< Rapar Mar Chik 12 >

1 Magi e buche kod chike manyaka une ni uluwo e piny ma Jehova Nyasaye ma Nyasach kwereu, osemiyou mondo ukaw obed maru ka pod udak e pinyni.
Awa ndi malangizo ndi malamulo amene muyenera kusamalitsanso kuti muwatsatire mʼdziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu wakupatsani kuti mutenge pa nthawi yonse imene muti mudzakhale mʼdzikomo.
2 Kethuru kuonde duto manie gode, thuche kendo kuonde duto manie tipo yiende madongo mane ogendini makoro uriembo ne lamoe nyisechegi.
Muwonongeretu kwathunthu malo onse a pamwamba pa mapiri ataliatali ndi pa mapiri angʼonoangʼono ndi pansi pa mtengo uliwonse wotambalala pamene mitundu imene muyilande dzikolo ankapembedzerapo milungu yawo.
3 Mukuru kendegi mag misango, touro kitegi ma gilamo kendo wangʼuru sirni mag-gi mag Ashera e mach; ngʼaduru matindo tindo kido mag nyisechegi kendo ugol nying-gi oko kuonde duto.
Mugumule maguwa awo ansembe, ndi kuphwanya miyala yawo yachipembedzo ndipo mutenthe pa moto mafano awo a Asera: mugwetse mafano a milungu yawo ndi kufafaniza mayina awo mʼmalo amenewo.
4 Kik ulam Jehova Nyasaye ma Nyasachu e yo ma gilamogo nyiseche manono.
Musapembedze Yehova Mulungu wanu monga mmene amachitira iwowa.
5 To nyaka udwar kama Jehova Nyasaye ma Nyasachu oseyiero e kind dhoutu duto, mondo Nyinge obedie kaka kar dak mare. Kanyo ema onego udhiye
Koma inu muzifunafuna kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati pa mafuko anu kuti ayikeko dzina lake ndi kukhalako. Ku malo amenewa muyenera kupitako.
6 mondo uterie misango miwangʼo pep, kod misango magu kaachiel gi chiwo mar achiel kuom apar kod chiwo moyiedhi, kaachiel gi chiwo mar kwongʼruok kod chiwo mar hera, gi chiwo mag nyithindo makayo mag dhou kod jambu.
Kumeneko muzipititsako zopereka zanu ndi nsembe zanu zopsereza, ndi chakhumi chanu ndi mphatso zapadera zimene munalonjeza kupereka ndi zopereka zanu zaufulu ndi ana oyamba a ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu.
7 E nyim Jehova Nyasaye ma Nyasachu kanyo ema un kod jou duto unuchiemie gi mor e gik moko duto ma lwetu timo, nimar Jehova Nyasaye ma Nyasachu osegwedhou.
Kumeneko, pamaso pa Yehova Mulungu wanu, inu ndi mabanja anu mudzadya ndi kusangalalako pa china chilichonse chimene mudzakhudza, chifukwa Yehova Mulungu wanu wakudalitsani.
8 Kik utim kaka watimo e ndaloni, ma ngʼato ka ngʼato timo mana gima oneno ni berne,
Musadzachite monga tikuchitira lero lino, aliyense kumachita zimene akuona kuti ndi zoyenera,
9 nikech pok uchopoe kar yweyo, kendo yudo girkeni ma Jehova Nyasaye ma Nyasachu miyou.
pakuti simunafike ku malo opumulirako ndi ku cholowa chimene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
10 To ubiro ngʼado loka Jordan mondo udagi e piny ma Jehova Nyasaye ma Nyasachu miyou kaka girkeni mi enomiu yweyo e lwet wasiku moluorou, mondo udagi gi kwe.
Koma mudzawoloka Yorodani ndi kukhazikika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, ndipo Iye adzakupatsani inu mpumulo ku adani anu okuzungulirani kuti mukhale motchinjirizidwa.
11 To kama Jehova Nyasaye ma Nyasachu noyier miluongo e Nyinge, kanyo ema unukelie gik moko duto ma achikou, ma gin misango miwangʼo pep, kod misango magu, achiel kuom apar magu, mich moyiedhi kod chiwo mag mwandu mugeno musingoru ni ubiro kelo ne Jehova Nyasaye ma Nyasachu.
Tsono kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe kuti azikhalako muzikabweretsako chilichonse chimene ndikulamulirani inu: zopereka ndi nsembe zanu zopsereza, chakhumi chanu ndi mphatso zapadera, ndi chuma chanu chonse chosankhika chimene munalonjeza kwa Yehova.
12 Kendo kanyo bedie mamor gi Jehova Nyasaye ma Nyasachi, in kaachiel gi yawuoti kod nyigi, jotichni ma yawuowi kod ma nyiri, jo-Lawi manie miechu, maonge gi pok kata girkeni ma mekgi giwegi.
Ndipo kumeneko inu mukasangalale pamaso pa Yehova Mulungu wanu pamodzi ndi ana anu aamuna ndi ana anu aakazi, antchito anu aamuna ndi adzakazi anu, ndi Alevi a mʼmidzi yanu, amene alibe gawo kapena cholowa chawochawo.
13 Bed motangʼ mondo kik ichiw misango miwangʼo pep kamoro amora ma ihero.
Musamalitse kuti musakaphere nsembe zanu zopsereza paliponse pamene mungafune.
14 Chiwgi mana e kama Jehova Nyasaye biro yiero e kind jo-dhoutu, kendo kanyo ema itimie gik moko duto ma achiki.
Mukaphere pa malo okhawo amene Yehova adzawasankhe mwa limodzi la mafuko anu, ndipo kumeneko mukasunge chilichonse chimene ndikulamulireni.
15 Kata kamano unyalo yangʼo chiayo meku kamoro amora e miechu, ma ucham ringʼo kaka udwaro, mana ka gima en ring mwanda kata ogunde. Kaluwore gi gweth ma Jehova Nyasaye ma Nyasachu miyou, joma ogak kod jomaler nyalo chamo ringʼogo.
Koma mukhoza kumapha ziweto zanu mʼmizinda iliyonse ndi kudya nyama yake mmene mungafunire, ngati kuti ndi agwape kapena mbawala, monga mwadalitso limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. Woyeretsedwa ndi wosayeretsedwa akhoza kuyidya.
16 To kata kamano kik ucham remo, to pukgiuru piny mana ka pi.
Koma musamadye magazi. Muziwathira pansi ngati madzi.
17 Kik ucham pok mar achiel kuom apar mar cham, divai manyien, kod mo, kata chiwo mag nyithindo makayo mag dhou kod jambu kata chiwo mar kwongʼruok kata chiwo mar hera kata chiwo mogen e miechu.
Musamadyere mʼmizinda yanu chakhumi cha tirigu wanu ndi vinyo watsopano ndi mafuta, kapena za ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu, kapena chilichonse chimene mwalonjeza kuchipereka, nsembe zanu zaufulu, kapena mphatso zapadera,
18 Unucham gigo kama Jehova Nyasaye ma Nyasachu biro yiero, in kaachiel gi yawuoti kod nyigi, jotichgi machwo kod ma nyiri, gi jo-Lawi manie miechu, kendo nyaka ubed mamor e nyim Jehova Nyasaye ma Nyasachu kuom gik moko duto ma lwetu timo.
mʼmalo mwake, muzidya pamaso pa Yehova Mulungu wanu, kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhira inu, ana anu aamuna ndi aakazi, antchito anu aamuna ndi adzakazi anu, ndi Alevi ochokera mʼmizinda yanu, ndipo mudzasangalale pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa chilichonse chimene mudzachikhudza.
19 Beduru motangʼ mondo kik ujwangʼ kod jo-Lawi modak e dieru e ndalo duto ma udak e pinyni.
Muonetsetse kuti musawataye Alevi pa masiku onse amene mukhale mʼdziko lanumo.
20 Ka Jehova Nyasaye ma Nyasachu osemedo tongʼ maru kaka ne osingorenu, mi ugombo chamo ringʼo ma uwacho niya, “Agombo chamo ringʼo,” to nucham ringʼo mangʼeny kaka unyalo.
Yehova Mulungu wanu akadzakulitsa dziko lanu monga anakulonjezerani, ndipo mukapukwa nyama mumanena kuti, “Ndikufuna nyama,” pamenepo mudzadya mmene mungafunire.
21 Ka kama Jehova Nyasaye ma Nyasachu oyiero mondo nyinge obedie bor kodu, to unyalo yangʼo chiayo moa e kweth jambu kod dhou moa e miechu kaka asechikou kendo ucham ringʼo kaka udwaro.
Ngati malo amene Yehova Mulungu wanu awasankha kuti ayike Dzina lake ali kutali kwambiri ndi inu, mukhoza kupha ziweto pakati pa ngʼombe ndi nkhosa zimene Yehova wakupatsani, monga ndinakulamulani, ndipo mʼmizinda yanuyanu mukhoza kuzidya mmene mungafunire.
22 Chamgiuru mana kaka ducham mwanda kata ogunde. Joma ogak kod jomaler duto manie dieru nochiem duto.
Muzidye ngati mukudya gwape kapena mbawala. Onse oyeretsedwa monga mwa mwambo ndi osayeretsedwa omwe akhoza kudya.
23 To kik ucham remo, nikech remo en ngima, to ok onego ucham ngima gimoro kod ringe.
Koma muonetsetse kuti musadye magazi, chifukwa magazi ndi moyo, ndipo musamadye moyo pamodzi ndi nyama.
24 To kata kamano kik ucham remo, to pukgiuru piny mana ka pi.
Inu musamadye magazi, muziwathira pansi ngati madzi.
25 Ka ok uchamo chiemogo to ubiro dhi maber kaachiel gi nyikwau, nikech mano utimo gima ber kendo malongʼo e nyim wangʼ Jehova Nyasaye ma Nyasachu.
Musamadye magazi kuti zikuyendereni bwino inu pamodzi ndi ana anu a pambuyo panu, popeza mudzakhala mukuchita zoyenera pamaso pa Mulungu.
26 To kawuru giu mowal kod gimoro amora ma usesingoru kukwongʼoru ni unuchiw kendo udhi kama Jehova Nyasaye noyier.
Koma mutenge zinthu zanu zoyeretsedwa ndi china chilichonse chimene munalumbira kupereka, ndi kupita kumalo kumene Yehova adzasankhe.
27 Ket misango miwangʼo pep e kendo mar misango mar Jehova Nyasaye ma Nyasachu, ringʼo kaachiel gi remo. Remb misenginigo nyaka ol e bath kendo mar Jehova Nyasaye ma Nyasachu, to ringʼo to unyalo chamo.
Mupereke nsembe zanu zopsereza pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu, nyama pamodzi ndi magazi omwe. Magazi a nsembe zanu athiridwe pambali pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu, koma nyamayo mukhoza kudya.
28 Beduru motangʼ ka urito chike ma amiyou mondo udhi maber kaachiel gi nyikwau nikech mano utimo gima ber kendo malongʼo e nyim wangʼ Jehova Nyasaye ma Nyasachu.
Onetsetsani kuti muzimvera mawu onsewa amene ndikukupatsani kuti zinthu zizikuyenderani bwino nthawi zonse inu ndi ana anu chifukwa mudzakhala mukuchita zabwino ndi zoyenera pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
29 Jehova Nyasaye ma Nyasachu biro riembo ogendini ma ubiro monjo kendo kawo pinygi ka uneno. To ka useriembogi oko mi udak e pinygi,
Yehova Mulungu wanu adzachotsa pamaso panu mitundu ya anthu amene mukufuna kuwathira nkhondo ndi kuwalanda dzikolo. Koma mukawapirikitsa ndi kukhazikika mʼdziko lawo,
30 kendo bangʼ ka osetiekgi chuth e nyimu, to beduru motangʼ kendo kik upenj weche mag nyisechegi ka uwacho niya, “Ere kaka ogendinigi ne tiyo ni nyisechegi? Wan bende wabiro timo kamano.”
ndipo pamene iwo awonongeka pamaso panu, samalirani kuti musakodwe mu msampha pa kufufuza za milungu yawo, nʼkumati, “Kodi anthu a mitunduwa amatumikira bwanji milungu yawo? Ifenso tichita momwemo.”
31 Ok onego ulam Jehova Nyasaye ma Nyasachu kaka gilamo nyisechegi, nikech Jehova Nyasaye mon gi kit lamo ma gilamogo nyisechegigo, kendo gitimo giko mamono duto ma Jehova Nyasaye osin-go. To bende gitimo misango gi yawuotgi kod nyigi e mach ka gichiwo ne nyisechegi.
Musapembedze Yehova Mulungu wanu momwe amachitira iwowo, chifukwa popembedza milungu yawoyo amachita zonyansa zamitundumitundu zimene Yehova amadana nazo. Amatentha ngakhale ana awo aamuna ndi aakazi pa moto ngati nsembe za kwa milungu yawo.
32 Neuru ni utimo gik moko duto machikou, kendo kik umedie gimoro kata kik ugol.
Onetsetsani kuti mukuchita zimene ndikukulamulirani. Musawonjezerepo kapena kuchotserapo.

< Rapar Mar Chik 12 >