundu ya anthu.
4 Mad ogwedhi kod nyikwayi kaka nogwedho Ibrahim mondo ikaw piny makoro idakieni kaka jadak, ma en piny mane Nyasaye omiyo Ibrahim.”
Mulunguyo akudalitse iwe monga mmene anamudalitsira Abrahamu kuti zidzukulu zako zidzalandira dziko limene ukukhalamo ngati mlendo kuti lidzakhale lawo. Ili ndi dziko limene Mulungu anapereka kwa Abrahamu.”
5 Eka Isaka nogolo Jakobo modhi kendo Jakobo nodhi Padan Aram, ir Laban wuod Bethuel ja-Aram, owad gi Rebeka, mane min Jakobo kod Esau.
Ndipo Isake anamulola Yakobo kuti anyamuke kupita ku Padanaramu kwa Labani mwana wa Betueli Mwaramu. Labani anali mlongo wa Rebeka, mayi wa Yakobo ndi Esau.
6 Koro Esau nofwenyo ni Isaka osegwedho Jakobo kendo oseore Padan Aram mondo odhi okend kuno. Nowinjo bende ni kane Isaka gwedho Jakobo, nochike niya, “Kik ikend nyar jo-Kanaan.”
Tsopano Esau anadziwa kuti Isake anadalitsa Yakobo ndi kumutumiza ku Padanaramu kuti akakwatire kumeneko. Anawuzidwanso kuti, “Usakwatire mkazi wa ku Kanaani.”
7 Mi Jakobo nowinjo wach min gi wuon modhi Padan Aram.
Yakobo anamvera abambo ake ndi amayi ake ndi kupita ku Padanaramu.
8 Esau nofwenyo kaka Isaka wuon mare ne ok mor gi nyi jo-Kanaan.
Ndiye pamenepo Esau anazindikira kuti abambo ake Isake sankakondwera ndi akazi a ku Kanaani;
9 Kuom mano Esau nodhi ir Ishmael mi okendo Mahalath nyamin Nebayoth mane nyar Ishmael wuod Ibrahim, mondo obed chiege ewi monde mane okwongo kendo.
anapita kwa Ismaeli mwana wa Abrahamu nakwatira Mahalati mwana wa Ismaeli, mlongo wake wa Nebayoti. Anatero kuwonjezera akazi amene anali nawo kale.
10 Jakobo nowuok Bersheba kendo nodhi Haran.
Yakobo ananyamuka pa ulendo kuchoka ku Beeriseba kupita ku Harani.
11 Kane ochopo kamoro, nobworo gotieno nikech chiengʼ nosepodho. Nonindo kanyo moteno wiye gi kidi moro mane okwanyo kanyo.
Atafika pa malo pena, anayima kuti agonepo chifukwa dzuwa linali litalowa. Anatenga mwala wina pomwepo natsamiritsapo mutu wake, ndipo anagona.
12 Noleko ni oneno ngas konyono piny to wiye ochopo e polo kendo malaika mag Nyasaye ne luwe kadhi malo kendo lor piny.
Mʼmaloto, anaona makwerero oyimikidwa pansi ndipo anakafika kumwamba. Angelo a Mulungu amakwera ndi kutsika pa makwereropo.
13 To ewi ngasno gi malo Jehova Nyasaye nochungʼie kawacho niya, “An Jehova Nyasaye Nyasach wuonu Ibrahim kendo Nyasach Isaka. Piny minindoeni abiro miyi gi nyikwayi.
Tsono Yehova anayimirira pambali pake, nati, “Ine ndine Yehova, Mulungu wa Abrahamu kholo lake la Isake abambo ako. Ndidzakupatsa iwe ndi zidzukulu zako dziko limene ukugonamolo.
14 Nyikwayi nobed mangʼeny ka kwoyo, kendo unudag koa yo podho chiengʼ nyaka wuok chiengʼ, bende koa yo nyandwat nyaka yo milambo. Ogendini duto manie piny nogwedh kokadho kuomi kod nyikwayi.
Zidzukulu zako zidzachuluka ngati fumbi la pa dziko lapansi ndipo zidzabalalikira kumadzulo ndi kummawa, kumpoto ndi kummwera. Anthu onse adzalandira madalitso kudzera mwa iwe ndi zidzukulu zako.
15 Anabed kodi kendo anariti kamoro amora ma idhiye nyaka adwoki e pinyni. Ok anaweyi nyaka chop atim mana ma asesingorani.”
Ine ndili nawe pamodzi ndipo ndidzakuyangʼanira kulikonse upiteko, ndipo ndidzakubwezera ku dziko lino. Sindidzakusiya mpaka nditachita zimene ndakulonjezazi.”
16 Kane Jakobo ochiewo oa e nindo, noparo niya, “Adier Jehova Nyasaye nika kendo ne ok angʼeyo.”
Yakobo atadzidzimuka, anati, “Zoonadi Yehova ali pa malo ano, ndipo ine sindinadziwe.”
17 Luoro nomake mi owacho niya, “Ma kama lich manade! Nyaka bedni ma en od Nyasaye; ma en dhoranga polo.”
Tsono anachita mantha ndipo anati, “Malo ano ndi woopsa ndithu. Zoonadi pano ndi pa nyumba ya Mulungu ndi khomo la kumwamba.”
18 Kinyne gokinyi mangʼich Jakobo nokawo kidi mane otenogo wiye kendo nochunge ka siro mi oolo mo e wiye.
Mmamawa mwake Yakobo anatenga mwala umene anatsamira mutu wake uja nawuyimika ngati chipilala ndi kuthira mafuta pamwamba pake
19 Nochako kanyo ni Bethel to kinde mokwongo nying dalano niluongo ni Luz.
Iye anawatcha malowo Beteli, ngakhale kuti poyamba mzindawo ankawutcha Luzi.
20 Eka Jakobo nokwongʼore kawacho niya, “Ka Nyasaye nobed koda kendo norita e wuodhani ma adhiye kendo miya chiemo ma achamo kod lewni ma arwako,
Pamenepo Yakobo analumbira kwa Yehova nati, “Ngati inu Mulungu mukhala ndi ine, kundiyangʼanira pa ulendo wangawu ndi kundipatsa chakudya ndi chovala;
21 mi anadogi maber e od wuora eka Jehova Nyasaye nobed Nyasacha,
ngati inu mudzandibweretsa kwathu mu mtendere, ndiye kuti mudzakhala Mulungu wanga,
22 kendo kidi ma asechungo kaka sironi, nobed od Nyasaye kendo duto ma imiya, namiyi achiel kuom apar.”
ndipo mwala uwu ndawuyimikawu udzakhala Nyumba ya Mulungu. Ine ndidzakupatsani chakhumi cha zinthu zonse zimene mudzandipatse.”

< Chakruok 28 >