< 2 Samuel 22 >

1 Kane Jehova Nyasaye osereso Daudi e lwet wasike duto kod e lwet Saulo, Daudi nowerne Jehova Nyasaye kopake gi weche mag wendni.
Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.
2 Nowacho ni: “Jehova Nyasaye en lwandana, en ohingana kendo en e jaresna;
Iye anati, “Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga.
3 Nyasacha e lwandana, kuome ema apondoe, kendo en e okumbana kendo en e teko mar warruokna. En e ohingana, kar pondana, kendo jawarna en ema oresa kuom jo-mahundu.
Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo, chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa. Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga. Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
4 “Aluongo Jehova Nyasaye, mowinjore pako, kendo oresa kuom wasika.
“Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
5 Apaka mag tho nolwora; kendo oula mar kethruok nohewa.
“Mafunde a imfa anandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
6 Tonde mag tho nondhoga morida kendo obadho mar tho nochika tir. (Sheol h7585)
Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
7 “E chandruokna ne aluongo Jehova Nyasaye kendo naluongo Nyasacha. Nowinjo dwonda ka en e hekalu mare kendo ywakna nochopo e ite.
“Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinapemphera kwa Mulungu wanga. Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.
8 Piny notetni kendo oyiengni, mise mag polo noyiengni; negitetni nikech nokecho.
“Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, maziko a miyamba anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
9 Iro nowuok e ume; mach mangʼangʼni nowuokie dhoge, mirni maliel maliet bende nowuok kuome.
Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
10 Nobaro polo mobiro e piny; rumbi molil ti nonyono gi tiende.
Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
11 Noidho kerubi mi ofuyogo ka kalausi.
Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
12 Noloso mudho obedo ka hema molwore, ma en rumbi motwere mar koth manie polo.
Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, mitambo yakuda ya mlengalenga.
13 Ler nowuok kama entie mamil ka mil polo.
Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera makala amoto alawilawi.
14 Jehova Nyasaye nomor gie polo; dwond Nyasaye Man Malo Moloyo nowuo.
Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
15 Nodiro aserni mokeyo wasigu, mor polo gi mil polo noriembogi.
Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
16 Kude mag nam kod mise mag piny noelore, kane Jehova Nyasaye okwerogi kokudho gi much ume.
Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera, ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake.
17 “Norieyo bade ka en malo momaka, nogola ei pige matut.
“Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
18 Noresa e lwet jasika maratego, kuom jowasika, mane tek moloya.
Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.
19 Negimonja e kinde mane an gi masira, to Jehova Nyasaye ema nokonya.
Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
20 Nokela kama ni thuolo; noresa nikech nomor koda.
Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
21 “Jehova Nyasaye osetimona mana maromre gi timna makare; osechula kaluwore gi tich lweta maler.
“Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
22 Nimar aserito yore Jehova Nyasaye; ok asetimo marach kuom weyo Nyasacha.
Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga.
23 Chikene duto ni e nyima; pok alokora aweyo buchene.
Malamulo ake onse ali pamaso panga, sindinasiye malangizo ake.
24 Asebedo maonge ketho e nyime, kendo aseritora mondo kik atim richo.
Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
25 Jehova Nyasaye osemiya pokna mowinjore gi timna makare, mana machal gi kaka aler e wangʼe.
Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake.
26 “Ne jo-adiera, ibedonegi ja-adiera, to ni joma onge ketho, to ibedonegi maonge ketho,
“Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu, kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
27 ne jomaler, inyisori kaka ngʼama ler, to ne joma yoregi obam, inyisori kaka ngʼama rach.
Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
28 Ireso joma muol, to wangʼi rango josunga mondo idwokgi piny.
Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa.
29 In e tacha, yaye Jehova Nyasaye Jehova Nyasaye loko mudho momaka bedo ler.
Inu Yehova, ndinu nyale yanga; Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
30 Ka ikonya to anyalo loyo jolweny momonja; ka an gi Nyasacha to anyalo lwenyo ohinga.
Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo, ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
31 “Yor Nyasaye en yo malongʼo; wach Jehova Nyasaye onge ketho. En okumba ni jogo duto mopondo kuome.
“Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa iye.
32 Ere Nyasaye moro makmana Jehova Nyasaye? Kendo en ngʼatno ma en Lwanda makmana Nyasachwa?
Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
33 Nyasaye ema miya teko kendo omiyo yora bedo mokwe.
Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
34 Omiyo tiendena bedo mayot ka tiende mwanda; kendo en ema omiyo achungʼ kuonde man malo maboyo.
Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
35 Otiego lwetena ne lweny; bedena nyalo ywayo atungʼ mar nyinyo.
Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
36 Imiya okumbani mar loch; ikulori piny mondo imi abed maduongʼ.
Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso; mumawerama kuti mundikweze.
37 Imiyo yo mawuothoe bedo malach, mondo tiendena kik ba yo.
Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino, kuti mapazi anga asaterereke.
38 “Ne alawo wasika mi atiekogi; ne ok aweyogi nyaka negirumo.
“Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha; sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa.
39 Ne atiekogi chuth, mane ok ginyal chungʼ; negipodho e tienda.
Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso; Iwo anagwera pansi pa mapazi anga.
40 Ne imiya teko mar kedo lweny; ne imiyo jomamon koda kulore e nyima.
Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo; munagwaditsa adani anga pa mapazi anga.
41 Ne imiyo wasika oringo kadhi, mine atieko joma ok dwara.
Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa; ndipo ndinawononga adani anga.
42 Ne giywak mondo okonygi, to ne onge ngʼama ne nyalo resogi; ne giywakne Jehova Nyasaye, to ne ok odwokogi.
Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.
43 Ne agoyogi ma giregore ka buru mayom mar lowo; nanyonogi mawuotho kuomgi ka chwodho man e yo.
Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi; ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
44 “Iseresa e lwet jowa mane monja; iserita kaka jatelo mar ogendini. Joma ne ok angʼeyo nobet e bwo lochna,
“Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu; Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
45 kendo jopinje mamoko biro ira kobolore, ka awuoyo to giwinja kendo gitimo gima adwaro.
Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine, amandigonjera.
46 Negibiro ka gitetni; kendo ka chunygi ool, ka gia kuondegi mag pondo.
Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
47 “Jehova Nyasaye ngima! Pak obed ne Lwandana! Duongʼ obed ni Nyasaye, ma Lwanda kendo ma Jawarna.
“Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa. Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga!
48 En e Nyasaye ma chulona kuor, maketo ogendini e bwoya,
Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga,
49 ma gonya e lwet wasika. Nitingʼa malo moloyo wasika; ne iresa e lwet jo-mahundu.
amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
50 Emomiyo anapaki e kind ogendini, yaye Jehova Nyasaye, kendo anawer wende mapako nyingi.
Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
51 “Jehova Nyasaye kelo resruok maduongʼ ne ruoth moketo; onyiso ngʼwonone mogundho ma ok rum ne ngʼate mowir, ni Daudi gi nyikwaye nyaka chiengʼ.”
“Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake, amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”

< 2 Samuel 22 >