< Salme 8 >

1 (Til sangmesteren. Al-haggittit. En salme af David.) HERRE, vor Herre, hvor herligt er dit Navn på den vide Jord du, som bredte din Højhed ud over Himlen!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa gititi. Salimo la Davide. Inu Yehova Ambuye athu, dzina lanu ndi la lamphamvudi pa dziko lonse lapansi! Inu mwakhazikitsa ulemerero wanu mʼmayiko onse akumwamba.
2 Af spædes og diendes Mund har du rejst dig et Værn for dine Modstanderes Skyld, for at bringe til Tavshed Fjende og Hævner.
Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda, Inu mwakhazikitsa mphamvu chifukwa cha adani anu, kukhazikitsa bata adani ndi anthu obwezera zoyipa.
3 Når jeg ser din Himmel, dine Fingres Værk, Månen og Stjernerne, som du skabte,
Pamene ndilingalira za mayiko anu akumwamba, ntchito ya zala zanu, mwezi ndi nyenyezi, zimene mwaziyika pa malo ake,
4 hvad er da et Menneske, at du kommer ham i Hu, et Menneskebarn, at du tager dig af ham?
munthu ndani kuti Inu mumamukumbukira, ndi mwana wa munthu kuti inu mumacheza naye?
5 Du gjorde ham lidet ringere end Gud. med Ære og Herlighed kroned du ham;
Inu munamupanga kukhala wocheperapo kusiyana ndi zolengedwa zakumwamba ndipo mwamuveka ulemerero ndi ulemu.
6 du satte ham over dine Hænders Værk, alt lagde du under hans Fødder,
Inu munamuyika wolamulira ntchito ya manja anu; munayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake;
7 Småkvæg og Okser til Hobe, ja, Markens vilde Dyr,
nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe pamodzi ndi nyama zakuthengo,
8 Himlens Fugle og Havets Fisk, alt, hvad der farer ad Havenes Stier.
mbalame zamlengalenga ndi nsomba zamʼnyanja zonse zimene zimayenda pansi pa nyanja.
9 HERRE, vor Herre, hvor herligt er dit Navn på den vide Jord!
Inu Yehova, Ambuye athu, dzina lanu ndi lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!

< Salme 8 >