< Højsangen 8 >

1 Oh, var du min broder, som died min moders bryst! Jeg kyssed dig derude, når vi mødtes, og blev ikke agtet ringe,
Ukanakhala kuti ndiwe mlongo wanga, amene anayamwa mawere a amayi anga! Ndikanakumana nawe pa njira, ndikanakupsompsona, ndipo palibe wina aliyense akanandinyoza.
2 tog dig ind i min Moders hus, i min moders kamre, gav dig krydret vin at drikke, Granatæblers Most.
Ndikanakutenga ndi kukulowetsa mʼnyumba ya amayi anga, amayi amene anandiphunzitsa, ndikanakupatsa vinyo wotsekemera kuti umwe, zotsekemera za makangadza.
3 Hans venstre under mit hoved, hans højre tager mig i favn.
Mutu wanga watsamira dzanja lake lamanzere ndipo dzanja lake lamanja landikumbatira.
4 Jeg besværger eder, Jerusalems Døtre: Gør ikke Kærligheden Uro, væk den ikke før den ønsker det selv!
Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani: musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa mpaka pamene chifunire ichocho.
5 Hvem er hun, der kommer fra Ørkenen, støttet til sin ven? "Under Æbletræet vækked jeg dig; der nedkom din moder med dig, der nedkom hun, som dig fødte."
Kodi ndani uyo akutuluka ku chipululuyo, atatsamira wokondedwa wakeyo? Mkazi Ndinakudzutsa pa tsinde pa mtengo wa apulosi, pamenepo ndi pamene amayi anachirira, pamenepo ndi pamene wokubereka anamva ululu pokubala iweyo.
6 Læg mig som en seglring om dit hjerte, som et Armbånd om din Arm! Thi Kærlighed er stærk som døden, Nidkærhed hård som Dødsriget; i dens gløder er Brændende Glød, dens lue er HERRENS Lue. (Sheol h7585)
Undiyike pamtima pako ngati chidindo, ngati chidindo cha pa dzanja lako; pakuti chikondi nʼchamphamvu ngati imfa, nsanje ndiyaliwuma ngati manda. Chikondi chimachita kuti lawilawi ngati malawi a moto wamphamvu. (Sheol h7585)
7 Mange Vande kan ikke slukke den, Strømme skylle den bort. Gav nogen alt Gods i sit Hus for Kærlighed, Hvem vilde agte ham ringe?
Madzi ochuluka sangachizimitse chikondi, mitsinje singachikokolole chikondicho. Ngati wina apereka chuma chonse cha mʼnyumba mwake chifukwa cha chikondi, adzangonyozeka nazo kotheratu.
8 Vi har en lille Søster, som endnu ej har bryster; hvad gør vi med med vor Søster, den dag hun får en Bejler?
Ife tili naye mlongo wathu wamngʼono, koma alibe mawere, kodi tidzamuchitira chiyani mlongo wathuyu pa tsiku limene adzamufunsire?
9 Er hun en Mur, så bygger vi en krone af sølv derpå, men er hun en Dør, så spærrer vi den med Cederplanke.
Ngati iye ndi khoma, tidzamumangira nsanja ya siliva. Ngati iye ndi chitseko, tidzamutchinga ndi matabwa a mkungudza.
10 Jeg er en Mur, Mine Bryster Tårne. Da blev jeg i hans Øjne som en, der finder Fred.
Ine ndili ngati khoma, ndipo mawere anga ndi nsanja zake. Tsono mʼmaso mwa bwenzi langa ndine wobweretsa mtendere.
11 Salomo havde en Vingård i Ba'al-Hamon, til vogtere gav han den Vingård; hver kunne tjene tusind sekel Sølv på dens Frugt.
Solomoni anali ndi munda wampesa ku Baala-Hamoni; iyeyo anabwereketsa munda wamphesawo kwa alimi, aliyense mwa iwo ankayenera kupereka ndalama zasiliva 1,000 mʼmalo mwa zipatso zake.
12 Jeg har for mig selv min Vingård; de tusinde, Salomo, er dine, to hundrede deres, som vogter dens Frugt.
Koma munda wanga wampesa ndi wangawanga ndiponso wa ine ndekha. Iwe Solomoni, khala nazo ndalama zasiliva 1,000 ndipo ndalama zasiliva 200 ndi za amene akusamalira mundawo.
13 Du, som bor i Haverne, Vennerne lytter, lad mig høre din røst!
Iwe amene umakhala mʼminda uli pamodzi ndi anzako, ndilole kuti ndimve liwu lako!
14 Fly, min Ven, og vær som en Gazel, som den unge Hjort på Balsambjerge!
Fulumira wokondedwa wanga, ndipo ukhale ngati gwape kapena mwana wa mbawala wothamanga mʼmapiri mʼmene mumamera mbewu zokometsera chakudya.

< Højsangen 8 >