< Salme 77 >
1 (Til Sangmesteren. Til Jedutun. Af Asaf. En Salme.) Jeg råber, højt til Gud, og han hører mig,
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Asafu. Ndinafuwulira Mulungu kupempha thandizo; ndinafuwula mokweza kwa Mulungu kuti anditcherere khutu.
2 jeg søger Herren på Nødens Dag, min Hånd er om Natten utrættet udrakt, min Sjæl vil ikke lade sig trøste;
Pamene ndinali pa masautso ndinafunafuna Ambuye; usiku ndinatambasula manja mosalekeza ndipo moyo wanga unakana kutonthozedwa.
3 jeg ihukommer Gud og stønner, jeg sukker, min Ånd vansmægter. (Sela)
Ndinakumbukira Inu Mulungu, ndipo ndinabuwula; ndinasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unalefuka. (Sela)
4 Du holder mine Øjne vågne, jeg er urolig og målløs.
Munagwira zikope zanga kuti ndisagone ndipo ndinavutika kwambiri kuti ndiyankhule.
5 Jeg tænker på fordums dage, ihukommer længst henrundne År;
Ndinaganizira za masiku akale, zaka zamakedzana;
6 jeg gransker om Natten i Hjertet, grunder og ransager min Ånd.
Ndinakumbukira nyimbo zanga usiku. Mtima wanga unasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unafunsa kuti,
7 Vil Herren bortstøde for evigt og aldrig mer vise Nåde,
“Kodi Ambuye adzatikana mpaka muyaya? Kodi Iwo sadzaonetsanso kukoma mtima kwawo?
8 er hans Miskundhed ude for stedse, hans Trofasthed omme for evigt og altid,
Kodi Chikondi chake chosatha chija chatheratu? Kodi malonjezo ake alephera nthawi yonse?
9 har Gud da glemt at ynkes, lukket sit Hjerte i Vrede? (Sela)
Kodi Mulungu wayiwala kukhala wokoma mtima? Kodi mu mkwiyo wake waleka chifundo chake?”
10 Jeg sagde: Det er min Smerte; at den Højestes højre er ikke som før.
Ndipo ndinaganiza, “Pa izi ine ndidzapemphanso: zaka za dzanja lamanja la Wammwambamwamba.
11 Jeg kommer HERRENs Gerninger i Hu, ja kommer dine fordums Undere i Hu.
Ine ndidzakumbukira ntchito za Yehova; Ine ndidzakumbukira zodabwitsa zanu za kalekale.
12 Jeg tænker på al din Gerning og grunder over dine Værker.
Ndidzakumbukira ntchito zanu ndi kulingalira zodabwitsa zanu.”
13 Gud, din Vej var i Hellighed, hvo er en Gud så stor som Gud!
Njira zanu Mulungu ndi zoyera. Kodi ndi mulungu uti ali wamkulu kuposa Mulungu wathu?
14 Du er en Gud, som gør Undere, du gjorde din Vælde kendt blandt Folkene,
Inu ndinu Mulungu wochita zodabwitsa; Mumaonetsera mphamvu yanu pakati pa mitundu ya anthu.
15 udøste dit Folk med din Arm, Jakobs og Josefs Sønner. (Sela)
Ndi dzanja lanu lamphamvu munawombola anthu anu, zidzukulu za Yakobo ndi Yosefe. (Sela)
16 Vandene så dig, Gud, Vandene så dig og vred sig i Angst, ja Dybet tog til at skælve;
Madzi anakuonani Mulungu, madzi anakuonani ndipo anachita mantha; nyanja yozama inakomoka.
17 Skyerne udøste Vand, Skyhimlens Stemme gjaldede, dine Pile for hid og did;
Mitambo inakhuthula madzi ake pansi, mu mlengalenga munamveka mabingu; mivi yanu inawuluka uku ndi uku.
18 din bragende Torden rullede, Lynene oplyste Jorderig, Jorden bæved og skjalv;
Bingu lanu linamveka mʼmphepo ya kamvuluvulu, mphenzi yanu inawalitsa dziko lonse; dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.
19 din Vej gik midt gennem Havet, din Sti gennem store Vande, dine Fodspor kendtes ikke.
Njira yanu inadutsa pa nyanja, njira yanu inadutsa pa madzi amphamvu, ngakhale zidindo za mapazi anu sizinaoneke.
20 Du førte dit Folk som en Hjord ved Moses's og Arons Hånd.
Inu munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa mwa dzanja la Mose ndi Aaroni.