< Zakarias 12 >

1 Et Udsagn; HERRENs Ord om Israel. Det lyder fra HERREN; som udspændte Himmelen, grundfæstede Jorden og dannede Menneskets Ånd i dets Indre:
Uthenga wa Yehova kwa Israeli. Yehova, amene amayala mlengalenga, amene amayika maziko a dziko lapansi, ndiponso amene amalenga mzimu wokhala mwa munthu, akunena kuti,
2 Se, jeg gør Jerusalem til et berusende Bæger for alle Folkeslag trindt om; også Juda skal være med til at belejre Jerusalem.
“Taonani, ndidzasandutsa Yerusalemu kukhala chakumwa choledzeretsa chimene chidzasokoneza mitundu yonse ya anthu yomuzungulira. Yuda adzazingidwa pamodzinso ndi Yerusalemu.
3 På hin Dag gør jeg Jerusalem til Løftesten for alle Folkeslag - enhver, som løfter den, skal rive sig på den! Og alle Jordens Folk skal samle sig imod det.
Pa tsiku limenelo, pamene mitundu yonse ya anthu a dziko lapansi idzasonkhana kulimbana naye, ndidzasandutsa Yerusalemu thanthwe losatheka kusunthidwa ndi mitundu yonse ya anthu. Onse oyesa kumusuntha adzadzipweteka.
4 På hin Dag, lyder det fra HERREN, slår jeg alle Heste med Angst og Rytterne med Vanvid; Judas Hus åbner jeg Øjnene på, men alle Folkeslagene slår jeg med Blindhed.
Pa tsiku limenelo kavalo aliyense ndidzamuchititsa mantha kuti asokonezeke, ndipo wokwerapo wake ndidzamuchititsa misala,” akutero Yehova. “Ndidzayangʼanira nyumba ya Yuda koma ndidzachititsa khungu akavalo onse a anthu a mitundu ina.
5 Og Judas Stammer skal tænke: "Jerusalems Indbyggere er stærke i Hærskarers HERRE, deres Gud."
Pamenepo atsogoleri a Yuda adzayankhula mʼmitima mwawo kuti, ‘Anthu a ku Yerusalemu ndi amphamvu, chifukwa Yehova Wamphamvuzonse ndiye Mulungu wawo.’
6 På hin Dag gør jeg Judas Stammer til en Ildgryde mellem Brændestykker, et brændende Blus mellem Neg, og de skal æde til højre og venstre alle Folkeslag trindt om, og Jerusalem bliver roligt på sit Sted, i Jerusalem.
“Pa tsiku limenelo ndidzasandutsa atsogoleri a Yuda kukhala ngati mbawula yotentha pakati pa nkhuni, ngati sakali yoyaka pa mitolo ya tirigu. Adzatentha mitundu yonse ya anthu yowazungulira, kumanja ndi kumanzere, koma Yerusalemu sadzasuntha pa malo ake.
7 Så giver HERREN først Judas Telte Sejr, for at Davids Hus og Jerusalems Indbyggere ikke skal vinde større Ry end Juda.
“Yehova adzapulumutsa malo okhala Yuda poyamba, kuti ulemu wa nyumba ya Davide ndi wa anthu okhala mu Yerusalemu usapambane ulemu wa Yuda.
8 På hin Dag værner HERREN om Jerusalems Indbyggere, og den skrøbeligste iblandt dem skal på hin Dag blive som David, men Davids Hus som Gud, som HERRENs Engel foran dem.
Pa tsiku limenelo Yehova adzatchinjiriza onse okhala mu Yerusalemu, kotero kuti anthu ofowoka kwambiri pakati pawo adzakhala ngati Davide, ndipo nyumba ya Davide idzakhala ngati Mulungu, ngati mngelo wa Yehova wowatsogolera.
9 På hin Dag vil jeg søge at tilintetgøre alle de Folk, som kommer imod Jerusalem.
Pa tsiku limenelo ndidzawononga mitundu yonse yofuna kuthira nkhondo Yerusalemu.
10 Og så udgyder jeg over Davids Hus og Jerusalems Indbyg- gere Nådens og Bønnens Ånd, så de ser hen til ham, de har gennemstunget, og sørger over ham, som man sørger over en enbåren Søn, og holder Klage over ham, son1 man holder Klage over den førstefødte.
“Ndipo pa nyumba ya Davide ndi pa anthu okhala mu Yerusalemu ndidzakhuthulirapo mzimu wachisomo ndi wopemphera. Iwo adzandiyangʼana Ine, amene anamubaya, ndipo adzamulirira kwambiri monga momwe munthu amalirira mwana wake mmodzi yekhayo, ndiponso adzamva chisoni kwambiri monga momwe amachitira ndi mwana woyamba kubadwa.
11 På hin Dag skal Sorgen blive stor i Jerusalem som Sorgen over Hadadrimmon i Megiddos Dal.
Pa tsiku limenelo mudzakhala kulira kwakukulu mu Yerusalemu, monga kulira kwa ku Hadadi-Rimoni ku chigwa cha Megido.
12 Landet skal sørge, hver Slægt for sig, Davids Hus's Slægt for sig og deres Kvinder for sig, Natans Hus's Slægt for sig og deres Kvinder for sig,
Dziko lidzalira kwambiri, fuko lililonse pa lokha, akazi awo pa okhanso: fuko la Davide pamodzi ndi akazi awo, fuko la Natani pamodzi ndi akazi awo,
13 Levis Hus's Slægt for sig og deres Kvinder for sig, Sjim'iternes Slægt for sig og deres Kvinder for sig,
nyumba ya Levi pamodzi ndi akazi awo, fuko la Simei pamodzi ndi akazi awo,
14 alle de tiloversblevne Slægter hver for sig og deres Kvinder for sig.
ndiponso mafuko onse pamodzi ndi akazi awo.

< Zakarias 12 >