< Salme 60 >

1 (Til sangmesteren. Al-sjusjan-edut. En miktam af David til til indøvelse, dengang han kæmpede med Aram-Naharajim og Aram-Zoba, og Joab vendte tilbage og slog edomitterne i Saltdalen, 12000 mand.) Gud, du har stødt os fra dig, nedbrudt os, du vredes - vend dig til os igen;
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere. Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza. Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
2 du lod Landet skælve, slå Revner, læg nu dets Brist, thi det vakler!
Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba, konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
3 Du lod dit Folk friste ondt, iskænked os døvende Vin.
Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto; inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
4 Dem, der frygter dig, gav du et Banner, hvorhen de kan fly for Buen. (Sela)
Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera kuti tisonkhanireko pothawa uta.
5 Til Frelse for dine elskede hjælp med din højre, bønhør os!
Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja, kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
6 Gud talede i sin Helligdom: "Jeg vil udskifte Sikem med jubel, udmåle Sukkots Dal;
Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwakupambana ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
7 mit er Gilead, mit er Manasse, Efraim er mit Hoveds Værn, Juda min Herskerstav,
Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
8 Moab min Vaskeskål, på Edom kaster jeg min Sko, over Filisterland jubler jeg."
Mowabu ndi mbale yanga yosambira, pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga, pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
9 Hvo bringer mig hen til den faste Stad, hvo leder mig hen til Edom?
Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
10 Har du ikke, Gud, stødt os fra dig? Du ledsager ej vore Hære.
Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
11 Giv os dog Hjælp mod Fjenden! Blændværk er Menneskers Støtte.
Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu, pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
12 Med Gud skal vi øve vældige Ting, vore Fjender træder han ned!
Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano ndipo tidzapondaponda adani athu.

< Salme 60 >