< Salme 61 >

1 (Til sangmesteren. Til strengespil. Af David.) Hør, o Gud, på mit råb og lyt til min bøn!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Loyimbidwa ndi zipangizo za zingwe. Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu; mvetserani pemphero langa.
2 Fra Jordens Ende råber jeg til dig. Når mit Hjerte vansmægter, løft mig da op på en Klippe,
Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka; tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo.
3 led mig, thi du er min Tilflugt, et mægtigt Tårn til Værn imod Fjenden.
Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga, nsanja yolimba polimbana ndi adani anga.
4 Lad mig evigt bo som Gæst i dit Telt, finde Tilflugt i dine Vingers Skjul! (Sela)
Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu.
5 Ja du, o Gud, har hørt mine Løfter, opfyldt deres Ønsker, der frygter dit Navn.
Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga; mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu.
6 Til Kongens Dage lægger du Dage, hans År skal være fra Slægt til Slægt.
Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu, zaka zake kwa mibado yochuluka.
7 Han skal trone evigt for Guds Åsyn; send Nåde og Sandhed til at bevare ham!
Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya; ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze.
8 Da vil jeg evigt love dit Navn og således Dag efter Dag indfri mine Løfter.
Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.

< Salme 61 >