< Chakruok 17 >

1 Kane Abram ne ja-higni piero ochiko gochiko, Jehova Nyasaye nofwenyorene mi nowachone niya, “An Nyasaye Maratego; bed ngʼama odimbore e nyima kendo maonge ketho.
Pamene Abramu anali ndi zaka 99, Yehova anamuonekera nati, “Ine ndine Mulungu Wamphamvuzonse. Ukhale munthu wochita zolungama nthawi zonse.
2 Abiro guro singruokna e kinda kodi kendo anamed kothi obed mangʼeny.”
Ndipo Ine ndikulonjeza kuti ndidzakupatsa zidzukulu zambiri.”
3 Abram nopodho auma e nyim Nyasaye kendo Nyasaye nowachone niya,
Pomwepo Abramu anadziponya pansi ndipo Mulungu anati kwa iye,
4 “Singruok matimo kodi ema: Inibed wuon ogendini mangʼeny.
“Pangano langa ndi iwe ndi ili: Udzakhala kholo la mitundu yambiri ya anthu.
5 Ok nochak oluongi ni Abram; to enoluongi ni Ibrahim, nimar aseketi ibedo wuon ogendini mangʼeny.
Sudzatchedwanso Abramu; dzina lako lidzakhala Abrahamu, chifukwa ndakusandutsa kukhala kholo la mitundu yambiri ya anthu.
6 Anamiyi nyikwayo mathoth; ginidog ogendini madongo kendo ruodhi nowuog kuomgi.
Ndidzakupatsa zidzukulu zambiri motero kuti mitundu yambiri ya anthu idzatuluka mwa iwe. Mafumunso adzatuluka mwa iwe.
7 Anagur singruokna manyaka chiengʼ e kinda kodi gi nyikwayi kod tienge mabiro, mi anabed Nyasachi kendo Nyasach nyikwayi nyaka chiengʼ.
Pangano langa ndi iwe pamodzi ndi zidzukulu za mibado ya mʼtsogolo lidzakhala la muyaya. Ndidzakhala Mulungu wako ndi Mulungu wa zidzukulu zako.
8 Piny Kanaan duto makoro udakieni anamiyi kaachiel gi nyikwayi mondo obed girkeni manyaka chiengʼ kendo anabed Nyasachgi.”
Dziko lonse la Kanaani, limene iwe ukukhala tsopano, ndalipereka kwa iwe ndi kwa zidzukulu zako kuti likhale chuma chanu mpaka muyaya. Ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wa zidzukulu zako.”
9 Eka Nyasaye nowacho ne Ibrahim niya, “In kaachiel gi nyikwayi kod tienge mabiro nyaka rit singruokna.
Kenaka Mulungu anati kwa Abrahamu, “Koma iwe pamodzi ndi zidzukulu zako zobwera pambuyo pako mʼmibado ya mʼtsogolomo, sungani pangano langali.
10 Singruokna manyaka iriti, in kaachiel gi nyikwayi ema: Ngʼato ka ngʼata madichwo e kindu nyaka ter nyangu.
Iwe pamodzi ndi zidzukulu zako zobwera pambuyo pako muzisunga pangano ili loti mwamuna aliyense pakati panupa azichita mdulidwe.
11 Nyaka teru nyangu kendo ma nobed ranyisi mar singruokna e kinda kodu.
Kuyambira tsopano muzichita mdulidwe ndipo ichi chidzakhala chizindikiro cha pangano langa ndi iwe.
12 Kuom tienge mabiro ngʼato angʼata madichwo monywol e uteu kata ongʼiew gi pesa ma ok kothu nyaka ter nyangu, e odiechiengʼ mar aboro bangʼ nywolne.
Kuyambira tsopano mpaka mibado ya mʼtsogolomo mwana wamwamuna aliyense pakati panu amene wakwana masiku asanu ndi atatu ayenera kuchita mdulidwe. Awa ndi ana obadwa mʼbanja lako, kapena akapolo ochita kugula ndi ndalama, mlendo osakhala wa mʼmbumba yako.
13 Nyaka tergi nyangu bedni onywolgi e uteu kata ongʼiewogi gi pesa. Singruokna man kuom ringreu nyaka bed mosiko.
Achite mdulidwe ndithu mwana wamwamuna aliyense, mbadwa ngakhale kapolo wochita kugula ndi ndalama, ndipo ichi chidzakhala chizindikiro pa thupi lanu cha pangano langa lamuyaya.
14 Ngʼato angʼata madichwo, mane ok oter nyangu e ringruok, nogol oko kuom jogi; nikech oseketho singruokna.”
Mwamuna aliyense amene adzakhala wosachita mdulidwe adzachotsedwa pakati pa anthu ake chifukwa sanasunge pangano langa.”
15 Nyasaye nomedo wachone Ibrahim niya, “Koro ok inichak iluong Sarai chiegi ni Sarai, to iniluonge ni Sara.
Mulungu anatinso kwa Abrahamu, “Sarai mkazi wako, sudzamutchanso Sarai; dzina lake lidzakhala Sara.
16 Anagwedhe kendo anamiyi nyathi ma wuowi koa kuome. Anagwedhe mi nobed min ogendini; kendo ruodhi mag ogendini noa kuome.”
Ndidzamudalitsa ndipo adzakubalira mwana wamwamuna. Ndidzamudalitsa kuti akhale mayi wa mitundu ya anthu; mafumu a anthuwo adzachokera mwa iye.”
17 Ibrahim nopodho auma; monyiero kowacho e chunye niya, “Bende ngʼama ja-higni mia achiel nyalo nywolo wuowi? Bende Sara ma ja-higni piero ochiko nyalo nywolo nyathi?”
Abrahamu anadzigwetsa pansi pamaso pa Yehova, Iye anaseka nati, “Kodi munthu wa zaka 100 nʼkubala mwana? Kodi Sara adzabereka mwana pa msinkhu wa zaka makumi asanu ndi anayi?”
18 Kendo Ibrahim nowacho ne Nyasaye niya, “Mano nyalo mana timore kaponi Ishmael odak e bwo ngʼwono mari!”
Ndipo Abrahamu anati kwa Mulungu, “Bwanji mumudalitse Ismaeli.”
19 Eka Nyasaye nodwoke niya, “Ooyo, en mana Sara chiegi ema nonywolni wuowi, kendo iniluong nyinge ni Isaka. Anaket singruokna kode kaka singruok manyaka chiengʼ ne nyikwaye.
Koma Mulungu anati, “Ayi, koma mkazi wako Sara adzakubalira mwana wamwamuna, ndipo udzamutcha Isake. Ndidzasunga pangano langa losatha ndi iyeyu komanso ndi zidzukulu zobwera pambuyo pake.
20 To bende asewinjo kwayo mikwayo nikech Ishmael, omiyo anagwedhe, kendo anamiye nyithindo gi nyikwayo mangʼeny.
Koma za Ismaeli, ndamva. Ndidzamudalitsadi, ndipo adzakhala ndi zidzukulu zambiri. Iye adzakhala kholo la mafumu khumi ndi awiri ndipo mwa iye mudzatuluka mtundu waukulu wa anthu.
21 Makmana singruokna abiro chopo gi Isaka ma Sara biro nywolone e kinde maka ma e higa mabiro.”
Koma ndidzasunga pangano langali ndi Isake amene Sara adzakubalira pofika nthawi ngati ino chaka chamawa.”
22 Kane Nyasaye osetieko wuoyo kod Ibrahim, noweye modhi.
Atatha kuyankhula, Mulungu anamuchokera Abrahamu.
23 E odiechiengno Ibrahim nokawo wuode Ishmael kod jogo duto machwo monywol e ode kata mane ongʼiewo gi pesa, kendo noterogi nyangu, mana kaka Nyasaye nonyise.
Tsono Abrahamu anachita mdulidwe mwana wake Ismaeli ndi onse amene anali mʼbanja lake, mbadwa ngakhale kapolo ochita kugula ndi ndalama, monga mmene Mulungu analamulira.
24 Ibrahim ne ja-higni piero ochiko gochiko kane otere nyangu,
Abrahamu anali ndi zaka 99 pamene anachita mdulidwe,
25 to wuode Ishmael ne ja-higni apar gadek.
ndipo mwana wake Ismaeli anali ndi zaka khumi ndi zitatu;
26 Ibrahim kod wuode Ishmael noter nyangu odiechiengno.
Onse, Abrahamu ndi mwana wake Ismaeli, anachita mdulidwe tsiku limodzi.
27 Kendo chwo duto mane ni e od Ibrahim, kaachiel gi monywol e ode kata ma ongʼiewo, bende noter nyangu kode.
Aliyense wamwamuna wa pa banja pa Abrahamu, kuphatikizapo iwo amene anabadwira pa banja pomwepo kapena akapolo ogula ndi ndalama kwa alendo, anachita mdulidwe.

< Chakruok 17 >