< Salme 78 >

1 (En Maskil af Asaf.) Lyt, mit folk til min lære, bøj eders øre til ord fra min Mund;
Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
2 jeg vil åbne min Mund med Billedtale, fremsætte Gåder fra fordums Tid,
Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
3 hvad vi har hørt og ved, hvad vore Fædre har sagt os;
zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
4 vi dølger det ikke for deres Børn, men melder en kommende Slægt om HERRENs Ære og Vælde og Underne, som han har gjort.
Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
5 Han satte et Vidnesbyrd i Jakob, i Israel gav han en Lov, idet han bød vore Fædre at lade deres Børn det vide,
Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
6 at en senere Slægt kunde vide det, og Børn, som fødtes siden, stå frem og fortælle deres Børn derom,
kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
7 så de slår deres Lid til Gud og ikke glemmer Guds Gerninger, men overholder hans Bud,
Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
8 ej slægter Fædrene på, en vanartet, stridig Slægt, hvis Hjerte ikke var fast, hvis Ånd var utro mod Gud
Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
9 - Efraims Børn var rustede Bueskytter, men svigted på Stridens Dag -
Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
10 Gudspagten holdt de ikke, de nægtede at følge hans Lov;
iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
11 hans Gerninger gik dem ad Glemme, de Undere, han lod dem skue.
Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
12 Han gjorde Undere for deres Fædre i Ægypten på Zoans Mark;
Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
13 han kløvede Havet og førte dem over, lod Vandet stå som en Vold;
Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
14 han ledede dem ved Skyen om Dagen, Natten igennem ved Ildens Skær;
Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
15 han kløvede Klipper i Ørkenen, lod dem rigeligt drikke som af Strømme,
Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
16 han lod Bække rinde af Klippen og Vand strømme ned som Floder.
Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
17 Men de blev ved at synde imod ham og vække den Højestes Vrede i Ørkenen;
Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
18 de fristede Gud i Hjertet og krævede Mad til at stille Sulten,
Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
19 de talte mod Gud og sagde: "Kan Gud dække Bord i en Ørken?
Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
20 Se, Klippen slog han, så Vand flød frem, og Bække vælded ud; mon han også kan give Brød og skaffe kød til sit Folk?"
Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
21 Det hørte HERREN, blev vred, der tændtes en Ild mod Jakob, ja Vrede kom op mod Israel,
Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
22 fordi de ikke troede Gud eller stolede på hans Frelse.
pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
23 Da bød han Skyerne oventil, lod Himlens Døre åbne
Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
24 og Manna regne på dem til Føde, han gav dem Himmelkorn;
anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
25 Mennesker spiste Englebrød, han sendte dem Mad at mætte sig med.
Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
26 Han rejste Østenvinden på Himlen, førte Søndenvinden frem ved sin Kraft;
Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
27 Kød lod han regne på dem som Støv og vingede Fugle som Havets Sand,
Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
28 lod dem falde midt i sin Lejr, rundt omkring sine Boliger;
Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
29 Og de spiste sig overmætte, hvad de ønskede, lod han dem få.
Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
30 Men før deres Attrå var stillet, mens Maden var i deres Mund,
Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
31 rejste Guds Vrede sig mod dem; han vog deres kraftige Mænd, fældede Israels Ynglinge.
mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
32 Og dog blev de ved at synde og troede ej på hans Undere.
Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
33 Da lod han deres Dage svinde i Tomhed og endte brat deres År.
Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
34 Når han vog dem, søgte de ham, vendte om og spurgte om Gud,
Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
35 kom i Hu, at Gud var deres Klippe, Gud den Allerhøjeste deres Genløser.
Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
36 De hyklede for ham med Munden, løj for ham med deres Tunge;
Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
37 deres Hjerter holdt ikke fast ved ham, hans Pagt var de ikke tro.
Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
38 Og dog er han barmhjertig, han tilgiver Misgerning, lægger ej øde, hans Vrede lagde sig Gang på Gang, han lod ikke sin Harme fuldt bryde frem;
Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
39 han kom i Hu, de var Kød, et Pust, der svinder og ej vender tilbage.
Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
40 Hvor tit stod de ham ikke imod i Ørkenen og voldte ham Sorg i det øde Land!
Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
41 De fristede alter Gud, de krænkede Israels Hellige;
Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
42 hans Hånd kom de ikke i Hu, de Dag han friede dem fra Fjenden,
Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
43 da han gjorde sine Tegn i Ægypten, sine Undere på Zoans Mark,
tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
44 forvandlede deres Floder til Blod, så de ej kunde drikke af Strømmene,
Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
45 sendte Myg imod dem, som åd dem, og Frøer, som lagde dem øde,
Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
46 gav Æderen, hvad de avlede, Græshoppen al deres Høst,
Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
47 slog deres Vinstokke ned med Hagl, deres Morbærtræer med Frost,
Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
48 prisgav Kvæget for Hagl og deres Hjorde for Lyn.
Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
49 Han sendte sin Vredesglød mod dem, Harme, Vrede og Trængsel, en Sendefærd af Ulykkesengle;
Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
50 frit Løb gav han sin Vrede, skånede dem ikke for Døden, gav deres Liv til Pris for Pest;
Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
51 alt førstefødt i Ægypten slog han, Mandskraftens Førstegrøde i Kamiternes Telte,
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
52 lod sit Folk bryde op som en Hjord, ledede dem som Kvæg i Ørkenen,
Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
53 ledede dem trygt, uden Frygt, mens Havet lukked sig over deres Fjender;
Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
54 han bragte dem til sit hellige Land, de Bjerge, hans højre vandt,
Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
55 drev Folkeslag bort foran dem, udskiftede ved Lod deres Land og lod Israels Stammer bo i deres Telte.
Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
56 Dog fristed og trodsede de Gud den Allerhøjeste og overholdt ikke hans Vidnesbyrd;
Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
57 de faldt fra, var troløse som deres Fædre, svigtede som en slappet Bue,
Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
58 de krænkede ham med deres Offerhøje, æggede ham med deres Gudebilleder.
Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
59 Det hørte Gud og blev vred følte højlig Lede ved Israel;
Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
60 han opgav sin Bolig i Silo, det Telt, hvor han boede blandt Mennesker;
Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
61 han gav sin Stolthed i Fangenskab, sin Herlighed i Fjendehånd,
Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
62 prisgav sit Folk for Sværdet, blev vred på sin Arvelod;
Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
63 Ild fortærede dets unge Mænd, dets Jomfruer fik ej Bryllupssange,
Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
64 dets Præster faldt for Sværdet, dets Enker holdt ikke Klagefest.
ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
65 Da vågnede Herren som en, der har sovet, som en Helt, der er døvet af Vin;
Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
66 han slog sine Fjender på Ryggen, gjorde dem evigt til Skamme.
Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
67 Men han fik Lede ved Josefs Telt, Efraims Stamme udvalgte han ikke;
Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
68 han udvalgte Judas Stamme, Zions Bjerg, som han elsker;
Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
69 han byggede sit Tempel himmelhøjt, grundfæstede det evigt som Jorden.
Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
70 Han udvalgte David, sin Tjener, og tog ham fra Fårenes Folde,
Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
71 hentede ham fra de diende Dyr til at vogte Jakob, hans Folk, Israel, hans Arvelod;
kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
72 han vogtede dem med oprigtigt Hjerte, ledede dem med kyndig Hånd.
Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.

< Salme 78 >