< Rapar Mar Chik 30 >

1 Ka gweth kata kwongʼ-gi ma aseketo e nyimu obironu kendo uketogi e chunyu kamoro amora ma Jehova Nyasaye ma Nyasachu nokewu e kind pinje,
Madalitso ndi matemberero awa onse amene ndawayika pamaso panu akadzafika pa inu, inu nʼkukumbukira kulikonse kumene Yehova Mulungu wanu wakubalalitsirani pakati pa mitundu ya anthu,
2 kendo ka un kod nyithindu udwogo ir Jehova Nyasaye ma Nyasachu ka uchiwo ne luor kod chunyu duto gi ngimau duto ma achikou kawuono,
ndipo inu pamodzi ndi ana anu nʼkudzatembenukira kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse molingana ndi chilichonse chimene ndakulamulani lero lino,
3 eka Jehova Nyasaye ma Nyasachu biro chopo gweth mare kuomu obiro bedo gi miwafu ne un ma ochoku duto ka uwuok e pinje duto mane okeyoue.
pamenepo Yehova Mulungu wanu adzakukhalitsani monga kale ndi kukuchitirani chifundo, ndipo adzakusonkhanitsani kukuchotsani ku mitundu ina ya anthu kumene anakubalalitsirani.
4 Kata bed nine ojwangʼu e piny mabor ahinya e bwo polo ka, koa kuno Jehova Nyasaye ma Nyasachu biro chokou mi duogu uduto.
Ngakhale atakupirikitsirani ku malekezero a dziko lapansi, adzakusonkhanitsani kuchokera kumeneko ndi kukubweretsaninso.
5 Obiro kelou e piny mane mar kwereu, mi unukawe. Enomi ubed gi mwandu bende ununyaa mangʼeny maloyo kaka ne kwereu romo.
Adzakubweretsani ku dziko limene linali la makolo anu, ndipo lidzakhala lanu. Iye adzakulemeretsani ndi kukuchulukitsani kupambana makolo anu.
6 Jehova Nyasaye ma Nyasachu nopwodh chunyu kod chuny nyikwau mondo uhere gi chunyu duto kod ngimau duto mondo udagi amingʼa.
Yehova Mulungu wanu adzasintha mitima yanu pamodzi ndi mitima ya zidzukulu zanu, kotero kuti mudzamukonda ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse, ndipo mudzakhala ndi moyo.
7 Jehova Nyasaye ma Nyasachu noket kwongʼ-gi duto ne wasiku ma ochayou kendo sandou.
Yehova Mulungu wanu adzayika matemberero awa onse pa adani anu amene amadana nanu ndi kukuzunzani.
8 Ubiro chiwo luor ne Jehova Nyasaye kendo mako chikene duto ma amiyou kawuono.
Inu mudzamveranso Yehova ndi kutsatira malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino.
9 Eka Jehova Nyasaye ma Nyasachu biro miyou mwandu e tije lweteu duto kod nyak mag kothu, nyiroye mag dhou kod cham mag piny. Jehova Nyasaye nobed mamor kodu kendo mi uchak uyud mwandu, mana kaka ne otimo ne kwereu,
Pamenepo Yehova Mulungu wanu adzakulemeretsani pa zochita zanu zonse ndipo adzakupatsani ana ambiri, zoweta zambiri, ndiponso mudzakhala ndi zokolola zambiri za mʼdziko lanu. Yehova adzakondwera nanunso ndi kukulemeretsani monga momwe anakondwera ndi makolo anu,
10 ka uchiwo luor ne Jehova Nyasaye ma Nyasachu kendo rito chikene kod buchene ma ondiki e kitabuni kendo udwogo ir Jehova Nyasaye ma Nyasachu gi chunyu duto kod ngimani duto.
ngati mudzamvera Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ake ndi mawu ake amene alembedwa Mʼbuku ili la Malamulo ndi kutembenukira kwa Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
11 Chik ma amiyou kawuononi ok en chik matek to bende ok en kuma bor ma ok unyal chopoe.
Tsopano zimene ndikukulamulirani leroli sizovuta kapena zapatali.
12 Ok enie polo malo madimi uwach niya, “Ere ngʼama didhinwa e polo malo mondo oomnwago kendo opuonjwa eka warite?”
Sizili kumwamba, kuti muzichita kufunsa kuti, “Kodi ndani amene akwere kumwamba kuti akazitenge ndi kudzatilalikira kuti timvere?”
13 Bende ok en loka nam, madimi upenj niya, “En ngʼa madingʼad loka nam mondo oomnwago kendo opuonjwa eka warite?”
Komanso sizili pa tsidya la nyanja, kuti muzichita kufunsa kuti, “Kodi ndani amene adzawoloke nyanja kuti akatenge ndi kudzatilalikira kuti timvere?”
14 Ooyo, wach ni machiegni kodu, en mana e dhou kendo e chunyu omiyo unyalo rite.
Ayi, mawu ali pafupi ndi inu; ali mʼkamwa mwanu ndi mu mtima mwanu kuti muwamvere.
15 Neuru, kawuono aketo e nyimu ngima kod mwandu, tho kod kethruok.
Taonani, lero ine ndayika pamaso panu moyo ndi zokoma, imfa ndi chiwonongeko.
16 Nimar achikou kawuono mondo uher Jehova Nyasaye ma Nyasachu, kuwuotho e yorene kendo urito buchene kod chikene, eka unudag mi umedru mangʼeny kendo Jehova Nyasaye ma Nyasachu nogwedhu e piny ma udonjoe mondo ukaw kaka girkeni.
Pakuti lero ndikukulamulani kuti mukonde Yehova Mulungu wanu, kuti muyende mʼnjira zake, ndi kusunga malamulo ake, malangizo ake. Mukatero mudzakhala ndi moyo ndi kuchulukana, ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene mukulowa kukakhalamo.
17 To ka chunyu odagi ma ok uchiwo luor kendo ka uwuok ma ukuloru ne nyiseche mamoko mi ulamogi,
Koma ngati mtima wanu udzatembenuka, inu nʼkukhala osandimvera, ndipo ngati mudzatengeka ndi kupita kukagwadira milungu ina ndi kuyipembedza,
18 to awachonu kawuononi ni nyaka notieku. Ok unudag amingʼa e piny ma ubiro donjoe mondo ukaw ka usengʼado aora Jordan.
lero ndikulengeza kwa inu kuti mudzawonongeka ndithu. Simudzakhala nthawi yayitali mʼdziko limene mukulowamo pamene mukuwoloka Yorodani kuti mulitenge.
19 Kawuononi aluongo polo gi piny mondo obed joneno ni aseketo gik moko ariyo e nyimu ma gin ngima gi gweth, kata tho kod kwongʼ. Koro yieruru ngima mondo un kaachiel gi nyikwau udag maber
Lero kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni zodzakutsutsani pakuti ndayika pamaso panu moyo ndi imfa, madalitso ndi matemberero. Tsopano sankhani moyo kuti inu ndi ana anu mukhale ndi moyo.
20 kendo mondo uher Jehova Nyasaye ma Nyasachu, kuwinjo wechene kendo kuketo chunyu kuome. Nimar Jehova Nyasaye e ngimau, kendo obiro miyou higni mangʼeny e piny mane osesingore ne kwereu Ibrahim, Isaka kod Jakobo.
Ndi kuti mukonde Yehova Mulungu wanu, kumvera mawu ake, ndi kukhulupirika kwa Iye. Pakuti Yehova ndiye moyo wanu, ndipo mudzakhala zaka zambiri mʼdziko limene analumbira kulipereka kwa makolo anu, Abrahamu, Isake ndi Yakobo.

< Rapar Mar Chik 30 >