< Zakarias 5 >
1 Derpå løftede jeg mine Øjne og skuede, og se, der var en flyvende Bogrulle.
Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona chikalata chimene chimawuluka.
2 Og han spurgte mig: "Hvad ser du?" Jeg svarede: "Jeg ser en flyvende Bogrulle, som er tyve Alen lang og ti Alen bred."
Mngelo uja anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ndikuona chikalata chikuwuluka, mulitali mwake mamita asanu ndi anayi ndipo mulifupi mwake mamita anayi ndi theka.”
3 Da sagde han til mig: "Det er Forbandelsen, som udgår over hele Landet; thi alle, som stjæler, er nu længe nok gået fri, og alle, som sværger, er nu længe nok gået fri.
Ndipo mngeloyo anandiwuza kuti, “Awa ndi matemberero amene akupita pa dziko lonse lapansi; potsata zimene zalembedwa mʼkati mwa chikalatamo, aliyense wakuba adzachotsedwa, ndipo potsata zomwe zalembedwa kunja kwake, aliyense wolumbira zabodza adzachotsedwanso.
4 Jeg lader den udgå, lyder det fra Hærskarers HERRE, for at den skal komme i Tyvens Hus og dens Hus, som sværger falsk ved mit Navn, og sætte sig fast i deres Huse og tilintetgøre dem med Tømmer og Sten."
Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Temberero limeneli ndidzalitumiza, ndipo lidzalowa mʼnyumba ya munthu wakuba ndi munthu wolumbira zabodza mʼdzina langa. Lidzakhala mʼnyumbamo mpaka kuyiwonongeratu, matabwa ake ndi miyala yake yomwe.’”
5 Derpå trådte Engelen, som talte med mig, frem og sagde til mig: "Løft dine Øjne og se, hvad det er, som kommer der!"
Kenaka mngelo amene amayankhula nane uja anabwera patsogolo panga ndipo anandiwuza kuti, “Kweza maso ako tsopano kuti uwone kuti ndi chiyani chikubwerachi.”
6 Jeg spurgte: "Hvad er det?" Og han svarede: "Det er Efaen, som kommer." Og han vedblev: "Det er deres Brøde i hele Landet."
Ndinafunsa kuti, “Kodi chimenechi nʼchiyani?” Mngeloyo anayankha kuti, “Limeneli ndi dengu loyezera.” Ndipo anawonjezera kunena kuti, “Umenewu ndi uchimo wa anthu mʼdziko lonse.”
7 Og se, et Blylåg løftedes, og se, i Efaen sad en Kvinde.
Pamenepo chovundikira chake chamtovu chinatukulidwa, ndipo mʼdengumo munali mutakhala mkazi.
8 Og han sagde: "Det er Gudløsheden!" Så stødte han hende ned i Efaen og slog Blylåget i over Åbningen.
Mngeloyo anati, “Chimenechi ndi choyipa,” ndipo anamukankhira mkaziyo mʼdengu muja, nabwezera chovundikira chamtovu chija pamwamba pake.
9 Og jeg løftede mine Øjne og skuede, og se, to Kvinder kom båret af Vinden, og deres Vinger var som Storkevinger; og de løftede Efaen op mellem Himmel og Jord.
Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona akazi awiri akuwuluka kubwera kumene kunali ine; akuwuluzika ndi mphepo. Iwo anali ndi mapiko ngati a kakowa, ndipo ananyamula dengu lija, kupita nalo pakati pa mlengalenga ndi dziko lapansi.
10 Så spurgte jeg Engelen, som talte med mig: "Hvor bærer de Efaen hen?"
Ine ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Dengulo akupita nalo kuti?”
11 Han svarede: "Hen at bygge hende et Hus i Sinears Land, og når det er rejst, sætter de hende der, hvor hendes Sted er."
Iye anayankha kuti, “Ku dziko la Babuloni kuti akalimangire nyumba. Nyumbayo ikadzatha, adzayikamo dengulo.”