< Rapar Mar Chik 13 >

1 Ka janabi moro kata ngʼat mokoro gik mabiro timore e lek otuch e dieru kendo ohulo wach moro mar hono kod ranyisi,
Ngati mneneri kapena wina aliyense amene amanena zamʼtsogolo mwa maloto atuluka pakati panu, nalengeza za chizindikiro chozizwitsa kapena chodabwitsa,
2 kendo ka honono kod ranyisino ma ohulo otimore bangʼe owacho niya, “We walu nyiseche mamokogi (ma gin nyiseche ma ok ungʼeyo) kendo ka owacho ni we walamgi,”
chinthu nʼkuchitikadi, tsono iyeyo nʼkunena kuti, “Tiyeni titsatire milungu ina, tiyeni tiyipembedze,” (kunena milungu imene simunayidziwe),
3 to kik uwinj wach janabino kata jalekno. Jehova Nyasaye ma Nyasachu temou mondo ongʼe ane ka uhere gi chunyu duto kod ngimau duto.
musamumvere mneneriyo kapena wolotayo. Yehova Mulungu wanu afuna akuyeseni kuti aone ngati mumamukonda ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
4 En Jehova Nyasaye ma Nyasachu kende ema onego uluw kendo en kende ema owinjore umiye luor. Rituru chikene, luoreuru, tineuru kendo upadru kuome.
Muyenera kutsatira Yehova Mulungu wanu, ndipo ndi Iyeyo amene muyenera kumuopa. Muzisunga malamulo ake ndi kumamumvera, muzimutumikira ndipo kumukangamira Iyeyo.
5 Janabino kata jalekno nyaka negi nimar opuonjo tim ngʼanyo ne Jehova Nyasaye ma Nyasachu mane oresou kagolou Misri kaka wasumbini; kendo osetemo golou e yore mane Jehova Nyasaye ma Nyasachu ochikou mondo uluw. Tim marachni nyaka ugol e dieru.
Mneneri kapena wolotayo ayenera kuphedwa, popeza analalikira zopandukira Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto ndi kukupulumutsani ku dziko la ukapolo. Wolalikirayo anafuna kukupatutsani pa njira imene Yehova Mulungu wanu anakulamulirani kuti muyitsatire. Muzichotsa choyipa pakati panu.
6 Ka dipo owadu hie, wuodi, nyari kata chiegi mihero kata osiepni migeno hoyi lingʼ-lingʼ kawachoni niya, “We wadhi mondo walam nyiseche mamoko” (ma gin nyiseche ma in kata kwereni ne ok ongʼeyo;
Ngati mʼbale wanu weniweni kapena mwana wanu wamwamuna kapena wamkazi, kapena mkazi wanu wokondedwa, kapena mnzanu wapamtima akukakamizani mwachinsinsi, nʼkumati, “Tiyeni tipite tikapembedze milungu ina” (milungu imene inuyo kapena makolo anu sanayidziwe,
7 ma gin nyiseche mag ogendini mokiewo kodu, bed ni gin machiegni kata mabor, kochakore e bath piny konchiel nyaka komachielo);
milungu ya anthu okuzungulirani, kaya ndi apafupi kapena akutali, kuchokera kumapeto mpaka kumapeto kwina kwa dziko lapansi),
8 to kik iyie olok pachi kata winjo wachne. Kik itimne ngʼwono moro amora kendo kik iluwe kata pande.
musamugonjere kapena kumumvera. Musamumvere chisoni. Musamuleke kapena kumutchinjiriza.
9 Nyaka inege kendo lweti owuon ema okuong tere e tho. Bangʼe lwet ji moko duto bende otim kamano.
Mumuphe ndithu. Dzanja lanu likhale loyambirira kumupha, kenaka manja a anthu ena onse.
10 Chieleuru gi kite nyaka otho, nimar otemo golou kuom Jehova Nyasaye ma Nyasachu, mane ogolou Misri e piny mane unie wasumbini.
Mumuponye miyala mpaka kumupha, chifukwa anafuna kukupatutsani pa njira ya Yehova Mulungu amene anakutulutsani ku Igupto, dziko la ukapolo.
11 Eka jo-Israel nowinj wachno mabed giluoro, to onge ngʼato kuomu kendo manotim gima rachno kendo.
Tsono Aisraeli onse adzamva nachita mantha, ndipo palibe mmodzi pakati panu amene adzachitenso choyipa chotere.
12 Ka iwinjo ka iwacho e achiel kuom miechu ma Jehova Nyasaye ma Nyasachu miyou mondo udagie
Ngati mumvetsedwa kuti ku umodzi mwa mizinda imene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti mukhalemo,
13 ni joma timbegi mono osedonjo e miechgi ma osewuondo ji mangʼeny kuondego kawachonegi niya, “Wadhiuru walam nyiseche mamoko” (ma gin nyiseche ma ok usengʼeyo),
kwapezeka anthu ena oyipa pakati panu ndipo asocheretsa anthu ambiri mʼmizinda yanu, pomanena kuti, “Tiyeni tikapembedze milungu ina” (milungu imene simunayidziwe),
14 to wachno nyaka unon matut ahinya ka en adieri. Ka osenwangʼo kamano ni gima kwero osetimore e dieru,
mukuyenera kufunsa, kulondola ndi kufufuza bwino nkhaniyo. Ndipo ngati zitatsimikizikadi kuti ndi zoona kuti chinthu chonyansa chotere chachitikadi pakati panu,
15 to nyaka uneg jogo duto modak e dalano gi ligangla. Neg-giuru duto kaachiel gi jambgi.
muyenera kuwapha onse okhala mu mzinda umenewo. Muwonongeretu kwathunthu mzindawo, anthu ake ndi ziweto zake zomwe.
16 Chokuru gik moyaki dalano kendo uketgi e laru mi uwangʼ-gi kaka misango miwangʼo pep ne Jehova Nyasaye ma Nyasachu. Nyaka odongʼ gunda ma ok nochak ger.
Katundu yense wa anthu mu mzindawo mumuwunjike pamodzi pakatikati pa bwalo losonkhanako ndipo mutenthe mzindawo pamodzi ndi katundu wake yense monga nsembe yathunthu yopsereza ya kwa Yehova Mulungu wanu. Mzinda umenewo ukhale bwinja mpaka muyaya, usadzamangidwenso.
17 Gik mamonogo kik yud e lwetu eka mirima mager mar Jehova Nyasaye norum, mi notimnu ngʼwono kendo ununyaa kaka nosingore ne kwereu.
Musapezeke ndi kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa kuti Yehova abweze mkwiyo wake wochititsa manthawu. Adzakuchitirani chifundo ndi kukumverani chisoni, ndipo adzakuchulukitsani monga analonjeza mwa lumbiro kwa makolo anu,
18 Nikech uluoro Jehova Nyasaye ma Nyasachu, kurito chikene duto ma amiyi kawuono kendo ka utimo gik makare e wangʼ Jehova Nyasaye.
chifukwa mumamvera Yehova Mulungu wanu, kusunga malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino ndi kuchita zoyenera pamaso pake.

< Rapar Mar Chik 13 >