< Rapar Mar Chik 4 >

1 Yaye, jo-Israel, winjuru buche kod chike ma amiyou, luwgi mondo udagi kendo mondo ukaw piny ma Jehova Nyasaye, ma Nyasach kwereu miyou.
Mverani inu Aisraeli, malangizo ndi malamulo amene ndikuphunzitseni. Muwatsatire kuti mukhale ndi moyo ndi kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu akukupatsani.
2 Kik umedi kata ugol gimoro amora kuom chik ma amiyou, to rituru chike ma amiyou mag Jehova Nyasaye ma Nyasachu.
Musawonjezere pa zimene ndikukulamulirani ndipo musachotserepo, koma muwasunge malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani.
3 Ne uneno gi wengeu uwegi gima Jehova Nyasaye ne otimo Baal Peor. Jehova Nyasaye ma Nyasachu notieko koa kuomu jogo duto mane oluwo Baal mar Peor,
Inu munaona ndi maso anu zimene Yehova anachita ku Baala-Peori. Yehova Mulungu wanu anawononga aliyense amene anatsata Baala wa ku Peori pakati panu.
4 to ne un uduto mane usiko kupadoru kuom Jehova Nyasaye ma Nyasachu pod ungima nyaka chil kawuono.
Koma inu nonse amene munagwiritsitsa Yehova Mulungu wanu mukanali ndi moyo mpaka lero.
5 Ne, asepuonjou buche kod chike kaka ne Jehova Nyasaye ma Nyasacha nochika, mondo uluw chikenego e piny mudhidonjoe kendo kawo.
Taonani, ndakuphunzitsani malangizo ndi malamulo monga Yehova Mulungu wanga anandilamulira kuti inuyo muwatsatire mʼdziko limene mukulowa ndi kulitengali.
6 Ritgiuru maber, nimar mano ema biro nyiso riekou gi ngʼeyou ni ogendini mamoko mabiro winjo buchegi duto wach niya, “Adier, onge oganda mariek kendo man-gi ngʼeyo koganda maduongʼni.”
Muwasunge mosamalitsa pakuti zimenezi zidzaonetsa nzeru zanu ndi kuzindikira kwanu kwa anthu a mitundu ina, amene adzamva za malangizo onsewa nati, “Ndithudi, mtundu waukulu uwu ndi wa anthu anzeru ndi ozindikira.”
7 Ere oganda machielo ma ogen man kod nyasachgi machiegni e yo ma Jehova Nyasaye ma Nyasachwa chiegnigo kodwa e yo moro amora ma walame?
Mtundu wina wa anthu ndi uti umene uli waukulu chomwechi, woti ukhoza kukhala ndi milungu yawo pafupi monga mmene alili Yehova Mulungu wathu ndi ife nthawi zonse pamene tipemphera kwa Iye?
8 Kara ere oganda machielo maduongʼ man kod buche gi chike makare machal gi chike mamiyou kawuononi?
Ndipo ndi mtundu uti mwa mitundu ya anthu umene ndi waukulu chotere kuti nʼkukhala ndi malangizo ndi malamulo olungama ngati malamulo amene ndikuyika pamaso panu lero?
9 Beduru motangʼ kendo neuru ni wiu ok owil gi gik museneno gi wangʼu kendo kik uwegi gia e chunyu ka pod ungima. Puonjuru nyithindu kod nyikwau wechegi.
Inu mungosamala ndi kudziyangʼanira kwambiri nokha kuti musayiwale zimene maso anu aona. Musalole kuti zichoke mʼmitima mwanu pa moyo wanu wonse. Zimenezi muziphunzitse kwa ana anu ndi zidzukulu zanu ngakhale mʼtsogolo.
10 Paruruane chiengʼ mane uchungʼ e nyim Jehova Nyasaye ma Nyasachu e Horeb, kane owachona niya, “Chok ji e nyima ka mondo giwinj wechena mondo mi gipuonjre luora ndalo duto mag ngimagi kendo bende gipuonj nyithindgi wechegi.”
Kumbukirani tsiku limene munayimirira pamaso pa Yehova Mulungu wanu ku Horebu, pamene anati kwa ine, “Sonkhanitsa anthu pamaso panga kuti amve mawu anga ndi kuti aphunzire kundilemekeza mʼmoyo wawo onse mʼdzikomo ndi kuti ana awo aziwaphunzitsa zimenezi.”
11 Ne ubiro machiegni ma uchungʼ e tiend got. Godno mach ne liele mochopo nyaka e polo, ka en-gi rumbi maratengʼ kod mudho mandiwa.
Munabwera pafupi ndi kuyima pa tsinde pa phiri pamene phirilo limayaka moto umene umafika mpaka kumwamba. Panalinso mtambo wakuda ndi mdima wambiri.
12 Eka Jehova Nyasaye ne owuoyonu kokalo ei mach. Ne uwinjo dwol kawuok ei mach, to ne ok uneno ngʼat mane wuoyono, to makmana dwol kende ema nuwinjo.
Kenaka Yehova anayankhula nanu kuchokera mʼmotowo. Inu munamva mawu ake okha koma simunamuone pakuti panali mawu chabe.
13 Ne owachonu singruokne, ma gin Chike Apar, mane ochikou mondo uluw kendo ne ondikogi e kite mopa ariyo.
Iye anakuwuzani Malamulo Khumi omwe ndi pangano lake limene anakulamulirani kuti mutsatire. Ndipo anawalemba malamulowo pa mapale awiri a miyala.
14 Kendo Jehova Nyasaye ne owachona e kindeno mondo apuonju buche kod chike ma onego uluw e piny ma udhiye loka Jordan mondo ukaw.
Ndipo Yehova anandilamula nthawi imene ija kuti ndikuphunzitseni malangizo ndi malamulo amene muyenera kutsata mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani.
15 Ne ok uneno Jehova Nyasaye gi wangʼu e kinde mane uwinjo dwonde koa e mach e got Horeb. Omiyo beduru motangʼ ahinya,
Tsiku limene Yehova anayankhula nanu ku Horebu mʼmoto uja, simunaone thupi lake. Choncho mudziyangʼanire nokha mosamalitsa,
16 mondo kik ubed jo-mibadhi ka uloso nyisecheu uwegi, kata kido moro amora mochwe ka dichwo kata ka dhako,
kuti musasokonezeke ndi kudzipangira nokha fano kapena chifanizo cha mtundu uliwonse, kaya chokhala ngati mwamuna kapena ngati mkazi,
17 kata ka chiayo moro e piny kata ka winyo mafuyo e kor polo,
kaya chokhala ngati nyama iliyonse ya pa dziko lapansi kapena mbalame iliyonse yowuluka mlengalenga.
18 kata ka gimoro amora mochwe mamol e lowo kata ka rech manie pi.
Kapena cholengedwa chilichonse choyenda pa nthaka kapena nsomba ya mʼmadzi akuya.
19 Ka ungʼiyo polo ma uneno chiengʼ, dwe kod sulwe karieny (ma gin gigo manyiso duongʼ mar polo), to kik gimak pachu mi ukulrunegi ka ulamo. Gin gigo ma Jehova Nyasaye ma Nyasachu osemiyo jopinje duto manie piny bwo polo.
Ndipo pamene muyangʼana kumwamba muona dzuwa, mwezi ndi nyenyezi, zonse zakumwambazo musakopeke kuti muzigwadire ndi kumapembedza zinthu zimene Yehova wapereka kwa anthu a mitundu yonse pa dziko lapansi.
20 To un, Jehova Nyasaye noresou mogolou e mach mager kuwuok e piny Misri mondo ubed kaka girkeni mare nyaka chiengʼ, mana kaka un sani.
Koma inuyo, Yehova anakutengani ndi kukutulutsani mʼngʼanjo yosungunulira zitsulo, ku Igupto kuti mukhale anthu olandira chuma chake monga mmene mulili tsopano.
21 Jehova Nyasaye nokecho koda nikech un, kendo ne okwongʼoreni ok anangʼad aora Jordan mondo adonji e piny maber ma Jehova Nyasaye ma Nyasachu miyou ka girkeni.
Yehova anakwiya nane chifukwa cha inu, ndipo analumbira kwathunthu kuti sindidzawoloka Yorodani ndi kulowa mʼdziko labwinolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani inu ngati cholowa chanu.
22 Abiro tho e pinyni, ok anangʼad aora Jordan, to un uchiegni ngʼado mondo udhi ukaw kereu e piny maberno.
Ine ndifera mʼdziko lino, sindiwoloka Yorodani. Koma inu mwatsala pangʼono kuwoloka ndi kukatenga dziko labwinolo.
23 Beduru motangʼ mondo kik wiu wil gi singruok mane Jehova Nyasaye ma Nyasachu otimo kodu, kik ulos ne un uwegi kido moro amora milamo ma Jehova Nyasaye ma Nyasachu okwero.
Samalani, musayiwale pangano limene Yehova Mulungu wanu anapangana nanu ndipo musadzipangire nokha fano la chinthu chilichonse chimene Yehova Mulungu wanu waletsa.
24 Nimar Jehova Nyasaye ma Nyasachu en mach matieko gik mowangʼo kendo en Nyasaye ma janyiego.
Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi moto wonyeketsa ndipo ndi Mulungu wansanje.
25 Bangʼ ka usedak e pinyno kuom higni mangʼeny mi ubedo gi nyithindo kod nyikwau, bangʼe ubedo jo-mibadhi ma uloso kido mopa kendo utimo gik mamono e wangʼ Jehova Nyasaye ma Nyasachu, ka umiye mirima;
Mukadzakhala nthawi yayitali mʼdzikomo ndi kubereka ana ndi kukhala ndi zidzukulu ndipo mukadzasokonekera ndi kupanga fano la mtundu uliwonse, nʼkumachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kumukwiyitsa,
26 to aluongo polo gi piny mondo obed joneno kuomu kawuono, ni ubiro rumo mapiyo nono e piny ma ubiro kawo loka Jordan.
ine ndi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni lero zokutsutsani kuti mudzawonongedwa msanga ndipo mudzachotsedwa mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani. Simudzakhalitsa kumeneko koma mudzawonongedwa ndithu.
27 Jehova Nyasaye biro keyou e dier ogendini kendo ji manok kuomu ema notony e kind pinje ma Jehova Nyasaye noterue.
Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu ena. Ochepa okha pakati panu ndi amene adzapulumuke pakati pa anthu a mitundu ina kumene Yehova adzakupirikitsireniko.
28 Kuno unulamie gik ma dhano oloso gi lwetgi, ma gin nyiseche molos gi bao kata gi kite mopa, gin gik ma ok nyal neno, winjo, chiemo kata winjo tik gimoro.
Kumeneko mudzapembedza milungu ya mitengo ndi miyala yopangidwa ndi anthu, imene singaone kapena kumva kapena kudya kapena kununkhiza.
29 To ka udwaro Jehova Nyasaye ma Nyasachu kanyo, to unuyude ka umanye gi chunyu duto kod ngimau duto.
Mukanali komweko, ngati mudzamufunafuna Yehova Mulungu wanu mudzamupeza koma ngati mutamufunafuna ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
30 Bangʼ ka gigi duto osetimorenu mi ubedo gi chuny mool, eka unuduog ir Jehova Nyasaye ma Nyasachu kendo uluore.
Mukadzakhala pa chipsinjo ndipo zonsezi zikadzakuchitikirani, ndi pamene pambuyo pake mudzabwerera kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera Iye.
31 Nimar Jehova Nyasaye ma Nyasachu en Nyasaye ma jangʼwono ok enojwangʼu kata tiekou kata wiye wil kod singruok mane otimo gi kwereu kokwongʼore.
Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wachifundo, Iye sadzakutayani kapena kukuwonongani kapena kuyiwala pangano lake ndi makolo anu, limene analitsimikiza mwa lumbiro.
32 Penj ane sani gik mane timore chon, ndalo mane pok onywolu, kochakore e ndalo mane Nyasaye ochweyo dhano e piny; penj ane koa e bath polo konchiel nyaka komachielo. Bende gima duongʼ kama osetimore kata gima chal kama osewinji?
Tsopano tafunsani za masiku a mʼmbuyomu, zakale inu musanabadwe, kuyambira tsiku limene Mulungu analenga munthu pa dziko lapansi. Tafufuzani kuyambira kumapeto mpaka mapeto anzake a thambo. Kodi chinachitikako china chachikulu ngati ichi, kapena chinayamba chamvekako chokhala ngati ichi?
33 Bende nitie oganda moro mosewinjo dwond Nyasaye kawuoyo e mach kaka usewinjoni ma obedo mangima?
Kodi uliponso mtundu wina wa anthu umene unamva mawu a Mulungu akuyankhula kuchokera mʼmoto nʼkukhala ndi moyo monga mwachitira inumu?
34 Bende nitiere nyasaye moro mosegolo oganda kuom oganda machielo moselok wasumbini? Koso bende nitiere moro mosetemo timo timbe madongogi gi ranyisi, honni gi lweny kendo gi teko maduongʼ kod bat morie kaka Jehova Nyasaye notimonu e piny Misri e wangʼu kuneno.
Kodi alipo mulungu amene anayeserapo kudzitengera mtundu wa anthu kuwachotsa mu mtundu unzake mwa mayesero, zizindikiro zozizwitsa, nkhondo, komanso mwa mphamvu zake zopanda malire, kapena mwa zochita zazikulu ndi zochititsa mantha, monga zimene Yehova Mulungu wanu anakuchitirani ku Igupto inu mukupenya?
35 Osenyisu gigi duto mondo ungʼe ni Jehova Nyasaye en Nyasaye; onge Nyasaye moro ma ok en.
Iye anakuonetsani zonsezi kuti inu muzindikire kuti Yehova ndiye Mulungu, palibenso wina wofanana naye.
36 Noyie uwinjo dwonde gie polo mond opuonjugo. Bende noyienu ma uneno mach makakni e piny, kendo nuwinjo dwonde ei majno.
Kuchokera kumwamba, Iye anafuna kuti inu mumve mawu ake ndi kuti mukhale osunga mwambo. Pa dziko lapansi anakuonetsani moto waukulu, ndipo inu munamva mawu ake kuchokera mʼmotomo.
37 Nikech ne ohero kwereu mi oyiero nyikwagi bangʼ-gi, ne ogolou Misri en owuon kod tekone maduongʼ,
Popeza anakonda makolo anu ndi kusankha adzukulu awo, a pambuyo pawo, anakutulutsani kuchoka ku Igupto ali pakati panu ndi mphamvu yake,
38 mondo ogol oko ogendini maroteke moloyou, kokelou e pinygi mondo omiu bedo girkeni kaka en kawuononi.
kuti akupirikitsireni mayiko akuluakulu ndi amphamvu kuposa inu, ndi kukubweretsani inu ku dziko lawo kuti likhale lanu, monga liliri lero.
39 Yie kendo ikaw odiechiengni obed ei chunyi ni Jehova Nyasaye en Nyasaye e polo malo kendo e piny mwalo. Onge Nyasaye moro machielo.
Vomerezani lero ndipo dziwani mu mtima mwanu kuti Yehova ndiye Mulungu kumwamba ndi pa dziko lapansi. Palibenso wina.
40 Emomiyo rituru buchene kod chikene ma amiyou kawuono, mondo gik moko odhi maber kodu gi nyithindu kendo mondo udag amingʼa e piny ma Jehova Nyasaye ma Nyasachu miyou e kinde duto e piny.
Sungani malangizo ake ndi malamulo ake amene ndikukupatsani lero lino, kuti zikuyendereni bwino inu ndi ana anu kutsogoloko, ndi kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kwa nthawi zonse.
41 Eka Musa noketo tenge mier adek madongo man yo wuok chiengʼ mar aora Jordan,
Kenaka Mose anapatula mizinda itatu cha kummawa kwa Yorodani,
42 ma gin kuonde ma ka ngʼato onego wadgi ka ok ochano, to onyalo ringo dhi pondo kuondego mantie e miechgi madongo mondo ores ngimane.
kumene aliyense amene wapha munthu akhoza kuthawirako ngati wopha munthuyo sanaphe mnzakeyo mwadala ndi maganizo oyipa. Iye akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizinda imeneyi napulumutsa moyo wake.
43 Mier madongo-go gin magi: Bezer manie pinje gode motwo, mano ne jo-Reuben; Ramoth ei Gilead, obed kar jo-Gad; kendo Golan ei Bashan obed mar jo-Manase.
Mizindayo inali iyi: ku fuko la Rubeni, unali mzinda wa Bezeri ku mapiri a ku chipululu; ku fuko la Gadi, unali Ramoti ku Giliyadi; ndipo ku fuko la Manase, unali Golani ku Basani.
44 Ma e chik mane Musa omiyo jo-Israel.
Awa ndi malamulo amene Mose anapereka kwa Aisraeli.
45 Magi e weche, buche kod chike mane Musa omiyogi kane giwuok Misri,
Izi ndi ndondomeko, malangizo ndi malamulo amene Mose anawapatsa iwo pamene anatuluka ku Igupto.
46 kane gin e holo machiegni gi Beth Peor man yo wuok chiengʼ mar Jordan, e piny Sihon ruodh jo-Amor mane nigi loch Heshbon kendo ne oloye gi Musa kod jo-Israel kane giwuok Misri.
Anali ku chigwa cha kufupi ndi Beti-Peori mbali ya kummawa kwa Yorodani, mʼdziko la Sihoni mfumu ya Aamori amene ankalamulira ku Hesiboni ndipo anagonjetsedwa ndi Mose ndi Aisraeli pamene ankachokera ku Igupto.
47 Negikawo pinye gi piny Og ruodh Bashan, mane gin gi ruodhi ariyo mag jo-Amor man loka yo wuok chiengʼ mar Jordan.
Iye anamulanda dziko lake ndi dziko la Ogi mfumu ya ku Basani. Awa anali mafumu awiri Aamori a kummawa kwa Yorodani.
48 Pinyni nochakore Aroer koa e dier holo mar Arnon mochopo nyaka Got Siyon (tiende ni, Hermon),
Dziko ili linayambira ku Aroeri cha kumphepete kwa khwawa la Arinoni ku phiri la Siyoni (limeneli ndi phiri la Herimoni),
49 kendo nokawo gwenge mag Araba man yo wuok chiengʼ mar Jordan, mochopo nyaka Nam mar Araba mantiere e tiend gode mag Pisga.
ndi kuphatikizapo dziko lonse la Araba cha kummawa kwa Yorodani mpaka kukafika ku Nyanja ya Araba, kumunsi kwa Phiri la Pisiga.

< Rapar Mar Chik 4 >