< Zakarias 9 >

1 Et Udsagn: HERRENs Ord er over Hadraks Land, i Damaskus slår det sig ned - thi Aram forbrød sig mod HERREN - det er over alle, som hader Israel,
Mawu a Yehova odzudzula dziko la Hadiraki ndi mzinda wa Damasiko pakuti maso a anthu ndiponso mafuko onse a Israeli ali pa Yehova—
2 også over Hamat, som grænser dertil, Tyrus og Zidon, thi det er såre viist.
ndiponso mzinda wa Hamati, umene ukuchita malire ndi dzikoli, komanso pa Turo ndi Sidoni, ngakhale kuti iwo ndi anzeru kwambiri.
3 Tyrus bygged sig en Fæstning og ophobed Sølv som Støv og Guld som Gadeskarn.
Ndipo Turo anadzimangira linga; wadziwunjikira siliva ngati fumbi, ndi golide ngati zinyalala za mʼmisewu.
4 Se, Herren vil tage det i Eje og styrte dets Bolværk i Havet. det selv skal fortæres af Ild.
Taonani Ambuye adzamulanda chuma chakecho ndi kuwononga mphamvu zake mʼnyanja, ndipo adzapserera ndi moto.
5 Askalon ser det og frygter, Gaza og Ekron skælver voldsomt, thi Håbet brast. Gaza mister sin Konge, i Askalon skal ingen bo,
Mzinda wa Asikeloni udzaona zimenezi, nʼkuchita mantha; Gaza adzanjenjemera ndi ululu, chimodzimodzinso Ekroni, chifukwa chiyembekezo chake chidzatheratu. Mfumu ya ku Gaza idzaphedwa ndipo Asikeloni adzakhala opanda anthu.
6 i Asdod skal Udskud bo, Jeg gør Ende på Filisterens Hovmod,
Mu Asidodi mudzakhala mlendo, ndipo ndidzathetsa kunyada kwa Afilisti.
7 tager Blodet ud af hans Mund og Væmmelsen bort fra hans Tænder. Også han bliver reddet for vor Gud, han bliver som en Slægt i Juda, Ekron som, en, Jebusit.
Ndidzachotsa nyama ya magazi mʼkamwa mwawo, chakudya choletsedwa mʼmano mwawo. Amene atsala adzakhala anthu a Mulungu wathu, adzasanduka atsogoleri mu Yuda, ndipo Ekroni adzakhala ngati Ayebusi.
8 Som en Vagt lejrer jeg mig formit Hus mod dem, som kommer og går; aldrig mer skal en Voldsmand gå igennem deres Land, thi nu har jeg set det med mine egne Øjne.
Koma Ine ndidzalondera Nyumba yanga ndi kuyiteteza kwa ankhondo osakaza. Palibenso mdani amene adzagonjetse anthu anga, pakuti tsopano ndikuwayangʼanira.
9 Fryd dig såre, Zions Datter, råb med Glæde, Jerusalems Datter! Se, din Konge kommer til dig. Retfærdig og sejrrig er han, ydmyg, ridende på et Æsel, på en Asenindes Føl.
Sangalala kwambiri, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni! Fuwula, mwana wamkazi wa Yerusalemu! Taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe, yolungama ndi yogonjetsa adani, yodzichepetsa ndi yokwera pa bulu, pa mwana wamphongo wa bulu.
10 Han udrydder Vognene af Efraim, Hestene af Jerusalem, Stridsbuerne ryddes til Side. Hans Ord stifter Fred mellem Folkene, han hersker fra Hav til Hav, fra Floden til Jordens Ende.
Ndidzachotsa magaleta ankhondo ku Efereimu ndi akavalo ankhondo ku Yerusalemu, ndipo uta wankhondo udzathyoka. Mfumuyo idzabweretsa mtendere pakati pa mitundu ya anthu. Ulamuliro wake udzayambira ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina, ndipo kuchokera ku Mtsinje (Yufurate) mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
11 For Pagtblodets Skyld vil jeg også slippe dine Fanger ud, ja ud af den vandløse Brønd.
Tsono kunena za iwe, chifukwa cha magazi a pangano lako ndi Ine, ndidzamasula amʼndende ako, ndidzawatulutsa mʼdzenje lopanda madzi.
12 Hjem til Borgen, I Fanger med Håb! Også i Dag forkyndes: Jeg giver dig tvefold Bod!
Bwererani ku malo anu otetezedwa, inu amʼndende achiyembekezo; ngakhale tsopano ndikulengeza kuti ndidzakubwezerani zabwino mowirikiza.
13 Thi jeg spænder mig Juda som Bue, lægger Efraim på som Pil og vækker dine Sønner, Zion, imod dine Sønner, Javan. Jeg gør dig som Heltens Sværd.
Ndidzakoka Yuda monga ndimakokera uta wanga, ndipo Efereimu ndiye muvi wake. Ndidzadzutsa ana ako iwe Ziyoni, kulimbana ndi ana ako iwe Grisi, ndipo ndidzakusandutsa iwe lupanga la munthu wankhondo.
14 Over dem viser sig Herren, hans Pil farer ud som et Lyn. Den Herre HERREN støder i Horn, skrider frem i Søndenstorm;
Pamenepo Yehova adzaonekera kwa anthu ake; mivi yake idzangʼanima ngati chingʼaningʼani. Ambuye Yehova adzaliza lipenga; ndipo adzayenda mu mkuntho wochokera kummwera,
15 dem værner Hærskarers HERRE. De opæder, nedtramper Slyngekasterne, drikker deres Blod som Vin og fyldes som Offerskålen, som Alterets Hjørner.
ndipo Yehova Wamphamvuzonse adzawateteza. Iwo adzawononga ndipo adzagonjetsa ndi miyala ya legeni. Adzamwa magazi ndi kubangula ngati amwa vinyo; magazi adzayenderera ngati a mʼmbale yowazira magazi pa ngodya za guwa lansembe.
16 HERREN deres Gud skal på denne Dag frelse dem som sit Folks Hjord; thi de er Kronesten, der funkler over hans Land.
Tsiku limenelo Yehova Mulungu wawo adzawapulumutsa pakuti anthu ake ali ngati nkhosa. Adzanyezimira mʼdziko lake ngati miyala yokongola pa chipewa chaufumu.
17 Hvor det er dejligt, hvor skønt! Thi Korn giver blomstrende Ungersvende, Most giver blomstrende Møer.
Taonani chikoka ndi kukongola kwawo! Tirigu adzasangalatsa anyamata, ndi vinyo watsopano anamwali.

< Zakarias 9 >