< Salme 80 >
1 (Til Sangmesteren. El-sjosjannim-edut. Af Asaf. En Salme.) Lyt til, du Israels Hyrde, der leder Josef som en Hjord, træd frem i Glans, du, som troner på Keruber,
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Salimo la Asafu. Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli, Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa; Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani
2 for Efraims, Benjamins og Manasses Øjne; opbyd atter din Vælde og kom til vor Frelse!
kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase. Utsani mphamvu yanu; bwerani ndi kutipulumutsa.
3 Hærskarers Gud, bring os atter på Fode, lad dit Ansigt lyse, at vi må frelses!
Tibwezereni mwakale Inu Mulungu; nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
4 HERRE, Hærskarers Gud, hvor længe vredes du trods din Tjeners Bøn?
Inu Mulungu Wamphamvuzonse, mpaka liti mkwiyo wanu udzanyeka kutsutsana ndi mapemphero a anthu anu?
5 Du har givet os Tårebrød at spise, Tårer at drikke i bredfuldt Mål.
Mwawadyetsa buledi wa misozi; mwachitisa iwo kumwa misozi yodzaza mbale.
6 Du har gjort os til Stridsemne for vore Naboer, vore Fjender håner os.
Mwachititsa kuti tikhale gwero la mikangano pakati pa anansi athu, ndipo adani athu akutinyoza.
7 Hærskarers Gud, bring os atter på Fode, lad dit Ansigt lyse, at vi må frelses!
Tibwezereni mwakale Inu Mulungu Wamphamvuzonse, nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
8 Du rykked en Vinstok op i Ægypten, drev Folkeslag bort og plantede den;
Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto; munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo.
9 du rydded og skaffed den Plads, den slog Rod og fyldte Landet;
Munawulimira munda wamphesawo, ndipo unamera ndi kudzaza dziko.
10 Bjergene skjultes af dens Skygge. Guds Cedre af dens Ranker;
Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake, mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake.
11 den bredte sine Skud til Havet og sine kviste til Floden.
Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja, mphukira zake mpaka ku mtsinje.
12 Hvorfor har du nedbrudt dens Hegn, så alle vejfarende plukker deraf?
Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake?
13 Skovens Vildsvin gnaver deri, Dyrene på Marken æder den op!
Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga ndipo zirombo za mthengo zimawudya.
14 Hærskarers Gud, vend tilbage, sku ned fra Himlen og se! Drag Omsorg for denne Vinstok,
Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse! Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone! Uyangʼanireni mpesa umenewu,
15 for Skuddet, din højre planted!
muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala, mwana amene inu munamukuza nokha.
16 Lad dem, der sved den og huggede den sønder, gå til for dit Åsyns Trussel!
Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto; pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka.
17 Lad din Hånd være over din højres Mand, det Menneskebarn, du opfostrede dig!
Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja, mwana wa munthu amene mwalera nokha.
18 Da viger vi ikke fra dig, hold os i Live, så påkalder vi dit Navn!
Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu; titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu.
19 HERRE, Hærskarers Gud, bring os atter på Fode, lad dit Ansigt lyse, at vi må frelses!
Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.